< Mika 6 >
1 RAB'bin söylediğine kulak verin: Kalkın, davanızı dağların önünde dile getirin. Tepeler duysun sesinizi.
Tamverani zimene Yehova akunena: “Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri; zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.
2 Ey dağlar ve yeryüzünün sarsılmaz temelleri, RAB'bin suçlamasını dinleyin. Çünkü RAB halkından davacı, İsrail'den şikâyetçi.
Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri; tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi. Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake; Iye akutsutsa Aisraeli.
3 “Ey halkım, sana ne yaptım?” diyor RAB, “Sana nasıl yük oldum, yanıtla.
“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani? Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.
4 Seni Mısır'dan ben çıkardım, Ben kurtardım seni kölelik diyarından. Sana öncülük etsinler diye Musa'yı, Harun'u, Miryam'ı ben gönderdim.
Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo. Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni, pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.
5 Ey halkım, Moav Kralı Balak'ın neler öğütlediğini, Beor oğlu Balam'ın onu nasıl yanıtladığını anımsa. Şittim'den Gilgal'a dek olup biteni an. Sizleri nasıl kurtardığımı o zaman anlayacaksın.”
Anthu anga, kumbukirani zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha. Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala, kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”
6 RAB'bin önüne ne ile çıkayım, Yüce Tanrı'ya nasıl tapınayım? O'nun önüne yakmalık sunuyla mı, Bir yaşında danayla mı çıkayım?
Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba? Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza, ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?
7 Binlerce koç sunsam, Zeytinyağından on binlerce dere akıtsam, RAB hoşnut kalır mı? Suçuma karşılık ilk oğlumu, İşlediğim günah için bedenimin ürününü versem olur mu?
Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000, kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta? Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga? Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?
8 Ey insanlar, RAB iyi olanı size bildirdi; Adil davranmanızdan, sadakati sevmenizden Ve alçakgönüllülükle yolunda yürümenizden başka Tanrınız RAB sizden ne istedi?
Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino. Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe? Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.
9 Dinleyin! RAB kente sesleniyor. O'nun adından korkmak bilgeliktir. Diyor ki, “Ey halk ve kent meclisi, dinleyin.
Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda ndi nzeru kuopa dzina lanu. “Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.
10 Kötü adamların evleri Haksızca kazanılmış servetlerle dolu, Bilmiyor muyum sanıyorsunuz? Eksik ölçek lanetlidir.
Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo, ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?
11 Hileli terazi kullanan, Torbasında eksik ağırlıklar olan adamı nasıl aklayayım?
Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo, ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?
12 Kentin zenginleri zorba, Halkı da yalancıdır. Dillerinden aldatıcı sözler dökülür.
Anthu ake olemera amachita zachiwawa; anthu ake ndi abodza ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.
13 Günahlarınızdan ötürü yıkımınızı, Mahvınızı hazırladım bile.
Choncho, ndayamba kukuwonongani, kukusakazani chifukwa cha machimo anu.
14 Yiyecek, ama doymayacaksınız. Aç kalacak karnınız, Biriktireceksiniz, ama saklayamayacaksınız. Koruyabildiğinizi kılıçla yok edeceğim.
Mudzadya, koma simudzakhuta; mudzakhalabe ndi njala. Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika, chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.
15 Ekecek, ama biçemeyeceksiniz. Zeytin ezecek, ama yağını sürünemeyeceksiniz. Üzümü sıkacak, ama şarabını içemeyeceksiniz.
Mudzadzala, koma simudzakolola. Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito. Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.
16 Kral Omri'nin buyruklarına, Ahav soyunun kötü adetlerine uyduğunuz, Onların törelerini izlediğiniz için sizi utanca boğacağım, yıkıma uğratacağım. Halkım olarak aşağılanmaya dayanmak zorunda kalacaksınız.”
Inu mwatsatira malangizo a Omuri ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu, ndi khalidwe lawo lonse. Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu; mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”