< Luka 4 >
1 Kutsal Ruh'la dolu olarak Şeria Irmağı'ndan dönen İsa, Ruh'un yönlendirmesiyle çölde dolaştırılarak kırk gün İblis tarafından denendi. O günlerde hiçbir şey yemedi. Dolayısıyla bu süre sonunda acıktı.
Yesu, wodzazidwa ndi Mzimu Woyera, anachoka ku mtsinje wa Yorodani ndipo anatsogozedwa ndi Mzimu Woyerayo kupita ku chipululu,
kumene anayesedwa ndi mdierekezi masiku makumi anayi. Sanadye kena kalikonse pa masiku amenewo, ndipo pa mapeto pake anamva njala.
3 Bunun üzerine İblis O'na, “Tanrı'nın Oğlu'ysan, şu taşa söyle ekmek olsun” dedi.
Mdierekezi anati kwa Iye, “Ngati ndiwe Mwana wa Mulungu, uza mwala uwu kuti usanduke buledi.”
4 İsa, “‘İnsan yalnız ekmekle yaşamaz’ diye yazılmıştır” karşılığını verdi.
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Munthu sadzakhala ndi moyo ndi chakudya chokha.’”
5 Sonra İblis İsa'yı yükseklere çıkararak bir anda O'na dünyanın bütün ülkelerini gösterdi.
Mdierekezi anamutengera Iye pamalo aatali ndipo mʼkamphindi namuonetsa maufumu onse a dziko lapansi.
6 O'na, “Bütün bunların yönetimini ve zenginliğini sana vereceğim” dedi. “Bunlar bana teslim edildi, ben de dilediğim kişiye veririm.
Ndipo anati kwa Iye, “Ndidzakupatsani ulamuliro ndi ulemerero wawo; pakuti anandipatsa ine, ndipo ndingathe kupereka kwa aliyense amene ndikufuna.
7 Bana taparsan, hepsi senin olacak.”
Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
8 İsa ona şu karşılığı verdi: “‘Tanrın Rab'be tapacak, yalnız O'na kulluk edeceksin’ diye yazılmıştır.”
Yesu anayankha kuti, “Zalembedwa: ‘Pembedza Yehova Mulungu wako ndi kumutumikira Iye yekha.’”
9 İblis O'nu Yeruşalim'e götürüp tapınağın tepesine çıkardı. “Tanrı'nın Oğlu'ysan, kendini buradan aşağı at” dedi.
Mdierekezi anapita naye ku Yerusalemu namuyimiritsa pamwamba penipeni pa Nyumba ya Mulungu. Ndipo anati, “Ngati ndinu Mwana wa Mulungu dziponyeni nokha pansi kuchokera pano.
10 “Çünkü şöyle yazılmıştır: ‘Tanrı, seni korumaları için Meleklerine buyruk verecek.’
Pakuti kwalembedwa, “Adzalamulira angelo ake za iwe kuti akutchinjirize mosamala;
11 ‘Ayağın bir taşa çarpmasın diye Seni elleri üzerinde taşıyacaklar.’”
ndipo adzakunyamula ndi manja awo, kuti phazi lako lisagunde pa mwala.”
12 İsa ona şöyle karşılık verdi: “‘Tanrın Rab'bi denemeyeceksin!’ diye buyrulmuştur.”
Yesu anayankha kuti, “Mawu akuti, ‘Musamuyese Yehova Mulungu wanu.’”
13 İblis, İsa'yı her bakımdan denedikten sonra bir süre için O'nun yanından ayrıldı.
Mdierekezi atamaliza mayesero awa onse, anamusiya Iye kufikira atapeza mpata wina.
14 İsa, Ruh'un gücüyle donanmış olarak Celile'ye döndü. Haber bütün bölgeye yayıldı.
Yesu anabwerera ku Galileya mu mphamvu ya Mzimu Woyera, ndipo mbiri yake inafalikira ku madera onse a ku midzi.
15 Oranın havralarında öğretiyor, herkes tarafından övülüyordu.
Iye ankaphunzitsa mʼmasunagoge awo, ndipo aliyense ankamulemekeza.
16 İsa, büyüdüğü Nasıra Kenti'ne geldiğinde her zamanki gibi Şabat Günü havraya gitti. Kutsal Yazılar'ı okumak üzere ayağa kalkınca O'na Peygamber Yeşaya'nın Kitabı verildi. Kitabı açarak şu sözlerin yazılı olduğu yeri buldu:
Iye anapita ku Nazareti, kumene anakulira, ndipo pa tsiku la Sabata anakalowa mʼsunagoge, monga mwa chikhalidwe chake. Ndipo anayimirira kuti awerenge malemba.
