< Yeşu 8 >

1 RAB Yeşu'ya, “Korkma, yılma” dedi, “Bütün savaşçılarını yanına alıp Ay Kenti'nin üzerine yürü. Ay Kralı'nı, halkını ve kenti bütün topraklarıyla birlikte sana teslim ediyorum.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Usachite mantha kapena kutaya mtima. Tenga gulu lonse la nkhondo, ndipo upite ku Ai. Taona, ndapereka mfumu ya Ai pamodzi ndi anthu ake, mzinda wake ndi dziko lake lonse mʼmanja mwako.
2 Eriha'ya ve kralına ne yaptıysan, Ay Kenti'ne ve kralına da aynısını yap. Ama mal ve hayvanlardan oluşan ganimeti kendinize ayırın. Kentin gerisinde pusu kur.”
Mzinda wa Ai ndi mfumu yake muchite monga munachita ndi mzinda wa Yeriko ndi mfumu yake, koma katundu wa mumzindamo ndi zoweta mukazitenge ndi kuzisunga kuti zikhale zanu. Mukalalire mzinda wa Ai ndi kuwuthira nkhondo kuchokera kumbuyo.”
3 Böylece Yeşu bütün savaşçılarıyla birlikte Ay Kenti'nin üzerine yürümeye hazırlandı. Seçtiği otuz bin yiğit savaşçıyı geceleyin yola çıkarırken
Kotero Yoswa ndi gulu lonse la nkhondo anakonzeka kupita ku Ai. Iye anasankha amuna 30,000 odziwa kumenya nkhondo bwino ndipo anawatumiza usiku
4 onlara şöyle buyurdu: “Gidip kentin gerisinde pusuya yatın. Kentin çok uzağında durmayın. Hepiniz her an hazır olun.
nawapatsa malamulo awa kuti, “Mvetsani bwino; mukabisale kuseri kwa mzindawo. Musakapite patali ndi mzindawo, koma nonsenu mukakhale okonzekera nkhondo.
5 Ben yanımdaki halkla birlikte kente yaklaşacağım. Bir önceki gibi, düşman kentten çıkıp üzerimize gelince, önlerinde kaçar gibi yapıp
Ine ndi gulu langa lonse tikayamba kuwuputa mzindawu, ndipo akadzangotuluka kudzalimbana nafe, ife tidzawathawa monga tinachitira poyamba.
6 onları kentten uzaklaştırıncaya dek ardımızdan sürükleyeceğiz. Önceki gibi onlardan kaçtığımızı sanacaklar. Biz kaçar gibi yaparken,
Iwo adzatithamangitsa mpaka titawakokera kutali ndi mzindawo, pakuti iwo adzati, ‘Akutithawa monga anachitira poyamba.’ Pamene ife tizidzathawa,
7 siz de pusu kurduğunuz yerden çıkıp kenti ele geçirirsiniz. Tanrımız RAB orayı elinize teslim edecek.
inu mudzatuluke pamene mwabisalapo ndi kulanda mzindawo. Yehova Mulungu wanu adzakupatsani mzindawo.
8 Kenti ele geçirince ateşe verin. RAB'bin buyruğuna göre hareket edin. İşte buyruğum budur.”
Mukakawulanda mzindawo mudzawuyatse moto. Mukachite monga mwa mawu a Yehova. Amenewa ndiwo malamulo amene ndakupatsani.”
9 Ardından Yeşu onları yolcu etti. Adamlar gidip Beytel ile Ay Kenti arasında, Ay Kenti'nin batısında pusuya yattılar. Yeşu ise geceyi halkla birlikte geçirdi.
Yoswa atawatumiza, anapita ku malo wokabisalakowo ndipo anadikirira kumeneko. Malowa anali pakati pa Beteli ndi Ai, kumadzulo kwa Ai. Koma Yoswa anagona usiku umenewu pakati pa gulu lake lankhondo.
10 Yeşu sabah erkenden kalkarak halkı topladı. Sonra kendisi ve İsrail'in ileri gelenleri önde olmak üzere Ay Kenti'ne doğru yola çıktılar.
Mmawa mwake, Yoswa anadzuka nayitana asilikali ake. Tsono iye pamodzi ndi akuluakulu a Aisraeli anatsogola kupita ku Ai.
11 Yeşu, yanındaki bütün savaşçılarla kentin üzerine yürüdü. Yaklaşıp kentin kuzeyinde ordugah kurdular. Kentle aralarında bir vadi vardı.
Gulu lonse la nkhondo limene linali ndi iye linatsogolako ndi kukamanga zithando pafupi ndi mzindawo chakumpoto mopenyana nawo. Pakati pa iwo ndi mzindawo panali chigwa.
12 Yeşu beş bin kişi kadar bir güçle Beytel ile Ay Kenti arasında, kentin batısında pusu kurdurdu.
Yoswa anali atatenga asilikali 5,000 ndi kuwabisa pakati pa Ai ndi Beteli, kumadzulo kwa mzindawo.
