< Çölde Sayim 16 >

1 Levi oğlu Kehat oğlu Yishar oğlu Korah, Ruben soyundan Eliavoğulları'ndan Datan, Aviram ve Pelet oğlu On toplulukça seçilen, tanınmış iki yüz elli İsrailli önderle birlikte Musa'ya başkaldırdı.
Kora mwana wa Izihari, mwana wa Kohati, mwana wa Levi ndi Datani ndi Abiramu ana a Eliabu, pamodzi ndi Oni mwana wa Perezi, ana a Rubeni, anayamba kudzikuza,
2
ndipo anawukira Mose. Mʼgulu mwawo munali atsogoleri a Aisraeli 250, anthu otchuka amene anasankhidwa ndi anthu pa msonkhano.
3 Hep birlikte Musa'yla Harun'un yanına varıp, “Çok ileri gittiniz!” dediler, “Bütün topluluk, topluluğun her bireyi kutsaldır ve RAB onların arasındadır. Öyleyse neden kendinizi RAB'bin topluluğundan üstün görüyorsunuz?”
Iwo anasonkhana kudzatsutsana ndi Mose ndi Aaroni nawawuza kuti, “Mwawonjeza! Anthu onsewa ndi oyera, aliyense wa iwo, ndipo Yehova ali pakati pawo. Chifukwa chiyani mukudzikuza pakati pa gulu lonse la Yehova?”
4 Bunu duyan Musa yüzüstü yere kapandı.
Mose atamva izi, anagwa chafufumimba.
5 Sonra Korah'la yandaşlarına şöyle dedi: “Sabah RAB kimin kendisine ait olduğunu, kimin kutsal olduğunu açıklayacak ve o kişiyi huzuruna çağıracak. RAB seçeceği kişiyi huzuruna çağıracak.
Ndipo iye anawuza Kora ndi anthu onse amene ankamutsatira kuti, “Yehova mawa mmawa adzasonyeza yemwe ndi wake ndiponso amene ndi woyera mtima. Munthuyo adzabwera pafupi ndi Iye. Munthu amene adzamusankheyo adzamusendeza pafupi.
6 Ey Korah ve yandaşları, kendinize buhurdanlar alın.
Iwe Kora pamodzi ndi onse amene akukutsatira chitani izi: Tengani zofukizira
7 Yarın RAB'bin huzurunda buhurdanlarınızın içine ateş, ateşin üstüne de buhur koyun. RAB'bin seçeceği kişi, kutsal olan kişidir. Ey Levililer, çok ileri gittiniz!”
ndipo mawa muyikemo moto ndi lubani pamaso pa Yehova. Munthu amene Yehova amusankhe ndiye amene ali woyera. Alevi inu mwawonjeza kwambiri!”
8 Musa Korah'la konuşmasını şöyle sürdürdü: “Ey Levililer, beni dinleyin!
Mose anawuzanso Kora kuti, “Inu Alevi, tsopano tamverani!
9 İsrail'in Tanrısı sizi kendi huzuruna çıkarmak için ayırdı. RAB'bin Konutu'nun hizmetini yapmanız, topluluğun önünde durmanız, onlara hizmet etmeniz için sizi İsrail topluluğunun arasından seçti. Sizi ve bütün Levili kardeşlerinizi huzuruna çıkardı. Bu yetmiyormuş gibi kâhinliği de mi istiyorsunuz?
Kodi sizinakukwanireni kuti Mulungu wa Israeli anakupatulani pakati pa gulu lonse la Aisraeli ndi kukubweretsani pafupi ndi Iye, kuti muzigwira ntchito ku nyumba ya Yehova ndi kumayima pamaso pa gulu, kumatumikira?
Wakubweretsa iwe pamodzi ndi Alevi anzako kufupi ndi Iye mwini. Koma tsopano ukufuna kutenganso unsembe.
11 Ey Korah, senin ve yandaşlarının böyle toplanması RAB'be karşı gelmektir. Harun kim ki, ona dil uzatıyorsunuz?”
Nʼkulakwira Yehova kuti iwe ndi gulu lako lonseli mwasonkhana kuti mutsutsane ndi Yehova. Kodi Aaroni ndani kuti muzikangana naye?”
12 Sonra Musa Eliavoğulları Datan'la Aviram'ı çağırttı. Ama onlar, “Gelmeyeceğiz” dediler,
Kenaka Mose anayitana Datani ndi Abiramu, ana aamuna a Eliabu koma iwo anati, “Sitibwera!
