< Çölde Sayim 10 >

1 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 “Dövme gümüşten iki borazan yapacaksın; bunları topluluğu çağırmak ve halkın yola çıkması için kullanacaksın.
“Sula malipenga awiri a siliva, ndipo uziwagwiritsa ntchito posonkhanitsa anthu pamodzi ndiponso powasamutsa mʼmisasa.
3 İki borazan birden çalınınca, bütün topluluk senin yanında, Buluşma Çadırı'nın girişi önünde toplanacak.
Pamene akuliza malipenga onse awiri, anthu onse asonkhane kwa iwe pa khomo la tenti ya msonkhano.
4 Yalnız biri çalınırsa, önderler, İsrail'in oymak başları senin yanında toplanacak.
Akaliza limodzi lokha, atsogoleri, akulu a mafuko a Aisraeli, asonkhane kwa iwe.
5 Borazan kısa çalınınca, doğuda konaklayanlar yola çıkacak.
Akaliza lipenga lochenjeza, misasa yomwe ili kummawa iyambe kusamuka.
6 İkinci kez kısa çalınınca da güneyde konaklayanlar yola çıkacak. Borazanın kısa çalınması oymakların yola çıkması için bir işarettir.
Akaliza lipenga lochenjeza lachiwiri, misasa yakummwera iyambe kusamuka. Kuliza kwa lipenga lochenjeza kudzakhala chizindikiro choyamba ulendo.
7 Topluluğu toplamak için de borazan çaldırt, ama kısa olmasın.
Pofuna kusonkhanitsa anthu, muziliza malipenga, koma mosiyana ndi mmene malipenga ochenjeza amalizidwira.
8 “Borazanları kâhin olan Harunoğulları çalacak. Borazan çalınması sizler ve gelecek kuşaklar için kalıcı bir kural olacak.
“Ana a Aaroni, ansembe aja, ndiwo aziliza malipengawo. Zimenezi zikhale zokhazikika kwa inu ndi ku mibado yanu yonse.
9 Sizi sıkıştıran düşmana karşı ülkenizde savaşa çıktığınızda, borazan çalın. O zaman Tanrınız RAB sizi anımsayacak, sizi düşmanlarınızdan kurtaracak.
Pamene mukupita ku nkhondo mʼdziko lanu lomwe, kulimbana ndi mdani amene akukuzunzani, muziliza malipenga ochenjeza ndipo Yehova Mulungu wanu adzakukumbukirani ndi kukulanditsani mʼmanja mwa adani anu.
10 Sevinçli olduğunuz günler –kutladığınız bayramlar ve Yeni Ay Törenleri'nde– yakmalık sunular ve esenlik kurbanları üzerine borazan çalacaksınız. Böylelikle Tanrınız'ın önünde anımsanmış olacaksınız. Ben Tanrınız RAB'bim.”
Komanso pa nthawi yanu ya chisangalalo, pa maphwando anu oyikika ndi maphwando a mwezi watsopano, muziliza malipenga pa nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zanu za chiyanjano, ndipo zidzakhala chikumbutso chanu pamaso pa Mulungu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.”
11 İkinci yılın ikinci ayının yirminci günü bulut Levha Sandığı'nın bulunduğu konutun üzerinden kalktı.
Pa chaka chachiwiri, mwezi wachiwiri, tsiku la 20, mtambo unachoka pamwamba pa chihema cha umboni.
12 İsrailliler de Sina Çölü'nden göç etmeye başladılar. Bulut Paran Çölü'nde durdu.
Ndipo Aisraeli ananyamuka kuchoka mʼchipululu cha Sinai ndipo anayenda malo osiyanasiyana mpaka pamene mtambo unayima mʼchipululu cha Parani.
13 Bu, RAB'bin Musa aracılığıyla verdiği buyruk uyarınca ilk göç edişleriydi.
Kameneka kanali koyamba kuti Aisraeli anyamuke monga momwe Yehova analamulira Mose.
14 Önce Yahuda sancağı bölükleriyle yola çıktı. Yahuda bölüğüne Amminadav oğlu Nahşon komuta ediyordu.
Magulu a msasa wa Yuda ndiwo anayamba kunyamuka potsata mbendera yawo. Mtsogoleri wa gulu lawo anali Naasoni mwana wa Aminadabu.
15 İssakar oymağının bölüğüne Suar oğlu Netanel,
Mtsogoleri wa gulu la fuko la Isakara anali Netanieli mwana wa Zuwara,
16 Zevulun oymağının bölüğüne de Helon oğlu Eliav komuta ediyordu.
Eliabu mwana wa Heloni ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Zebuloni.
17 Konut yere indirilince, onu taşıyan Gerşonoğulları'yla Merarioğulları yola koyuldular.
Kenaka anagwetsa chihema, ndipo Ageresoni ndi Amerari amene ananyamula chihemacho, ananyamuka.
18 Sonra Ruben sancağı bölükleriyle yola çıktı. Ruben bölüğüne Şedeur oğlu Elisur komuta ediyordu.
Kenaka magulu a msasa wa fuko la Rubeni ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Elizuri mwana wa Sedeuri.