13 Ardından hem kuzeyde ordugah kuranlar, hem batıda pusuya yatanlar savaş düzenine girdiler. Yeşu o gece vadide ilerledi.
Anakhazika anthuwo mokonzekera nkhondo. Gulu lalikulu la nkhondo linakamanga zithando zawo kumpoto kwa mzinda, ndipo gulu lina linakamanga zithando zawo kumadzulo kwa mzindawo. Usiku umenewo Yoswa anakagona ku chigwa.
14 Bunu gören Ay Kralı, kent halkıyla birlikte sabah erkenden kalktı. Zaman yitirmeden, İsrailliler'e karşı savaşmak üzere Arava bölgesinin karşısında belirlenen yere çıktı. Ne var ki, kentin gerisinde kendisine karşı kurulan pusudan habersizdi.
Mfumu ya Ai itaona ankhondo a Yoswa, inachita zinthu mofulumira. Inadzuka mmamawa ndipo inapita pamodzi ndi anthu ake ku malo otsika oyangʼanana ndi Araba kuti akachite nkhondo ndi Aisraeli. Koma iyo sinadziwe kuti ayithira nkhondo kudzera kumbuyo kwa mzindawo.
15 Yeşu ile yanındaki İsrailliler, kent halkı önünde bozguna uğramış gibi, çöle doğru kaçmaya başladılar.
Yoswa ndi Aisraeli onse anachita ngati agonja ndi kumathawira ku chipululu.
16 Kentteki bütün halk İsrailliler'i kovalamaya çağrıldı. Ama Yeşu'yu kovalarken kentten uzaklaştılar.
Anthu onse a ku Ai anawuzidwa kuti awapirikitse. Ndipo iwo anapirikitsadi Yoswa uja, ndi kupita kutali ndi mzinda wawo.
17 Ay Kenti'yle Beytel'den İsrailliler'i kovalamaya çıkmayan tek kişi kalmamıştı. İsrailliler'i kovalamaya çıkarlarken kent kapılarını açık bıraktılar.
Palibe munthu wamwamuna wa mzinda wa Ai kapena wa Beteli amene sanatuluke kukapirikitsa Aisraeli. Iwo anasiya mzinda wosatseka ndi kumapirikitsa Aisraeli.
18 RAB Yeşu'ya, “Elindeki palayı Ay Kenti'ne doğru uzat; orayı senin eline teslim ediyorum” dedi. Yeşu elindeki palayı kente doğru uzattı.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Loza mkondo uli mʼdzanja lako ku Ai pakuti ine ndipereka mʼdzanja lanu mzindawo.” Kotero Yoswa analoza mkondowo ku Ai.
19 Elini uzatır uzatmaz, pusudakiler yerlerinden fırlayıp kente girdiler; kenti ele geçirip hemen ateşe verdiler.
Atangotambalitsa dzanja lake, anthu amene anabisala aja ananyamuka msangamsanga pamalo pawo ndi kuthamangira kutsogolo. Iwo analowa mu mzindamo ndi kuwulanda ndipo anawutentha mofulumira.
20 Kentliler arkalarına dönüp bakınca, yanan kentten göklere yükselen dumanı gördüler. Çöle doğru kaçan İsrailliler de geri dönüp onlara saldırınca artık kaçacak hiçbir yerleri kalmadı.
Anthu a ku Ai aja atangochewukira mʼmbuyo anaona utsi uli tolotolo. Koma mpata woti athawireko panalibe pakuti Aisraeli amene amathawira ku chipululu anabwerera nayamba kuwathamangitsa.
21 Pusuya yatmış olanların kenti ele geçirdiğini, kentten dumanlar yükseldiğini gören Yeşu ile yanındaki İsrailliler, geri dönüp Ay halkına saldırdılar.
Yoswa ndi Aisraeli onse ataona kuti obisalira aja alanda mzinda ndipo kuti utsi unali tolotolo, iwo anatembenuka ndi kuyamba kupha anthu a ku Ai.
22 Kenti ele geçirenler de çıkıp saldırıya katılınca, kent halkı iki yönden gelen İsrailliler'in ortasında kaldı. İsrailliler tek canlı bırakmadan hepsini öldürdüler.
Nawonso Aisraeli amene anali mu mzindamo anatuluka kudzalimbana ndi anthu a ku Ai. Choncho iwo anazingidwa mbali zonse ndi Aisraeli ndipo onse anaphedwa. Palibe amene anatsala wamoyo kapena wothawa
23 Sağ olarak tutsak aldıkları Ay Kralı'nı Yeşu'nun önüne çıkardılar.
kupatula mfumu ya ku Ai yokha imene anayigwira nabwera nayo kwa Yoswa.
24 İsrailliler Ay Kenti'nden çıkıp kendilerini kırsal alanlarda ve çölde kovalayanların hepsini kılıçtan geçirdikten sonra kente dönüp geri kalanları da kılıçtan geçirdiler.