13 “Bizi çölde öldürtmek için süt ve bal akan ülkeden çıkardın. Bu yetmiyormuş gibi başımıza geçmek istiyorsun.
Kodi sikukwanira kuti unatitulutsa, kutichotsa mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kuti udzatiphe mʼchipululu muno? Kodi tsopano ukufunanso kutilemetsa?
14 Bizi süt ve bal akan ülkeye götürmediğin gibi mülk olarak bize tarlalar, bağlar da vermedin. Bu adamları kör mü sanıyorsun? Hayır, gelmeyeceğiz.”
Kuwonjezera apo, sunatilowetse mʼdziko loyenda mkaka ndi uchi kapena kutipatsa malo wolima ndi minda ya mpesa. Kodi ukufuna kuchotsa maso a anthuwa? Ayi, sitibwera!”
15 Çok öfkelenen Musa RAB'be, “Onların sunularını önemseme. Onlardan bir eşek bile almadım, üstelik hiçbirine de haksızlık etmedim” dedi.
Pamenepo Mose anakwiya kwambiri ndipo anati kwa Yehova, “Musalandire chopereka chawo. Sindinatenge kalikonse kwa iwo ngakhale bulu, ndiponso sindinalakwire wina aliyense wa iwo.”
16 Sonra Korah'a, “Yarın sen ve bütün yandaşların –sen de, onlar da– RAB'bin önünde bulunmak için gelin” dedi, “Harun da gelsin.
Mose anati kwa Kora, “Iwe ndi okutsatira onse mudzaonekere pamaso pa Yehova mawa, iweyo ndi iwowo pamodzi ndi Aaroni.
17 Herkes kendi buhurdanını alıp içine buhur koysun. İki yüz elli kişi birer buhurdan alıp RAB'bin önüne getirsin. Harun'la sen de buhurdanlarınızı getirin.”
Munthu aliyense akatenge chofukizira ndi kuyikamo lubani, zofukizira 250 zonse pamodzi ndi kuzibweretsa pamaso pa Yehova. Iwe ndi Aaroni mudzabweretsenso zofukizira zanu.”
18 Böylece herkes buhurdanını alıp içine ateş, ateşin üstüne de buhur koydu. Sonra Musa ve Harun'la birlikte Buluşma Çadırı'nın giriş bölümünde durdular.
Choncho munthu aliyense anatenga chofukizira chake nayikamo moto ndi lubani, ndipo anayima pamodzi ndi Mose ndi Aaroni pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 Korah bütün topluluğu Musa'yla Harun'un karşısında Buluşma Çadırı'nın giriş bölümünde toplayınca, RAB'bin görkemi bütün topluluğa göründü.
Kora atasonkhanitsa omutsatira ake onse amene amatsutsa nawo pa khomo la tenti ya msonkhano, ulemerero wa Yehova unaonekera kwa gulu lonselo.
20 RAB, Musa'yla Harun'a, “Bu topluluğun arasından ayrılın da onları bir anda yok edeyim” dedi.
Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti,
“Chokani pakati pa gulu ili kuti ndithetse mkanganowu kamodzinʼkamodzi.”
22 Musa'yla Harun yüzüstü yere kapanarak, “Ey Tanrı, bütün insan ruhlarının Tanrısı!” dediler, “Bir kişi günah işledi diye bütün topluluğa mı öfkeleneceksin?”
Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa chafufumimba ndipo analira mokweza, “Chonde Mulungu, Mulungu wa mizimu ya anthu onse, kodi mudzakwiyira gulu lonse pamene munthu mmodzi yekha ndiye amene wachimwa?”
23 RAB Musa'ya, “Topluluğa söyle, Korah'ın, Datan'ın, Aviram'ın çadırlarından uzaklaşsınlar” dedi.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti,
“Uza gulu lonse kuti, ‘Khalani kutali ndi matenti a Kora, Datani ndi Abiramu.’”
25 Musa Datan'la Aviram'a gitti. İsrail'in ileri gelenleri onu izledi.
Mose anayimirira napita kwa Datani, Abiramu ndi kwa akuluakulu a Israeli amene ankamutsatira.
26 Topluluğu uyararak, “Bu kötü adamların çadırlarından uzak durun!” dedi, “Onların hiçbir şeyine dokunmayın. Yoksa onların günahları yüzünden canınızdan olursunuz.”
