< Yeşu 22 >

1 Bundan sonra Yeşu, Ruben ve Gad oymaklarıyla Manaşşe oymağının yarısını topladı.
Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
2 Onlara, “RAB'bin kulu Musa'nın size buyurduğu her şeyi yaptınız” dedi, “Benim bütün buyruklarımı da yerine getirdiniz.
ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
3 Bugüne dek, bunca zaman kardeşlerinizi yalnız bırakmadınız; Tanrınız RAB'bin sizi yükümlü saydığı buyruğu yerine getirdiniz.
Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
4 Görüyorsunuz, Tanrınız RAB, kardeşlerinize söylediği gibi, onları rahata kavuşturdu. Şimdi kalkın, RAB'bin kulu Musa'nın, Şeria Irmağı'nın ötesinde size mülk olarak verdiği topraklardaki evlerinize dönün.
Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
5 RAB'bin kulu Musa'nın size verdiği buyrukları ve Kutsal Yasa'yı yerine getirmeye çok dikkat edin. Tanrınız RAB'bi sevin, tümüyle gösterdiği yolda yürüyün, buyruklarını yerine getirin, O'na bağlı kalın, O'na candan ve yürekten hizmet edin.”
Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
6 Sonra onları kutsayıp yolcu etti. Onlar da evlerine döndüler.
Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
7 Musa Manaşşe oymağının yarısına Başan'da toprak vermişti. Yeşu da oymağın öbür yarısına Şeria Irmağı'nın batısında, öbür kardeşleri arasında toprak vermişti. Bu oymakları kutsayıp evlerine gönderirken,
Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
8 “Evlerinize büyük servetle, çok sayıda hayvanla, altın, gümüş, tunç, demir ve çok miktarda giysiyle dönün” dedi, “Düşmanlarınızdan elde ettiğiniz ganimeti kardeşlerinizle paylaşın.”
nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
9 Böylece Rubenliler'le Gadlılar ve Manaşşe oymağının yarısı, Kenan topraklarındaki Şilo'dan, İsrailliler'in yanından ayrıldılar; RAB'bin buyruğu uyarınca, Musa aracılığıyla yurt edindikleri Gilat topraklarına –kendi mülkleri olan topraklara– dönmek üzere yola çıktılar.
Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
10 Rubenliler'le Gadlılar ve Manaşşe oymağının yarısı, Şeria Irmağı'nın Kenan topraklarında kalan kesimine varınca, ırmak kıyısında büyük ve gösterişli bir sunak yaptılar.
Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
11 Rubenliler'le Gadlılar ve Manaşşe oymağının yarısının Kenan sınırında, Şeria Irmağı kıyısında, İsrailliler'e ait topraklarda bir sunak yaptıklarını
Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
12 duyan İsrail topluluğu, onlara karşı savaşmak üzere Şilo'da toplandı.
gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
13 Ardından İsrailliler Kâhin Elazar'ın oğlu Pinehas'ı Gilat bölgesine, Rubenliler'le Gadlılar'a ve Manaşşe oymağının yarısına gönderdiler.
Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
14 İsrail'in her oymağından birer temsilci olmak üzere on oymak önderini de onunla birlikte gönderdiler. Bunların her biri bir İsrail boyunun başıydı.
Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
15 Gilat topraklarına, Rubenliler'le Gadlılar'a ve Manaşşe oymağının yarısına gelen temsilciler şunları bildirdiler:
Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
16 “RAB'bin topluluğu, ‘Bugün kendinize bir sunak yaparak RAB'be başkaldırdınız, O'nu izlemekten vazgeçtiniz’ diyor, ‘İsrail'in Tanrısı'na karşı bu hainliği nasıl yaparsınız?
“Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
17 Peor'un günahı bize yetmedi mi? RAB'bin topluluğu onun yüzünden felakete uğradı. Bugüne dek kendimizi bu günahtan temizleyebilmiş değiliz.
Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
18 Bugün RAB'bi izlemekten vaz mı geçiyorsunuz? Eğer bugün RAB'be isyan ederseniz, O da yarın bütün İsrail topluluğuna öfkelenir.
Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
19 Eğer size ait olan topraklar murdarsa, RAB'bin Tapınağı'nın bulunduğu RAB'be ait topraklara gelip aramızda mülk edinin. Kendinize, Tanrımız RAB'bin sunağından başka bir sunak yaparak RAB'be ve bize karşı isyan etmeyin.
Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
20 Zerah oğlu Akan RAB'be adanan ganimete ihanet ettiğinde, bütün İsrail topluluğu RAB'bin öfkesine uğramadı mı? Akan'ın günahı yalnız kendisini ölüme götürmekle kalmadı!’”
Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
21 Rubenliler'le Gadlılar ve Manaşşe oymağının yarısı, İsrail boy başlarına şöyle karşılık verdiler:
Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
22 “Tanrıların Tanrısı RAB, tanrıların Tanrısı RAB her şeyi biliyor; İsrail de bilecek. Eğer yaptığımızı, RAB'be isyan etmek ya da O'na ihanet etmek için yaptıysak, ya RAB, bugün bizi esirgeme!
“Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
23 Eğer sunağı, RAB'bi izlemekten vazgeçip yakmalık sunular ve tahıl ya da esenlik sunuları sunmak için yaptıysak, RAB bizden hesap sorsun.
Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
24 Bunu yaparken kaygımız şuydu: Oğullarınız ilerde bizim oğullarımıza, ‘İsrail'in Tanrısı RAB ile ne ilginiz var?
“Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
25 Ey Rubenliler ve Gadlılar, RAB Şeria Irmağı'nı sizinle bizim aramızda sınır yaptı. Sizin RAB'de hiçbir payınız yoktur’ diyebilir, oğullarımızı RAB'be tapmaktan alıkoyabilirler.
Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
26 Bu nedenle, kendimize bir sunak yapalım dedik. Yakmalık sunu ya da kurban sunmak için değil,
“Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
27 yalnız sizinle bizim aramızda ve bizden sonra gelecek kuşaklar arasında bir tanık olması için yaptık. Böylece RAB'bin Tapınağı'nda yakmalık sunularla, kurbanlarla ve esenlik sunularıyla RAB'be tapınacağız. Oğullarınız da ilerde bizim oğullarımıza, ‘RAB'de hiçbir payınız yok’ diyemeyecekler.
Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
28 Şöyle düşündük: İlerde bize ya da gelecek kuşaklarımıza böyle bir şey diyecek olurlarsa, biz de, ‘Atalarımızın RAB için yaptığı sunağın örneğine bakın’ deriz. ‘Yakmalık sunu ya da kurban sunmak için değildir bu. Sizinle bizim aramızdaki birliğin tanığıdır.’
“Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
29 RAB'be isyan etmek, bugün RAB'bi izlemekten vazgeçmek, yakmalık sunu, tahıl sunusu ya da kurban sunmak için Tanrımız RAB'bin sunağından, tapınağının önündeki sunaktan başka bir sunak yapmak bizden uzak olsun.”
“Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
30 Kâhin Pinehas ve onunla birlikte olan topluluk önderleri, yani İsrail'in boy başları, Rubenliler'le Gadlılar'ın ve Manaşşeliler'in söylediklerini duyunca hoşnut kaldılar.
Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
31 Bunun üzerine Kâhin Elazar'ın oğlu Pinehas, Rubenliler'le Gadlılar'a ve Manaşşeliler'e, “Şimdi RAB'bin aramızda olduğunu biliyoruz” dedi, “Çünkü O'na ihanet etmediniz. Böylece İsrailliler'i O'nun elinden kurtardınız.”
Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
32 Kâhin Elazar'ın oğlu Pinehas ve önderler, Rubenliler'le Gadlılar'ın bulunduğu Gilat topraklarından Kenan topraklarına, İsrailliler'in yanına dönüp olan biteni anlattılar.
Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
33 Anlatılanlardan hoşnut kalan İsrailliler Tanrı'ya övgüler sundular. Rubenliler'le Gadlılar'ın yaşadıkları toprakların üzerine yürüyüp savaşmaktan ve orayı yakıp yıkmaktan bir daha söz etmediler.
Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
34 Rubenliler'le Gadlılar, “Bu sunak RAB'bin Tanrı olduğuna sizinle bizim aramızda tanıktır” diyerek sunağa “Tanık” adını verdiler.
Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.

< Yeşu 22 >