Aisraeli aja atatha kupha anthu onse a ku Ai amene anali mʼthengo ndi mʼchipululu kumene anawapirikitsira, onse anabwerera ku Ai ndi kupha onse amene anali mu mzindamo.
25 O gün Ay halkının tümü öldürüldü. Öldürülenlerin toplamı, kadın erkek, on iki bin kişiydi.
Chiwerengero cha anthu onse a ku Ai, amuna ndi akazi, amene anaphedwa pa tsiku limeneli chinali 12,000.
26 Yeşu kentte yaşayanların tümü yok edilinceye dek pala tutan elini indirmedi.
Yoswa sanatsitse dzanja lake limene ananyamula mkondo mpaka ataona kuti onse amene amakhala mu mzinda wa Ai aphedwa.
27 İsrailliler, RAB'bin Yeşu'ya verdiği buyruk uyarınca, kentin yalnız hayvanlarıyla mallarını yağmaladılar.
Tsono Aisraeli anatenga zoweta ndi katundu yense wa anthu ophedwa aja, monga momwe Yehova analamulira Yoswa.
28 Ardından Yeşu Ay Kenti'ni ateşe verdi, yakıp yıkıp viraneye çevirdi. Yıkıntıları bugün de duruyor.
Pambuyo pake Yoswa anawutentha mzinda wa Ai ndi kuwusiya bwinja monga ulili leromu.
29 Ay Kralı'nı ağaca asıp akşama dek orada bırakan Yeşu, güneş batarken cesedi ağaçtan indirerek kent kapısının dışına attırdı. Cesedin üzerine taşlardan büyük bir yığın yaptılar. Bu yığın bugün de duruyor.
Iye anapachika pa mtengo mfumu ya Ai ndipo anayisiya mpaka madzulo. Pomwe dzuwa linalowa Yoswa analamula kuti akachotse mtembowo ndi kukawutaya ku chipata cha mzindawo. Pamwamba pa mtembowo anawunjikapo mulu waukulu wa miyala. Muluwo ulipobe mpaka lero lino.
30 Bundan sonra Yeşu Eval Dağı'nda İsrail'in Tanrısı RAB'be bir sunak yaptı.
Ndipo Yoswa anamanga guwa lansembe la Yehova Mulungu wa Israeli pa phiri la Ebala.
31 Sunak, RAB'bin kulu Musa'nın İsrail halkına verdiği buyruk uyarınca, Musa'nın Yasa Kitabı'nda yazıldığı gibi yontulmamış, demir alet değmemiş taşlardan yapıldı. RAB'be orada yakmalık sunular sundular, esenlik kurbanları kestiler.
Analimanga motsata zimene Mose mtumiki wa Yehova analamulira Aisraeli, ndiponso potsata zomwe zinalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose kuti guwa lansembe likhale la miyala yosasemedwa ndi chitsulo. Pa guwalo anapereka kwa Yehova nsembe yopsereza ndi nsembe yachiyanjano.
32 Yeşu Musa'nın İsrail halkının önünde yazmış olduğu Kutsal Yasa'nın kopyasını orada taş levhalara yazdı.
Kenaka anthu onse akupenya, Yoswa analemba pa miyala chitsanzo cha malamulo amene Mose analemba.
33 Bütün İsrailliler, ileri gelenleriyle, görevlileriyle ve hâkimleriyle birlikte –yabancılar dahil– RAB'bin Antlaşma Sandığı'nın iki yanında, yüzleri, sandığı taşıyan Levili kâhinlere dönük olarak dizildiler. Halkın yarısı sırtını Gerizim Dağı'na, öbür yarısı da Eval Dağı'na verdi. Çünkü RAB'bin kulu Musa kutsanmaları için bu şekilde durmalarını daha önce buyurmuştu.
Aisraeli onse, akuluakulu awo, atsogoleri awo ndi oweruza awo, alendo pamodzi ndi mbadwa, anayimirira mbali zonse ziwiri za Bokosi la Chipangano la Yehova, ena uku ena uku moyangʼanana ndi ansembe a Chilevi. Theka la anthu linayima patsogolo pa phiri la Gerizimu ndipo theka lina patsogolo pa phiri la Ebala, monga momwe Mose mtumiki wa Yehova anawalamulira mʼmbuyomo pamene anawapatsa malangizo podalitsa Aisraeli.
34 Ardından Yeşu yasanın tümünü, kutsama ve lanetle ilgili bölümleri Yasa Kitabı'nda yazılı olduğu gibi okudu.
Pambuyo pake Yoswa anawerenga mawu onse a malamulo, madalitso ndi matemberero monga momwe zinalembedwera mʼbuku la malamulo a Mose.
35 Böylece Yeşu'nun, yabancıların da aralarında bulunduğu kadınlı, çocuklu bütün İsrail topluluğuna, Musa'nın buyruklarından okumadığı tek bir söz kalmadı.
Yoswa anawerenga mawu onse amene Mose analamula, gulu lonse la Israeli limene linasonkhana likumva. Amayi, ana ndi alendo omwe okhala pakati pawo anali pomwepo.

< Yeşu 8 >