< Çölde Sayim 34 >

1 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “İsrailliler'e de ki, ‘Mülk olarak size düşecek Kenan ülkesine girince, sınırlarınız şöyle olacak:
“Lamula Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pamene mulowa mʼdziko la Kanaani, dziko lomwe lidzaperekedwa kwa inu ngati cholowa chanu, lidzakhale ndi malire awa:
3 “‘Güney sınırınız Zin Çölü'nden Edom sınırı boyunca uzanacak. Doğuda, güney sınırınız Lut Gölü'nün ucundan başlayacak,
“‘Chigawo cha kummwera kwa dziko lanu chidzayambira ku chipululu cha Zini motsatana ndi malire a Edomu. Kummawa malire anu a kummwera adzayambira kummawa, kumathero a Nyanja ya Mchere.
4 Akrep Geçidi'nin güneyinden Zin'e geçip Kadeş-Barnea'nın güneyine dek uzanacak. Oradan Hasar-Addar'a ve Asmon'a,
Malirewo adzapita kummwera ndipo adzakwera phiri la Akirabimu mpaka ku Zini. Mathero ake adzakhala kummwera kwa Kadesi-Baranea. Ndipo adzapitenso ku Hazari Adari mpaka kukafika ku Azimoni,
5 oradan da Mısır Vadisi'ne uzanarak Akdeniz'de son bulacak.
kumene malirewo adzakhote kuchokera ku Azimoni mpaka ku khwawa la ku Igupto ndi kukathera ku Nyanja Yayikulu.
6 “‘Batı sınırınız Akdeniz ve kıyısı olacak. Batıda sınırınız bu olacak.
“‘Malire anu a ku madzulo adzakhala ku gombe la Nyanja Yayikulu. Amenewo ndiwo adzakhale malire anu a ku madzulo.
7 “‘Kuzey sınırınız Akdeniz'den Hor Dağı'na dek uzanacak.
“‘Malire anu a kumpoto, mzere wake uyambire ku Nyanja Yayikulu mpaka ku phiri la Hori
8 Hor Dağı'ndan Levo-Hamat'a, oradan Sedat'a,
ndi kuchokera ku phiri la Hori mpaka ku Lebo Hamati. Malirewa apite ku Zedadi,
9 Zifron'a doğru uzanarak Hasar-Enan'da son bulacak. Kuzeyde sınırınız bu olacak.
ndi kupitirira mpaka ku Ziforoni ndi kukathera ku Hazari-Enani. Awa ndiwo adzakhale malire anu a kumpoto.
10 “‘Doğu sınırınız Hasar-Enan'dan Şefam'a dek uzanacak.
“‘Za malire anu a kummawa, mulembe mzere kuchokera ku Hazari-Enani mpaka kukafika ku Sefamu.
11 Sınırınız Şefam'dan Ayin'in doğusundaki Rivla'ya dek inecek. Oradan Kinneret Gölü'nün doğu kıyısındaki yamaçlara dek uzanacak.
Malirewo adzatsikire ku Sefamu mpaka ku Ribila cha kummawa kwa Aini ndi kupitirira mpaka ku matsitso a cha kummawa kwa Nyanja ya Kinereti.
12 Oradan Şeria Irmağı boyunca uzanacak ve Lut Gölü'nde son bulacak. “‘Her yandan ülkenizin sınırları bu olacaktır.’”
Tsono malirewo adzatsika motsatana ndi Yorodani ndi kukathera ku Nyanja ya Mchere. “‘Limeneli lidzakhala dziko lanu ndi malire ake mbali zonse.’”
13 Musa İsrailliler'e, “Miras olarak kurayla paylaştıracağınız ülke budur” dedi, “RAB'bin buyruğu uyarınca ülke dokuz oymakla bir yarım oymak arasında paylaştırılacak.
Ndipo Mose analamula Aisraeli kuti, “Limeneli ndi dziko limene mudzalilandira pochita maere kuti likhale cholowa chanu. Yehova analamula kuti liperekedwe ku mafuko asanu ndi anayi ndi theka,
14 Çünkü Ruben oymağına bağlı ailelerle Gad oymağına bağlı aileler ve Manaşşe oymağının öbür yarısı mülklerini aldılar.
chifukwa mabanja a fuko la Rubeni, fuko la Gadi, ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo.
15 Bu iki oymakla yarım oymak mülklerini Eriha'nın karşısındaki Şeria Irmağı'nın doğusunda aldılar.”
Mafuko awiriwa pamodzi ndi theka la fuko la Manase analandiriratu cholowa chawo patsidya pa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko cha kummawa kotulukira dzuwa.”
16 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anawuza Mose kuti,
17 “Ülkeyi mülk olarak aranızda paylaştıracak adamlar şunlardır: Kâhin Elazar ve Nun oğlu Yeşu.
“Awa ndi mayina a anthu amene adzakugawireni dzikoli kuti likhale cholowa chanu: wansembe Eliezara ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Ülkeyi mülk olarak paylaştırmaları için her oymaktan birer önder görevlendirin.
Musankhe mtsogoleri mmodzi kuchokera ku fuko lililonse kuti athandize kugawa dzikolo.
19 Şu adamları görevlendireceksiniz: “Yahuda oymağından Yefunne oğlu Kalev,
Mayina awo ndi awa: Kalebe mwana wa Yefune, wochokera ku fuko la Yuda,
20 Şimon oymağından Ammihut oğlu Şemuel,
Semueli mwana wa Amihudi, wochokera ku fuko la Simeoni;
21 Benyamin oymağından Kislon oğlu Elidat,
Elidadi mwana wa Kisiloni, wochokera ku fuko la Benjamini;
22 Dan oymağından Yogli oğlu önder Bukki,
Buki mwana wa Yogili, mtsogoleri wochokera ku fuko la Dani;
23 Yusufoğulları'ndan: Manaşşe oymağından Efot oğlu önder Hanniel,
Hanieli mwana wa Efodi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Manase, mwana wa Yosefe;
24 Efrayim oymağından Şiftan oğlu önder Kemuel,
Kemueli mwana wa Sifitani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Efereimu, mwana wa Yosefe.
25 Zevulun oymağından Parnak oğlu önder Elisafan,
Elizafani mwana wa Parinaki, mtsogoleri wochokera ku fuko la Zebuloni;
26 İssakar oymağından Azzan oğlu önder Paltiel,
Palitieli mwana wa Azani, mtsogoleri wochokera ku fuko la Isakara,
27 Aşer oymağından Şelomi oğlu önder Ahihut,
Ahihudi mwana wa Selomi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Aseri;
28 Naftali oymağından Ammihut oğlu önder Pedahel.”
Pedaheli mwana wa Amihudi, mtsogoleri wochokera ku fuko la Nafutali.”
29 Kenan ülkesinde İsrailliler'e mülkü paylaştırmaları için RAB'bin görevlendirdiği adamlar bunlardı.
Awa ndiwo mayina a anthu amene Yehova analamula kuti agawe cholowa cha Aisraeli mʼdziko la Kanaani.

< Çölde Sayim 34 >