< Matta 11 >
1 İsa, on iki öğrencisine bu buyrukları verdikten sonra onların kentlerinde öğretmek ve Tanrı sözünü duyurmak üzere oradan ayrıldı.
Ndipo Yesu atamaliza kulangiza ophunzira ake khumi ndi awiri aja, anachoka kumeneko kupita kukaphunzitsa ndi kukalalikira ku mizinda ya ku Galileya.
2 Tutukevinde bulunan Yahya, Mesih'in yaptığı işleri duyunca, O'na gönderdiği öğrencileri aracılığıyla şunu sordu: “Gelecek Olan sen misin, yoksa başkasını mı bekleyelim?”
Yohane ali mʼndende anamva zimene Khristu ankachita, ndipo anatumiza ophunzira ake kukamufunsa Iye.
Anamufunsa kuti, “Kodi Inu ndinu uja ankanena kuti mudzabwerayu kapena tidikire wina?”
4 İsa onlara şöyle karşılık verdi: “Gidin, işitip gördüklerinizi Yahya'ya bildirin.
Yesu anayankha kuti, “Bwererani ndi kukamuwuza Yohane zimene mwamva ndi kuona.
5 Körlerin gözleri açılıyor, kötürümler yürüyor, cüzamlılar temiz kılınıyor, sağırlar işitiyor, ölüler diriliyor ve Müjde yoksullara duyuruluyor.
Osaona akuona, olumala akuyenda, akhate akuchiritsidwa, osamva akumva, akufa akuukitsidwa ndipo Uthenga Wabwino ukulalikidwa kwa osauka.
6 Benden ötürü sendeleyip düşmeyene ne mutlu!”
Odala ndi munthu amene sakhumudwa chifukwa cha Ine.”
7 Yahya'nın öğrencileri ayrılırken İsa halka Yahya'dan söz etmeye başladı. “Çöle ne görmeye gittiniz?” dedi. “Rüzgarda sallanan bir kamış mı?
Pamene ophunzira a Yohane ankachoka, Yesu anayamba kuyankhula kwa gulu la anthu za Yohane kuti, “Kodi munkapita ku chipululu kuti mukaone chiyani? Kodi bango logwedezeka ndi mphepo?
8 Söyleyin, ne görmeye gittiniz? Pahalı giysiler giymiş bir adam mı? Oysa pahalı giysi giyenler, kral saraylarında bulunur.
Nanga munkapita kukaona chiyani, munthu wovala zokongola? Ayi, wovala zokongola amakhala mʼnyumba za mafumu.
9 Öyleyse ne görmeye gittiniz? Bir peygamber mi? Evet! Size şunu söyleyeyim, gördüğünüz kişi peygamberden de üstündür.
Nanga munkapita kukaona chiyani? Mneneri kodi? Inde ndikuwuzani kuti munkakaona woposa mneneri.
10 ‘İşte, habercimi senin önünden gönderiyorum; O önden gidip senin yolunu hazırlayacak’ diye yazılmış olan sözler onunla ilgilidir.
Uyu ndi amene malemba akunena za iye kuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga patsogolo panu amene adzakonza njira yanu.
11 Size doğrusunu söyleyeyim, kadından doğanlar arasında Vaftizci Yahya'dan daha üstün biri çıkmamıştır. Bununla birlikte, Göklerin Egemenliği'nde en küçük olan ondan üstündür.
Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pakati pa obadwa ndi mkazi sipanaoneke wina aliyense wamkulu woposa Yohane Mʼbatizi; komatu amene ndi wamngʼono kwambiri mu ufumu wakumwamba ndi wamkulu koposa iye.
12 Vaftizci Yahya'nın ortaya çıktığı günden bu yana Göklerin Egemenliği zorlanıyor, zorlu kişiler onu ele geçirmeye çalışıyor.
Kuyambira masiku a Yohane Mʼbatizi mpaka tsopano, ufumu wakumwamba ndi wolimbirana ndipo anthu amphamvu okha ndi amene akuwulanda.
13 Yahya'ya dek bütün peygamberlerle Kutsal Yasa, olacakları önceden bildirdiler.
Pakuti aneneri onse ndi malamulo ananenera kufikira nthawi ya Yohane.
14 Eğer bunu kabul etmek isterseniz, gelecek olan İlyas odur.
Ndipo ngati inu mufuna kulandira izi, iyeyu ndi Eliya amene ankanena kuti adzabwera uja.
Iye amene ali ndi makutu amve.
16 “Bu kuşağın insanlarını neye benzeteyim? Çarşı meydanlarında oturup arkadaşlarına, ‘Size kaval çaldık, oynamadınız; Ağıt yaktık, dövünmediniz’ diye seslenen çocuklara benziyorlar.
