< Nehemya 8 >
1 İsrailliler kentlerine yerleştikten sonra, yedinci ay tek vücut halinde Su Kapısı'nın karşısındaki alanda toplandılar. Bilgin Ezra'ya RAB'bin Musa aracılığıyla İsrail halkına verdiği buyrukları içeren Yasa Kitabı'nı getirmesini söylediler.
Anthu onse anasonkhana ngati munthu mmodzi pabwalo limene lili patsogolo pa Chipata cha Madzi. Iwo anawuza mlembi Ezara kuti abwere ndi buku la malamulo a Mose limene Yehova anapereka kwa Aisraeli.
2 Yedinci ayın birinci günü Kâhin Ezra Yasa Kitabı'nı halkın toplandığı yere getirdi. Dinleyip anlayabilecek kadın erkek herkes oradaydı.
Choncho pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri wansembe Ezara, anabwera ndi buku la malamulo ku msonkhano wa amuna, akazi ndi ana onse amene ankatha kumvetsa zinthu bwino.
3 Ezra Su Kapısı'nın karşısındaki alanda kadınların, erkeklerin ve anlayabilecek yaştaki çocukların önünde, sabahtan öğlene kadar Yasa Kitabı'nı okudu. Herkes dikkatle dinledi.
Choncho Ezara anawerenga bukulo atayangʼana bwalo la Chipata cha Madzi kuyambira mmawa mpaka masana pamaso pa amuna, akazi ndi onse amene ankamvetsa bwino zinthu. Ndipo anthu onse anatchera khutu kuti amve malamulowo.
4 Bilgin Ezra toplantı için hazırlanmış ahşap bir zemin üzerinde duruyordu. Sağında Mattitya, Şema, Anaya, Uriya, Hilkiya ve Maaseya vardı. Solunda ise Pedaya, Mişael, Malkiya, Haşum, Haşbaddana, Zekeriya ve Meşullam duruyordu.
Mlembi Ezara anayimirira pa nsanja ya mitengo imene anthu anamanga chifukwa cha msonkhanowu. Ku dzanja lake lamanja kunayimirira Matitiya, Sema, Anaya, Uriya, Hilikiya ndi Maaseya, ndipo kudzanja lake lamanzere kunali Pedaya, Misaeli, Malikiya, Hasumu, Hasibadana, Zekariya ndi Mesulamu.
5 Ezra halkın gözü önünde kitabı açtı. Halktan daha yüksek bir yerde duruyordu. Kitabı açar açmaz herkes ayağa kalktı.
Tsono Ezara anatsekula buku, akuona popeza anayima pa nsanja. Pamene anafutukula bukulo anthu onse anayimirira.
6 Ezra yüce Tanrı'ya, RAB'be övgüler sundu. Bütün halk ellerini kaldırarak, “Amin! Amin!” diye karşılık verdi. Hep birlikte eğilip yere kapanarak RAB'be tapındılar.
Ezara anatamanda Yehova, Mulungu wamkulu, ndipo anthu onse anakweza manja awo ndi kuyankha kuti, “Ameni, ameni.” Pambuyo pake onse anaweramitsa pansi mitu yawo napembedza Yehova akanali chizolikire choncho.
7 Levililer'den Yeşu, Bani, Şerevya, Yamin, Akkuv, Şabbetay, Hodiya, Maaseya, Kelita, Azarya, Yozavat, Hanan ve Pelaya ayakta duran halka yasayı anlattılar.
Anthuwo atayimiriranso Alevi awa: Yesuwa, Bani, Serebiya, Yamini, Akubu, Sabetayi, Hodiya, Maaseya, Kerita, Azariya, Yozabadi, Hanani ndi Pelaya anawathandiza kuti amvetse bwino malamulowo.
8 Tanrı'nın Yasa Kitabı'nı okuyup açıkladılar, herkesin anlamasını sağlayacak biçimde yorumladılar.
Iwo anawerenga buku la malamulo a Mulungu momveka bwino ndi kutanthauzira mawuwo kuti anthu amvetse bwino zowerengedwazo.
9 Vali Nehemya, Kâhin ve Bilgin Ezra ve halka öğretmenlik yapan Levililer, “Bugün Tanrınız RAB için kutsal bir gündür. Yas tutup ağlamayın” dediler. Çünkü bütün halk Kutsal Yasa'yı dinlerken ağlıyordu.
Tsono bwanamkubwa Nehemiya pamodzi ndi wansembe ndi mlembi Ezara komanso Alevi amene amaphunzitsa anthu anati kwa anthu onse, “Lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova Mulungu wanu. Musakhale ndi chisoni ndipo musalire.” Anayankhula choncho popeza anthu onse ankalira atamva mawu a buku la malamulo lija.