Anachenjeza gulu lonse kuti, “Khalani kutali ndi matenti a anthu oyipawa! Musakhudze kanthu kawo kalikonse, mukatero mudzawonongedwa limodzi nawo chifukwa cha machimo awo.”
27 Bunun üzerine topluluk Korah, Datan ve Aviram'ın çadırlarından uzaklaştı. Datan'la Aviram çıkıp karıları, küçük büyük çocuklarıyla birlikte çadırlarının önünde durdular.
Choncho anthuwo anachokadi ku matenti a Kora, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali atatuluka nayima pamodzi ndi akazi awo, ana awo ndi makanda awo pa makomo a matenti awo.
28 Musa şöyle dedi: “Bütün bunları yapmam için RAB'bin beni gönderdiğini, kendiliğimden bir şey yapmadığımı şuradan anlayacaksınız:
Tsono Mose anati, “Umu ndi mmene mudzadziwire kuti Yehova ndiye amene anandituma kuti ndichite zinthu zonsezi ndipo kuti si maganizo anga.
29 Eğer bu adamlar herkes gibi doğal bir ölümle ölür, herkesin başına gelen bir olayla karşılaşırlarsa, bilin ki beni RAB göndermemiştir.
Ngati anthu awa afa ndi imfa ya chilengedwe ndi kuwachitikira zomwe zimachitikira munthu aliyense, ndiye kuti Yehova sananditume.
30 Ama RAB yepyeni bir olay yaratırsa, yer yarılıp onları ve onlara ait olan her şeyi yutarsa, ölüler diyarına diri diri inerlerse, bu adamların RAB'be saygısızlık ettiklerini anlayacaksınız.” (Sheol h7585)
Koma Yehova akachita china chake chachilendo, nthaka nitsekula pakamwa pake ndi kuwameza iwo pamodzi ndi zonse zimene ali nazo, iwowa nʼkulowa mʼmanda ali moyo, pamenepo mudzazindikira kuti anthu amenewa ananyoza Yehova.” (Sheol h7585)
31 Musa konuşmasını bitirir bitirmez Korah, Datan ve Aviram'ın altındaki yer yarıldı.
Atangotsiriza kuyankhula zimenezi, nthaka ya pamene anayimapo inagawikana
32 Yer yarıldı, onları, ailelerini, Korah'ın adamlarıyla mallarını yuttu.
ndipo dziko linatsekula pakamwa pake ndi kuwameza pamodzi ndi nyumba zawo ndi anthu onse a Kora ndi katundu wawo yense.
33 Sahip oldukları her şeyle birlikte diri diri ölüler diyarına indiler. Yer onların üzerine kapandı. Topluluğun arasından yok oldular. (Sheol h7585)
Analowa mʼmanda amoyo pamodzi ndi zonse zimene anali nazo. Nthaka inawatsekera ndi kuwawononga ndipo sanaonekenso. (Sheol h7585)
34 Çığlıklarını duyan çevredeki İsrailliler, “Yer bizi de yutmasın!” diyerek kaçıştılar.
Atamva kulira kwawo, Aisraeli onse amene anali pafupi ndi anthuwo anathawa akufuwula kuti, “Nthaka imezanso ife!”
35 RAB'bin gönderdiği ateş buhur sunan iki yüz elli adamı yakıp yok etti.
Ndipo moto wochokera kwa Yehova unabwera nʼkunyeketsa anthu 250 amene ankapereka nsembe yofukiza aja.
36 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anawuza Mose kuti,
37 “Kâhin Harun oğlu Elazar'a buhurdanları ateşin içinden çıkarmasını, ateş korlarını az öteye dağıtmasını söyle. Çünkü buhurdanlar kutsaldır.
“Uza Eliezara mwana wa Aaroni, wansembe kuti atenge zofukizirazo pakati pa mitembo yopsererayo ndipo amwazire makalawo kutali chifukwa zofukizirazo nʼzopatulika.
38 İşledikleri günahtan ötürü öldürülen bu adamların buhurdanlarını levha haline getirip sunağı bunlarla kapla. Buhurdanlar RAB'be sunuldukları için kutsaldır. Bunlar İsrailliler için bir uyarı olsun.”
Izi ndi zofukizira za anthu omwe anafa chifukwa cha uchimo wawo. Musule zofukizirazo kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe, chifukwa zinaperekedwa kwa Yehova ndipo ndi zopatulika. Zimenezi zikhale chizindikiro kwa Aisraeli.”