“Kodi mʼbado uwu ndingawufanizire ndi chiyani? Uli ngati ana opezeka mʼmisika amene akuyitana anzawo nʼkumati:
“‘Tinakuyimbirani zitoliro, koma inu simunavine; ife tinayimba nyimbo zamaliro, koma inu simunalire.’
18 Yahya geldiği zaman oruç tutup içkiden kaçındı, ona ‘cinli’ diyorlar.
Pakuti Yohane sanabwerere kudya kapena kumwa koma iwo ankanena kuti, ‘Iye anali ndi chiwanda.’
19 İnsanoğlu geldiği zaman yiyip içti. Bu kez de diyorlar ki, ‘Şu obur ve ayyaş adama bakın! Vergi görevlileri ve günahkârlarla dost oldu!’ Ne var ki bilgelik, ortaya koyduğu işlerle doğrulanır.”
Mwana wa Munthu anabwera ndi kumadya ndi kumwa koma iwo akuti, ‘Munthu wadyera, woledzera, bwenzi la amisonkho ndi bwenzi la ochimwa.’ Koma nzeru imatsimikizika kuti ndi yolondola mwa ntchito zake.”
20 Sonra İsa, mucizelerinin çoğunu yapmış olduğu kentleri, tövbe etmedikleri için şöyle azarlamaya başladı: “Vay haline, ey Horazin! Vay haline, ey Beytsayda! Sizlerde yapılan mucizeler Sur ve Sayda'da yapılmış olsaydı, çoktan çul kuşanıp kül içinde oturarak tövbe etmiş olurlardı.
Pamenepo Yesu anayamba kudzudzula mizinda imene zodabwitsa zake zambiri zinachitikamo, chifukwa chakuti sinatembenuke mtima.
“Tsoka kwa iwe Korazini! Tsoka kwa iwe Betisaida! Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe zikanachitidwa mu Turo ndi Sidoni, iwo akanalapa kale atavala ziguduli ndi kudzola phulusa.
22 Size şunu söyleyeyim, yargı günü sizin haliniz Sur ve Sayda'nın halinden beter olacaktır!
Koma ndikuwuzani inu kuti pa tsiku lachiweruzo mlandu wa Turo ndi Sidoni udzachepako kusiyana ndi wanu.
23 Ya sen, ey Kefarnahum, göğe mi çıkarılacaksın? Hayır, ölüler diyarına indirileceksin! Çünkü sende yapılan mucizeler Sodom'da yapılmış olsaydı, bugüne dek ayakta kalırdı. (Hadēs )
Ndipo iwe Kaperenawo, kodi udzakwezedwa kufika kumwamba? Ayi, udzatsitsidwa mpaka pansi kufika ku Hade. Ngati zodabwitsa zimene zinachitika mwa iwe, zikanachitika mu Sodomu, bwenzi iye alipo kufikira lero. (Hadēs )
24 Sana şunu söyleyeyim, yargı günü senin halin Sodom bölgesinin halinden beter olacaktır!”
Koma Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku la chiweruziro mlandu wa Sodomu udzachepako kusiyana ndi wanu.”
25 İsa bundan sonra şöyle dedi: “Baba, yerin ve göğün Rabbi! Bu gerçekleri bilge ve akıllı kişilerden gizleyip küçük çocuklara açtığın için sana şükrederim.
Pa nthawi imeneyo Yesu anati, “Ine ndikukuyamikani Inu Atate Ambuye akumwamba ndi dziko lapansi, chifukwa Inu mwawabisira zinthu izi anzeru ndi ophunzira ndi kuziwulula kwa ana angʼonoangʼono.
26 Evet Baba, senin isteğin buydu.
Inde, Atate, ichi chinali chokukomerani Inu.
27 “Babam her şeyi bana teslim etti. Oğul'u, Baba'dan başka kimse tanımaz. Baba'yı da Oğul'dan ve Oğul'un O'nu tanıtmak istediği kişilerden başkası tanımaz.
“Zinthu zonse zapatsidwa kwa Ine ndi Atate anga. Palibe mmodzi amene adziwa Mwana kupatula Atate ndipo palibe mmodzi amene adziwa Atate kupatula Mwana ndi kwa iwo amene Mwana awasankha kuwawululira.
28 “Ey bütün yorgunlar ve yükü ağır olanlar! Bana gelin, ben size rahat veririm.
“Idzani kwa Ine, inu nonse otopa ndi olemedwa ndipo Ine ndidzakupatsani mpumulo.
29 Boyunduruğumu yüklenin, benden öğrenin. Çünkü ben yumuşak huylu, alçakgönüllüyüm. Böylece canlarınız rahata kavuşur.
Senzani goli langa ndipo phunzirani kwa Ine, pakuti ndine wofatsa ndi wodzichepetsa. Ndipo inu mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.
30 Boyunduruğumu taşımak kolay, yüküm hafiftir.”
Pakuti goli langa ndi losavuta ndipo katundu wanga ndi wopepuka.”