10 Nehemya da, “Gidin, yağlı yiyip tatlı için” dedi, “Hazırlığı olmayanlara da bir pay gönderin. Çünkü bugün Rabbimiz için kutsal bir gündür. Üzülmeyin. RAB'bin verdiği sevinç sizi güçlü kılar.”
Nehemiya anatinso, “Pitani, kachiteni phwando ku nyumba ndipo mukawagawireko ena amene alibe kanthu kalikonse popeza lero ndi tsiku lopatulika kwa Yehova. Musakhale ndi chisoni, pakuti chimwemwe cha Yehova ndiye mphamvu yanu.”
11 Levililer, “Sakin olun, bugün kutsal bir gündür, üzülmeyin” diyerek halkı yatıştırdılar.
Alevi anakhalitsa bata anthu onse powawuza kuti, “Khalani chete, pakuti lero ndi tsiku lopatulika ndipo musakhale ndi chisoni.”
12 Böylece herkes yiyip içmek, yiyeceklerini başkalarıyla paylaşmak ve büyük şenlik yapmak üzere evinin yolunu tuttu. Çünkü kendilerine okunanları anlamışlardı.
Anthu onse anachoka kupita kukadya ndi kumwa. Chakudya china anatumiza kwa anzawo. Choncho panali chikondwerero chachikulu popeza tsopano anali atamvetsa bwino mawu a Mulungu amene anawawerengera ndi kuwafotokozerawo.
13 Ertesi gün bütün aile başları, kâhinler ve Levililer Kutsal Yasa'nın buyruklarını öğrenmek için Bilgin Ezra'nın çevresine toplandılar.
Mmawa mwake atsogoleri a mabanja pamodzi ndi ansembe ndi alevi anasonkhana kwa Ezara, mlembi wa malamulo kuti aphunzire mawu a malamulowo.
14 Yasada RAB'bin Musa aracılığıyla verdiği şu buyruğu buldular: Yedinci ayda kutlanan bayramda İsrailliler çardaklarda oturmalı.
Tsono anapeza kuti zinalembedwa mʼbuku la malamulo kuti Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti Aisraeli azikhala mʼzithando pa nthawi yonse ya chikondwerero cha mwezi wachisanu ndi chiwiri.
15 Bütün kentlerde ve Yeruşalim'de şu duyuru yapılsın: “Dağlara çıkın; yasada yazılana uygun olarak, çardak yapmak üzere zeytin, iğde, mersin ve hurma dalları, sık yapraklı ağaç dalları getirin.”
Choncho analengeza ndi kufalitsa mʼmizinda yawo yonse ndi mu Yerusalemu kuti, “Pitani ku phiri mukadule nthambi za mtengo wa olivi, za mtengo wa olivi wa kutchire, za mtengo wa mchisu, za mtengo wa mgwalangwa ndiponso za mitengo ina ya masamba, zomangira zithando monga zalembedweramu ndi kubwera nazo.”
16 Böylece halk dalları getirip damlarında, evlerinin ve Tanrı Tapınağı'nın avlularında, Su Kapısı ve Efrayim Kapısı alanlarında çardaklar yaptı.
Choncho anthu anapita kukatenga nthambi ndipo aliyense anadzimangira misasa pa denga ya nyumba yake, mʼmabwalo awo, mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu, mʼbwalo la pa Chipata cha Madzi ndiponso mʼbwalo la pa Chipata cha Efereimu.
17 Sürgünden dönen herkes yaptığı çardakta oturdu. İsrailliler Nun oğlu Yeşu'nun döneminden beri böyle bir kutlama yapmamışlardı. Herkes büyük sevinç içindeydi.
Gulu lonse la anthu limene linabwera ku ukapolo linamanga misasa ndipo linakhala mʼmenemo. Kuyambira nthawi ya Yoswa mwana wa Nuni mpaka tsiku limenelo nʼkuti Aisraeli asanachitepo zimenezi. Choncho panali chimwemwe chachikulu.
18 Ezra ilk günden son güne kadar, her gün Tanrı'nın Yasa Kitabı'nı okudu. Yedi gün bayram yaptılar. Sekizinci gün kural uyarınca kutsal toplantı yapıldı.
Tsiku ndi tsiku, kuyambira tsiku loyamba mpaka lomaliza, Ezara ankawerenga buku la malamulo a Mulungu. Anthu anachita chikondwerero masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachisanu ndi chitatu panachitika msonkhano potsata buku la malamulo lija.