19 Şimon oymağının bölüğüne Surişadday oğlu Şelumiel,
Mtsogoleri wa fuko la Simeoni anali Selumieli mwana wa Zurisadai,
20 Gad oymağının bölüğüne de Deuel oğlu Elyasaf komuta ediyordu.
ndipo Eliyasafu mwana wa Deuweli ndiye ankatsogolera fuko la Gadi.
21 Kehatlılar kutsal eşyaları taşıyarak yola koyuldular. Bunlar varmadan konut kurulmuş olurdu.
Kenaka Akohati ananyamuka atanyamula zinthu zopatulika. Chihema chinkayenera kuyimikidwa iwo asanafike.
22 Efrayim sancağı bölükleriyle yola çıktı. Efrayim bölüğüne Ammihut oğlu Elişama komuta ediyordu.
Magulu a msasa wa Aefereimu anatsatira potsatira mbendera yawo. Elisama mwana wa Amihudi ndiye anali mtsogoleri wawo.
23 Manaşşe oymağının bölüğüne Pedahsur oğlu Gamliel,
Gamalieli mwana wa Pedazuri ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Manase.
24 Benyamin oymağının bölüğüne de Gidoni oğlu Avidan komuta ediyordu.
Abidani mwana wa Gideoni ndiye anali mtsogoleri wa mtundu wa Benjamini.
25 En sonunda Dan sancağı ordunun artçı kolu olan bölükleriyle yola çıktı. Dan bölüğüne Ammişadday oğlu Ahiezer komuta ediyordu.
Pambuyo pa magulu onse panali magulu a msasa wa Dani, omwe ankateteza magulu onsewa ndipo ananyamuka potsatira mbendera yawo. Mtsogoleri wawo anali Ahiyezeri mwana wa Amisadai.
26 Aşer oymağının bölüğüne Okran oğlu Pagiel,
Pagieli mwana wa Okirani ndiye anali mtsogoleri wa fuko la Aseri,
27 Naftali oymağının bölüğüne de Enan oğlu Ahira komuta ediyordu.
ndipo mtsogoleri wa mtundu wa Nafutali anali Ahira mwana wa Enani.
28 Yola koyulduklarında İsrailli bölüklerin yürüyüş düzeni böyleydi.
Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.
29 Musa, kayınbabası Midyanlı Reuel oğlu Hovav'a, “RAB'bin, ‘Size vereceğim’ dediği yere gidiyoruz” dedi, “Bizimle gel, sana iyi davranırız. Çünkü RAB İsrail'e iyilik edeceğine söz verdi.”
Ndipo Mose anawuza Hobabu mwana wa Reueli Mmidiyani, mpongozi wa Mose kuti, “Tikunyamuka kupita ku malo amene Yehova anati, ‘Ndidzakupatsani.’ Tiye upite nafe ndipo tidzakusamalira bwino, pakuti Yehova analonjeza zinthu zabwino kwa Israeli.”
30 Hovav, “Gelmem” diye yanıtladı, “Ülkeme, akrabalarımın yanına döneceğim.”
Hobabu anayankha kuti, “Ayi, sindipita nanu, ndibwerera ku dziko la kwathu ndi kwa abale anga.”
31 Musa, “Lütfen bizi bırakma” diye üsteledi, “Çünkü çölde konaklayacağımız yerleri sen biliyorsun. Sen bize göz olabilirsin.
Ndipo Mose anati, “Pepa usatisiye popeza ukudziwa kumene tingamange misasa mʼchipululu muno ndipo udzakhala maso athu.
32 Bizimle gelirsen, RAB'bin yapacağı bütün iyilikleri seninle paylaşırız.”
Iweyo ukapita nafe, tidzagawana nawe zinthu zabwino zomwe Yehova adzatipatsa.”
33 RAB'bin Dağı'ndan ayrılıp üç günlük yol aldılar. Konaklayacakları yeri bulmaları için RAB'bin Antlaşma Sandığı üç gün boyunca önleri sıra gitti.
Motero ananyamuka ku Phiri la Yehova nayenda ulendo wa masiku atatu. Bokosi la Chipangano cha Yehova linkayenda patsogolo pawo pa masiku atatuwo kuti apeze malo woti apumulepo.
34 Konakladıkları yerden ayrıldıklarında da RAB'bin bulutu gündüzün onların üzerinde duruyordu.
Mtambo wa Yehova unkawaphimba masana pamene ankasamuka pa misasa yawo.
35 Sandık yola çıkınca Musa, “Ya RAB, kalk! Düşmanların dağılsın, Senden nefret edenler önünden kaçsın!” diyordu.
Nthawi iliyonse imene Bokosi la Chipangano likunyamuka, Mose ankanena kuti, “Dzukani, Inu Yehova! Adani anu abalalike; Odana nanu athawe pamaso panu.
36 Sandık konaklayınca da, “Ya RAB, binlerce, on binlerce İsrailli'ye dön!” diyordu.
“Pamene likupumula, ankanena kuti, “Bwererani, Inu Yehova, ku chinamtindi cha Aisraeli.”

< Çölde Sayim 10 >