< Hâkimler 16 >

1 Şimşon bir gün Gazze'ye gitti. Orada gördüğü bir fahişenin evine girdi.
Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
2 Gazzeliler'e, “Şimşon buraya geldi” diye haber verilince çevreyi kuşattılar. Bütün gece kentin kapısında pusuya yattılar. “Gün ağarınca onu öldürürüz” diyerek gece boyunca yerlerinden kımıldamadılar.
Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
3 Şimşon gece yarısına dek yattı. Gece yarısı kalktı, kent kapısının iki kanadıyla iki direğini tutup sürgüyle birlikte yerlerinden söktü. Hepsini omuzlayıp Hevron'un karşısındaki tepeye çıkardı.
Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
4 Bir süre sonra Şimşon Sorek Vadisi'nde yaşayan Delila adında bir kadına aşık oldu.
Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
5 Filist beyleri kadına gelip, “Şimşon'un üstün gücünün kaynağı nedir, onu kandırıp öğrenmeye bak” dediler, “Böylece belki onu bağlar, etkisiz hale getirip yenebiliriz. Her birimiz sana bin yüzer parça gümüş vereceğiz.”
Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
6 Bunun üzerine Delila Şimşon'a, “Lütfen, söyle bana, bu üstün gücü nereden alıyorsun?” diye sordu, “Seni bağlayıp yenmek olası mı?”
Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
7 Şimşon, “Beni kurumamış yedi taze sırımla bağlarlarsa sıradan bir adam gibi güçsüz olurum” dedi.
Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
8 Bunun üzerine Filist beyleri Delila'ya kurumamış yedi taze sırım getirdiler. Delila bunlarla Şimşon'u bağladı.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
9 Adamları bitişik odada pusuya yatmıştı. Delila, “Şimşon, Filistliler geldi!” dedi. Şimşon sırımları ateş değdiğinde dağılıveren kendir lifleri gibi koparıp attı. Gücünün sırrını vermemişti.
Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
10 Delila, “Beni kandırdın, bana yalan söyledin” dedi, “Lütfen söyle bana, seni neyle bağlamalı?”
Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
11 Şimşon, “Beni hiç kullanılmamış yeni urganla sımsıkı bağlarlarsa sıradan bir adam gibi güçsüz olurum” dedi.
Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
12 Böylece Delila yeni urgan alıp Şimşon'u bağladı. Sonra, “Şimşon, Filistliler geldi!” dedi. Adamlar hâlâ bitişik odada pusu kurmuş bekliyorlardı. Şimşon urganları iplik koparır gibi koparıp kollarından sıyırdı.
Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
13 Delila ona, “Şimdiye kadar beni hep kandırdın, bana yalan söyledin” dedi, “Söyle bana, seni neyle bağlamalı?” Şimşon, “Başımdaki yedi örgüyü dokuma tezgahındaki kumaşla birlikte dokuyup kazıkla burarsan sıradan bir adam gibi güçsüz olurum” dedi.
Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
14 Şimşon uyurken Delila onun başındaki yedi örgüyü dokuma tezgahındaki kumaşla birlikte dokuyup kazıkla burdu. Sonra, “Şimşon, Filistliler geldi!” dedi. Şimşon uykusundan uyandı, saçını tezgah kazığından ve kumaştan çekip kurtardı.
Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
15 Delila, “Bana güvenmiyorsan nasıl olur da, ‘Seni seviyorum’ diyorsun?” dedi, “Üç kezdir beni kandırıyorsun, üstün gücünün nereden geldiğini söylemiyorsun.”
Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
16 Bu sözlerle Şimşon'u sıkıştırıp günlerce başını ağrıttı. Sonunda Şimşon dayanamayıp
Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
17 yüreğini kadına tümüyle açtı. “Başıma hiç ustura değmedi” dedi, “Çünkü ben ana rahmindeyken Tanrı'ya adanmışım. Tıraş olursam gücümü yitiririm. Sıradan bir adam gibi güçsüz olurum.”
Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
18 Delila Şimşon'un gerçeği söylediğini anlayınca haber gönderip Filist beylerini çağırttı. “Bir kez daha gelin” dedi, “Şimşon bana gerçeği söyledi.” Kadının yanına gelen Filist beyleri gümüşü de birlikte getirdiler.
Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
19 Delila Şimşon'u dizleri üzerinde uyuttuktan sonra adamlardan birini çağırtıp başındaki yedi örgüyü kestirdi. Sonra alay ederek onu dürtüklemeye başladı. Çünkü Şimşon gücünü yitirmişti.
Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
20 Delila, “Şimşon, Filistliler geldi!” dedi. Şimşon uyandı ve, “Her zamanki gibi kalkıp silkinirim” diye düşündü. RAB'bin kendisinden ayrıldığını bilmiyordu.
Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
21 Filistliler onu yakalayıp gözlerini oydular. Gazze'ye götürüp tunç zincirlerle bağladılar, cezaevinde değirmen taşına koştular.
Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
22 Bu arada Şimşon'un kesilen saçları uzamaya başladı.
Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
23 Filist beyleri ilahları Dagon'un onuruna çok sayıda kurban kesip eğlenmek için toplandılar. “İlahımız, düşmanımız Şimşon'u elimize teslim etti” dediler.
Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
24 Halk Şimşon'u görünce kendi ilahlarını övmeye başladı. “İlahımız ülkemizi yakıp yıkan, Birçoğumuzu öldüren Düşmanımızı elimize teslim etti” diyorlardı.
Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
25 İyice coşunca, “Şimşon'u getirin, bizi eğlendirsin” dediler. Şimşon'u cezaevinden getirip oynatmaya başladılar, sonra sütunların arasında durdurdular.
Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
26 Şimşon, elinden tutan gence, “Beni tapınağın damını taşıyan sütunların yanına götür de onlara yaslanayım” dedi.
Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
27 Tapınak erkeklerle, kadınlarla doluydu. Bütün Filist beyleri de oradaydı. Üç bin kadar kadın erkek Şimşon'un oynayışını damdan seyrediyordu.
Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
28 Şimşon RAB'be yakarmaya başladı: “Ey Egemen RAB, lütfen beni anımsa. Ey Tanrı, bir kez daha beni güçlendir; Filistliler'den bir vuruşta iki gözümün öcünü alayım.”
Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
29 Sonra tapınağın damını taşıyan iki ana sütunun ortasında durup sağ eliyle birini, sol eliyle ötekini kavradı.
Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
30 “Filistliler'le birlikte öleyim” diyerek bütün gücüyle sütunlara yüklendi. Tapınak Filist beylerinin ve bütün içindekilerin üzerine çöktü. Böylece Şimşon ölürken, yaşamı boyunca öldürdüğünden daha çok insan öldürdü.
ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
31 Şimşon'un kardeşleriyle babası Manoah'ın bütün ailesi onun ölüsünü almaya geldiler. Şimşon'u götürüp babasının Sora ile Eştaol arasındaki mezarına gömdüler. Şimşon İsrail'i yirmi yıl süreyle yönetmişti.
Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.

< Hâkimler 16 >