Anamupatsa buku la mneneri Yesaya. Atalitsekula, anapeza pamalo pamene panalembedwa kuti,
18 “Rab'bin Ruhu üzerimdedir. Çünkü O beni yoksullara Müjde'yi iletmek için meshetti. Tutsaklara serbest bırakılacaklarını, Körlere gözlerinin açılacağını duyurmak için, Ezilenleri özgürlüğe kavuşturmak Ve Rab'bin lütuf yılını ilan etmek için Beni gönderdi.”
“Mzimu wa Ambuye ali pa Ine; chifukwa wandidzoza kuti ndilalikire Uthenga Wabwino kwa osauka. Wandituma kuti ndilalikire kwa a mʼndende kuti amasulidwe ndi kwa osaona kuti apenyenso, kumasulidwa kwa osautsidwa,
ndi kulalikira za nthawi imene Ambuye adzakomere mtima anthu awo.”
20 Sonra kitabı kapattı, görevliye geri verip oturdu. Havradakilerin hepsi dikkatle O'na bakıyordu.
Kenaka Iye anatseka bukulo, nalibwezera kwa wotumikira ndipo anakakhala pansi. Maso a aliyense mʼsunagogemo anali pa Iye,
21 İsa, “Dinlediğiniz bu Yazı bugün yerine gelmiştir” diye konuşmaya başladı.
ndipo anawawuza kuti, “Lero malemba awa akwaniritsidwa mmene mwamveramu.”
22 Herkes İsa'yı övüyor, ağzından çıkan lütufkâr sözlere hayran kalıyordu. “Yusuf'un oğlu değil mi bu?” diyorlardı.
Onse anayankhula zabwino za Iye ndipo anadabwa ndi mawu ogwira moyo amene anatuluka mʼkamwa mwake. Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu si mwana wa Yosefe?”
23 İsa onlara şöyle dedi: “Kuşkusuz bana şu deyimi hatırlatacaksınız: ‘Ey hekim, önce kendini iyileştir! Kefarnahum'da yaptıklarını duyduk. Aynısını burada, kendi memleketinde de yap.’”
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, mudzandiwuza mwambi uwu: Singʼanga, dzichiritse wekha! Chitanso mʼmudzi wa kwanu kuno zimene ife tamva kuti Iwe unazichita ku Kaperenawo.”
24 “Size doğrusunu söyleyeyim” diye devam etti İsa, “Hiçbir peygamber kendi memleketinde kabul görmez.
Iye anapitiriza kuti, “Zoonadi, ndikukuwuzani kuti palibe mneneri amene amavomerezedwa ku mudzi kwawo.
25 Yine size gerçeği söyleyeyim, gökyüzünün üç yıl altı ay kapalı kaldığı, bütün ülkede korkunç bir kıtlığın baş gösterdiği İlyas zamanında İsrail'de çok sayıda dul kadın vardı.
Ine ndikukutsimikizirani kunali amayi ambiri amasiye mu Israeli mʼnthawi ya Eliya, kumwamba kutatsekedwa kwa zaka zitatu ndi theka ndipo kunali njala yayikulu mʼdziko lonselo.
26 İlyas bunlardan hiçbirine gönderilmedi; yalnız Sayda bölgesinin Sarefat Kenti'nde bulunan dul bir kadına gönderildi.
Komabe Eliya sanatumidwe kwa mmodzi mwa iwo, koma kwa mkazi wamasiye wa ku Zerefati ku chigawo cha Sidoni.
27 Peygamber Elişa'nın zamanında İsrail'de çok sayıda cüzamlı vardı. Bunlardan hiçbiri iyileştirilmedi; yalnız Suriyeli Naaman iyileştirildi.”
Ndipo kunali akhate ambiri ku Israeli mʼnthawi ya mneneri Elisa, koma panalibe mmodzi mwa iwo anachiritsidwa kupatula Naamani wa ku Siriya.”
28 Havradakiler bu sözleri duyunca öfkeden kudurdular.
Anthu onse mʼsunagogemo anapsa mtima atamva izi.
29 Ayağa kalkıp İsa'yı kentin dışına kovdular. O'nu uçurumdan aşağı atmak için kentin kurulduğu tepenin yamacına götürdüler.
Anayimirira namutulutsira kunja kwa mzindawo, ndipo anamutengera pamwamba pa phiri pamene mzindawo unamangidwapo, ndi cholinga chakuti amuponyere ku phompho.
30 Ama İsa onların arasından geçerek oradan uzaklaştı.
Koma Iye anangoyenda pakati pa gulu la anthulo nachokapo.
31 Sonra İsa Celile'nin Kefarnahum Kenti'ne gitti. Şabat Günü halka öğretiyordu.
Kenaka Iye anapita ku Kaperenawo, mudzi wa ku Galileya, ndipo pa Sabata anayamba kuphunzitsa anthu.