39 Böylece Kâhin Elazar, yanarak ölen adamların getirdiği tunç buhurdanları RAB'bin Musa aracılığıyla kendisine söylediği gibi alıp döverek sunağı kaplamak için levha haline getirdi. Bu, İsrailliler'e Harun'un soyundan gelenlerden başka hiç kimsenin RAB'bin önüne çıkıp buhur yakmaması gerektiğini anımsatacaktı. Yoksa o kişi Korah'la yandaşları gibi yok olacaktı.
Choncho Eliezara, wansembe, anasonkhanitsa zofukizira zamkuwa zija zomwe anthu opsererawo anabwera nazo ndipo anazisula kuti zikhale zophimbira pa guwa lansembe,
monga momwe Yehova anamulangizira kudzera mwa Mose. Chimenechi chinali chikumbutso kwa Aisraeli kuti munthu wina aliyense, kupatula zidzukulu za Aaroni, sayenera kupsereza lubani pamaso pa Yehova, kuopa kuti munthu woteroyo angakhale ngati Kora ndi omutsatira ake.
41 Ertesi gün bütün İsrail topluluğu Musa'yla Harun'a söylenmeye başladı. “RAB'bin halkını siz öldürdünüz” diyorlardı.
Tsiku lotsatira, gulu lonse la Aisraeli linatsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Iwo anati, “Inu mwapha anthu a Yehova.”
42 Topluluk Musa'yla Harun'a karşı toplanıp Buluşma Çadırı'na doğru yönelince, çadırı ansızın bulut kapladı ve RAB'bin görkemi göründü.
Koma pamene anthuwo anasonkhana kuti atsutsane ndi Mose ndi Aaroni, atatembenuka kuyangʼana ku tenti ya msonkhano, mwadzidzidzi mtambo unaphimba tentiyo ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
43 Musa'yla Harun Buluşma Çadırı'nın önüne geldiler.
Pamenepo Mose ndi Aaroni anapita patsogolo pa tenti ya msonkhano ija
44 RAB Musa'ya, “Bu topluluğun arasından ayrılın da onları birden yok edeyim” dedi. Musa'yla Harun yüzüstü yere kapandılar.
ndipo Yehova anawuza Mose kuti,
“Chokani pakati pa gulu la anthuwa kuti ndiwawononge kamodzinʼkamodzi.” Ndipo iwo anagwa pansi chafufumimba.
46 Sonra Musa Harun'a, “Buhurdanını alıp içine sunaktan ateş koy, üstüne de buhur koy” dedi, “Günahlarını bağışlatmak için hemen topluluğa git. Çünkü RAB öfkesini yağdırdı. Öldürücü hastalık başladı.”
Kenaka Mose anawuza Aaroni kuti, “Tenga chofukizira chako ndipo ikamo lubani pamodzi ndi moto wochokera pa guwa lansembe, fulumira, pita pa gulu la anthuwo ndipo ukachite nsembe yopepesera machimo awo popeza mkwiyo wa Yehova wafika, mliri wayamba.”
47 Harun Musa'nın dediğini yaparak buhurdanını alıp topluluğun ortasına koştu. Halkın arasında öldürücü hastalık başlamıştı. Harun buhur sunarak topluluğun günahını bağışlattı.
Ndipo Aaroni anachita monga ananenera Mose, nathamangira mʼkatikati mwa gulu la anthuwo. Pamenepo nʼkuti mliri utayamba kale pakati pa anthu aja ndipo Aaroni anafukiza lubani ndi kupereka nsembe yopepesera machimo awo.
48 O ölülerle dirilerin arasında durunca, öldürücü hastalık da dindi.
Iye anayimirira pakati pa anthu amoyo ndi akufa ndipo mliri unaleka.
49 Korah olayında ölenler dışında, öldürücü hastalıktan ölenlerin sayısı 14 700 kişiydi.
Komabe anthu 14, 700 anafa ndi mliriwo, kuwonjezera pa aja amene anafa chifukwa cha Kora.
50 Öldürücü hastalık dindiğinden, Harun Musa'nın yanına, Buluşma Çadırı'nın giriş bölümüne döndü.
Ndipo Aaroni anabwerera kwa Mose ku khomo la tenti ya msonkhano, chifukwa mliriwo unali utatha.

< Çölde Sayim 16 >