< Malaki 3 >
1 “İşte habercimi gönderiyorum. Önümde yolu hazırlayacak. Aradığınız Rab ansızın tapınağına gelecek; görmeyi özlediğiniz antlaşma habercisi gelecek” diyor Her Şeye Egemen RAB.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”
2 Ama onun geleceği güne kim dayanabilir? O belirince kim durabilir? Çünkü o maden arıtıcının ateşi, çamaşırcının kül suyu gibi olacak;
Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa.
3 gümüş eritip arıtan gibi davranacak: Levililer'i arındırıp altın, gümüş temizler gibi temizleyecek. Böylece RAB'be doğrulukla sunular sunacaklar.
Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo,
4 Geçmiş günlerde, geçmiş yıllarda olduğu gibi, RAB Yahuda ve Yeruşalim'in sunacağı sunulardan hoşnut kalacak.
ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.
5 Her Şeye Egemen RAB, “Yargılamak için size yaklaşacağım” diyor, “Büyücülere, zina edenlere, yalan yere ant içenlere, işçinin, dulun, öksüzün, yabancının hakkını çiğneyenlere –benden korkmayanlara– karşı hemen tanık olacağım.”
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”
6 “Ben RAB'bim, değişmem. Siz bunun için yok olmadınız, ey Yakup soyu!
“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe.
7 Atalarınızın günlerinden bu yana kurallarımı çiğnediniz, onlara uymadınız. Bana dönün, ben de size dönerim” diyor Her Şeye Egemen RAB. “Oysa siz, ‘Nasıl döneriz?’ diye soruyorsunuz.
Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’
8 “İnsan Tanrı'dan çalar mı? Oysa siz benden çalıyorsunuz. “‘Senden nasıl çalıyoruz?’ diye soruyorsunuz. “Ondalıkları, sunuları çalıyorsunuz.
“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera. “Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’ “Pa zakhumi ndi pa zopereka.
9 Siz lanete uğradınız. Çünkü bütün ulus benden çalıyorsunuz.
Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera.
10 Tapınağımda yiyecek bulunması için bütün ondalıklarınızı ambara getirin. Beni bununla sınayın” diyor Her Şeye Egemen RAB. “Göreceksiniz ki, göklerin kapaklarını size açacağım, üzerinize dolup taşan bereket yağdıracağım.
Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo.
11 Çekirgelerin ekinlerinizi yemesini engelleyeceğim. Tarlada asmanız ürünsüz kalmayacak” diyor Her Şeye Egemen RAB.
Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 “Bütün uluslar ne mutlu size diyecekler. Çünkü ülkeniz özlenen bir yer olacak.” Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.
“Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
13 “Bana karşı sert sözler söylediniz” diyor RAB. “Oysa siz, ‘Sana karşı ne söyledik?’ diye soruyorsunuz.
Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine. “Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’
14 “Şunu dediniz: ‘Tanrı'ya kulluk etmek yararsızdır. Her Şeye Egemen RAB'bin isteklerini yerine getirmek, O'nun önünde yas tutar gibi davranmak bize ne kazanç sağlıyor?
“Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse?
15 Şimdi kendini beğenmişlere mutlu diyoruz. Kötülük edenler başarılı oluyor, Tanrı'yı deneyenler cezadan kurtuluyor.’”
Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’”
16 Bunun üzerine RAB'den korkanlar birbirleriyle konuştular. RAB dediklerine kulak verip duydu. RAB'den korkup adını sayanlar için O'nun önünde bir anma kitabı yazıldı.
Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.
17 Her Şeye Egemen RAB, “Öz halkımı ortaya çıkardığım gün, benim olacaklar” diyor, “Bir baba kendisine hizmet eden oğlunu nasıl esirgerse ben de onları öyle esirgeyeceğim.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira.
18 O zaman siz doğru kişiyle kötü kişi, Tanrı'ya kulluk edenle etmeyen arasındaki ayrımı yine göreceksiniz.”
Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”