< Levililer 4 >
1 RAB Musa'ya şöyle dedi:
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
2 “İsrail halkına söyle: ‘Biri buyruklarımdan birinde yasakladığım bir şeyi yapar, bilmeden günah işlerse;
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Munthu akachimwa mosadziwa ndi kuchita chilichonse chimene Yehova walamula kuti asachite, azichita izi:
3 meshedilmiş kâhin günah işleyerek halkını da suçlu kılarsa, işlediği günahtan ötürü RAB'be günah sunusu olarak kusursuz bir boğa sunmalı.
“‘Ngati wansembe wodzozedwa achimwa, ndi kuchimwitsa anthu onse, iyeyu ayenera kupereka mwana wangʼombe wamphongo wopanda chilema chifukwa cha tchimo limene wachitalo. Imeneyi ndi nsembe ya Yehova yopepesera tchimo lake.
4 Boğayı Buluşma Çadırı'nın giriş bölümüne, RAB'bin önüne getirip elini onun başına koymalı ve RAB'bin huzurunda onu kesmeli.
Wansembeyo abwere nayo ngʼombeyo pa khomo la tenti ya msonkhano pamaso pa Yehova. Asanjike dzanja lake pamutu pa ngʼombeyo ndipo ayiphe pamaso pa Yehova.
5 Meshedilmiş kâhin boğa kanının birazını Buluşma Çadırı'na götürecek.
Kenaka wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
6 Parmağını kana batırıp En Kutsal Yer'in perdesi önünde, RAB'bin huzurunda yedi kez serpecek.
Iye aviyike chala chake mʼmagazi, ndipo awawaze kasanu ndi kawiri pamaso pa Yehova, patsogolo pa katani yotchinga malo wopatulika.
7 Sonra çadırda, RAB'bin huzurunda, buhur sunağının boynuzlarına sürecek. Boğanın artakalan kanını çadırın giriş bölümündeki yakmalık sunu sunağının dibine dökecek.
Kenaka wansembe apake magaziwo pa nyanga za guwa lofukizira lubani limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza, limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
8 Günah sunusu olarak adanan boğanın bütün yağını alacak. Bağırsak ve işkembe yağlarını,
Pambuyo pake achotse mafuta onse a ngʼombe yayimuna yopepesera machimoyo: mafuta okuta zamʼkati kapena mafuta onse amʼkatimo.
9 böbrekleri, böbrek üstü yağlarını, karaciğerden böbreklere uzanan perdeyi,
Achotsenso ndi kubwera ndi impsyo zonse ziwiri pamodzi ndi mafuta onse ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi ndi impsyo
10 esenlik kurbanı olarak sunulan sığırda olduğu gibi ayıracak. Bunları yakmalık sunu sunağı üzerinde yakacak.
monga momwe amachotsera mafuta a ngʼombe yoperekedwa kuti ikhale chopereka chachiyanjano. Tsono wansembe atenthe zimenezi pa guwa lansembe zopsereza.
11 Boğanın artakalan parçalarını; derisini, etinin tümünü, başını, ayaklarını, işkembesini, bağırsaklarını, gübresini ordugahın dışında küllerin döküldüğü temiz bir yere götürecek; küllerin üzerinde odun ateşiyle yakacak.
Koma chikopa cha ngʼombe yayimunayo ndi mnofu wake wonse, pamodzi ndi mutu ndi miyendo, zamʼkati ndi matumbo,
kapena kuti ngʼombe yonse yotsalayo apite nayo kunja kwa msasa ku malo woyeretsedwa, kumene amatayako phulusa ndi kuyitentha pa nkhuni, pa phulusapo.
13 “‘Eğer bütün İsrail topluluğu bilmeden günah işler, RAB'bin buyruklarından birinde yasaklanmış olanı yaparsa durum gözden kaçsa bile suçlu sayılır.
“‘Ngati gulu lonse la Aisraeli lichimwa mosadziwa, nachita chomwe ndi choletsedwa ndi Yehova, ngakhale kuti gulu lonselo silikudziwa kuti lachimwa, anthuwo ndi olakwa ndithu.
14 İşlediği günah açığa çıkınca, topluluk günah sunusu olarak bir boğa sunmalı, onu Buluşma Çadırı'nın önüne getirmeli.
Akazindikira tchimo limene achita, gulu lonse lipereke mwana wangʼombe wamphongo kuti akhale chopereka chopepesera tchimo ndipo abwere naye pa khomo la tenti ya msonkhano.
15 RAB'bin huzurunda topluluğun ileri gelenleri ellerini boğanın başına koyacak ve boğa RAB'bin huzurunda kesilecek.
Akuluakulu a anthuwo asanjike manja awo pa mutu pa ngʼombe pamaso pa Yehova, ndipo ayiphe pomwepo pamaso pa Yehova.
16 Meshedilmiş kâhin boğanın kanını Buluşma Çadırı'na götürecek.
Tsono wansembe wodzozedwa atengeko magazi a ngʼombeyo ndi kulowa nawo mu tenti ya msonkhano.
17 Parmağını kana batırıp RAB'bin huzurunda, perdenin önünde yedi kez serpecek.
Aviyike chala chake mʼmagaziwo ndi kuwawaza pamaso pa Yehova kasanu ndi kawiri patsogolo pa nsalu yotchinga.
18 Sonra çadırda RAB'bin huzurunda bulunan sunağın boynuzlarına sürecek. Boğanın artakalan kanını çadırın giriş bölümündeki yakmalık sunu sunağının dibine dökecek.
Pambuyo pake iye apake magaziwo pa nyanga za guwa limene lili pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano. Magazi ena otsalawo awathire pa tsinde pa guwa lansembe zopsereza limene lili pa khomo la tenti ya msonkhano.