32 Yetkiyle konuştuğu için O'nun öğretişine şaşıp kaldılar.
Iwo anadabwa ndi chiphunzitso chake chifukwa uthenga wake unali ndi ulamuliro.
33 Havrada cinli, içinde kötü ruh olan bir adam vardı. Adam yüksek sesle, “Ey Nasıralı İsa, bırak bizi! Bizden ne istiyorsun?” diye bağırdı. “Bizi mahvetmeye mi geldin? Senin kim olduğunu biliyorum, Tanrı'nın Kutsalı'sın sen!”
Mʼsunagogemo munali munthu wogwidwa ndi mzimu woyipa. Iye analira ndi mawu akulu, akuti
“Aa! Kodi mukufuna chiyani kwa ife, Yesu wa ku Nazareti? Kodi mwabwera kudzatiwononga? Ndikudziwa kuti ndinu ndani, ndinu Woyerayo wa Mulungu!”
35 İsa, “Sus, çık adamdan!” diyerek cini azarladı. Cin adamı herkesin önünde yere vurduktan sonra, ona hiç zarar vermeden içinden çıktı.
Yesu anachidzudzula kwambiri nati, “Khala chete! Tuluka mwa iye.” Chiwandacho chinamugwetsa munthuyo pansi pamaso pa onse ndipo chinatuluka wosamupweteka.
36 Herkes şaşkına dönmüştü. Birbirlerine, “Bu nasıl söz? Güç ve yetkiyle kötü ruhlara çıkmalarını buyuruyor, onlar da çıkıyor!” diyorlardı.
Anthu onse anadabwa ndipo anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi chiphunzitso ichi ndi chotani? Ndi ulamuliro ndi mphamvu Iye akulamulira mizimu yoyipa ndipo ikutuluka!”
37 İsa'yla ilgili haber o bölgenin her yanında yankılandı.
Ndipo mbiri yake inafalikira madera onse ozungulira.
38 İsa havradan ayrılarak Simun'un evine gitti. Simun'un kaynanası hastaydı, ateşler içindeydi. Onun için İsa'dan yardım istediler.
Yesu anatuluka mʼsunagoge ndipo anapita kwa Simoni. Tsopano mpongozi wake wa Simoni amadwala malungo akulu, ndipo anamupempha Yesu kuti amuthandize.
39 İsa kadının başucunda durup ateşi azarladı, kadının ateşi düştü. Kadın hemen ayağa kalkıp onlara hizmet etmeye başladı.
Ndipo anawerama nadzudzula malungowo ndipo anamusiya. Anadzuka nthawi yomweyo nayamba kuwatumikira.
40 Güneş batarken herkes çeşitli hastalıklara yakalanmış akrabalarını İsa'ya getirdi. İsa her birinin üzerine ellerini koyarak onları iyileştirdi.
Pamene dzuwa linkalowa, anthu anabweretsa kwa Yesu onse amene anali ndi matenda osiyanasiyana, ndipo atasanjika manja ake pa aliyense, anachiritsidwa.
41 Birçoğunun içinden cinler de, “Sen Tanrı'nın Oğlu'sun!” diye bağırarak çıkıyordu. Ne var ki, İsa onları azarladı, konuşmalarına izin vermedi. Çünkü kendisinin Mesih olduğunu biliyorlardı.
Komanso ziwanda zinkatuluka mwa anthu ambiri, zikufuwula kuti, “Inu ndinu Mwana wa Mulungu!” Koma Iye anazidzudzula ndipo sanazilole kuyankhula chifukwa zimadziwa kuti Iye ndi Khristu.
42 Sabah olunca İsa dışarı çıkıp ıssız bir yere gitti. Halk ise O'nu arıyordu. Bulunduğu yere geldiklerinde O'nu yanlarında alıkoymaya çalıştılar.
Kutacha, Yesu anapita ku malo a yekha. Anthu ankamufunafuna Iye ndipo pamene anafika kumene anali, anthuwo anayesetsa kumuletsa kuti asawachokere.
43 Ama İsa, “Öbür kentlerde de Tanrı'nın Egemenliği'yle ilgili Müjde'yi yaymam gerek” dedi. “Çünkü bunun için gönderildim.”
Koma Iye anati, “Ine ndikuyenera kulalikira Uthenga Wabwino wa ufumu wa Mulungu ku mizinda inanso chifukwa ichi ndi chimene ananditumira.”
44 Böylece Yahudiye'deki havralarda Tanrı sözünü duyurmaya devam etti.
Ndipo Iye anapitirirabe kulalikira mʼmasunagoge a ku Yudeya.