19 Boğanın bütün yağını alıp sunağın üzerinde yakacak.
Kenaka achotse mafuta onse a ngʼombeyo ndi kuwatentha pa guwa,
20 Günah sunusu olarak sunulan boğaya yaptığının aynısını yapacak. Böylece kâhin halkın günahlarını bağışlatacak ve halk bağışlanacak.
ndipo achite ndi ngʼombe yayimunayi monga anachitira ndi ngʼombe yayimuna yopepesera machimo. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera anthu, ndipo machimo awo adzakhululukidwa.
21 İlk boğayı yaktığı gibi bunu da ordugahın dışına çıkarıp yakacak. Topluluğun günah sunusudur bu.
Kenaka atulutse ngʼombeyo kunja kwa msasa ndi kuyitentha monga anatenthera ngʼombe yoyamba ija. Imeneyi ndiyo nsembe yopepesera machimo a gulu lonse.
22 “‘Önderlerden biri günah işler, bilmeden Tanrısı RAB'bin buyruklarından birinde yasak olanı yaparsa, suçlu sayılır.
“‘Ngati mtsogoleri achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova Mulungu wake, ndiye kuti wapalamula.
23 İşlediği günah kendisine açıklanırsa, sunu olarak kusursuz bir teke getirmeli.
Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, iye abwere ndi mbuzi yayimuna yopanda chilema kuti ikhale chopereka chake.
24 Elini tekenin başına koymalı ve yakmalık sunuların kesildiği yerde RAB'bin huzurunda onu kesmeli. Bu bir günah sunusudur.
Asanjike dzanja lake pa mutu wa mbuziyo ndi kuyiphera pamalo pamene amaphera zopereka zopsereza pamaso pa Yehova. Ichi ndi chopereka chopepesera tchimo.
25 Kâhin günah sunusunun kanına parmağını batırıp yakmalık sunu sunağının boynuzlarına sürecek. Artakalan kanı yakmalık sunu sunağının dibine dökecek.
Pambuyo pake wansembe atengeko magazi a chopereka chopepesera tchimocho ndi chala chake, ndipo awapake pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Athire magazi otsalawo pa tsinde la guwalo.
26 Tekenin bütün yağını esenlik kurbanının yağı gibi sunak üzerinde yakacak. Kâhin kişinin günahını bağışlatacak ve kişi bağışlanacak.
Wansembeyo atenthe mafuta onse pa guwapo monga amatenthera chopereka chachiyanjano. Pochita zimenezi, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo, ndipo adzakhululukidwa.
27 “‘Eğer halktan biri RAB'bin buyruklarından birinde yasak olanı yapar, bilmeden günah işlerse, suçlu sayılır.
“‘Ngati munthu wamba achimwa mosadziwa nachita zimene ndi zoletsedwa ndi Yehova, ndiye kuti wapalamula.
28 İşlediği günah kendisine açıklanırsa, günahından ötürü sunu olarak kusursuz bir dişi keçi getirmeli.
Ndipo ngati wauzidwa za tchimo limene wachita, abweretse mbuzi yayikazi yopanda chilema kuti ikhale chopereka chopepesera tchimo.
29 Elini günah sunusunun başına koymalı ve yakmalık sunuların kesildiği yerde onu kesmeli.
Asanjike dzanja lake pamutu pa mbuziyo ndipo ayiphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
30 Kâhin sununun kanına parmağını batırıp yakmalık sunu sunağının boynuzlarına sürecek. Artakalan kanı sunağın dibine dökecek.
Ndipo wansembe atenge magazi ndi chala chake ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza ndi kuthira magazi wotsalawo pa tsinde la guwalo.
31 Kişi keçinin bütün yağını, esenlik kurbanında olduğu gibi ayıracak. Kâhin RAB'bi hoşnut eden koku olarak onu sunakta yakacak, kişinin günahını bağışlatacak ve kişi bağışlanacak.
Kenaka iye achotse mafuta onse monga momwe anachotsera mafuta a chopereka chachiyanjano, ndipo awatenthe pa guwa kuti akhale fungo lokomera Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo la munthuyo ndipo adzakhululukidwa.
32 “‘Eğer biri günah sunusu olarak bir kuzu getirirse, kuzu dişi ve kusursuz olmalı.
“‘Ngati munthu apereka mwana wankhosa ngati chopereka chopepesera tchimo lake, abwere ndi mwana wankhosa wamkazi wopanda chilema.
33 Elini günah sunusunun başına koyacak ve yakmalık sunuların kesildiği yerde onu günah sunusu olarak kesecek.
Asanjike dzanja lake pa mutu wa mwana wankhosayo ndipo amuphe pamalo pamene amaphera chopereka chopsereza.
34 Kâhin sununun kanına parmağını batırıp yakmalık sunu sunağının boynuzlarına sürecek. Artakalan kanı sunağın dibine dökecek.
Kenaka wansembe atengeko ndi chala chake magazi a mwana wankhosa uja ndi kuwapaka pa nyanga za guwa lansembe zopsereza. Magazi otsalawo athire pa tsinde la guwalo.
35 Esenlik kurbanı kuzusunda olduğu gibi kişi sununun bütün yağını ayırmalı. Kâhin RAB için yakılan sunuların üzerinde hepsini sunakta yakacak. Kâhin kişinin günahını bağışlatacak ve kişi bağışlanacak.
Iye achotse mafuta onse, monga amachotsera mafuta a mwana wankhosa wa chopereka chachiyanjano, ndipo wansembe awatenthe pa guwa pamodzi ndi zopereka zina zopsereza za Yehova. Potero, wansembe adzapereka nsembe yopepesera tchimo limene munthuyo anachita ndipo adzakhululukidwa.