< Yeşu 1 >

1 RAB, kulu Musa'nın ölümünden sonra onun yardımcısı Nun oğlu Yeşu'ya şöyle seslendi:
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 “Kulum Musa öldü. Şimdi kalk, bütün halkla birlikte Şeria Irmağı'nı geç. Size, İsrail halkına vereceğim ülkeye girin.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Musa'ya söylediğim gibi, ayak basacağınız her yeri size veriyorum.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 Sınırlarınız çölden Lübnan'a, büyük Fırat Irmağı'ndan –bütün Hitit ülkesi dahil– batıdaki Akdeniz'e kadar uzanacak.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 Yaşamın boyunca hiç kimse sana karşı koyamayacak; nasıl Musa ile birlikte oldumsa, seninle de birlikte olacağım. Seni terk etmeyeceğim, seni yüzüstü bırakmayacağım.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 “Güçlü ve yürekli ol. Çünkü halkı, atalarına vereceğime ant içtiğim ülkeyi miras almaya sen götüreceksin.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Yeter ki, güçlü ve yürekli ol. Kulum Musa'nın sana buyurduğu Kutsal Yasa'nın tümünü yerine getirmeye dikkat et. Gittiğin her yerde başarılı olmak için bu yasadan ayrılma, sağa sola sapma.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Yasa Kitabı'nda yazılanları dilinden düşürme. Tümünü özenle yerine getirmek için gece gündüz onu düşün. O zaman başarılı olacak ve amacına ulaşacaksın.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Sana güçlü ve yürekli ol demedim mi? Korkma, yılma. Çünkü Tanrın RAB gideceğin her yerde seninle birlikte olacak.”
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Bunun üzerine Yeşu, halkın görevlilerine şöyle buyurdu:
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 “Ordugahın ortasından geçip halka şu buyruğu verin: ‘Kendinize kumanya hazırlayın. Çünkü Tanrınız RAB'bin size vereceği ülkeye girip orayı mülk edinmek için üç gün sonra Şeria Irmağı'nı geçeceksiniz.’”
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 Yeşu, Ruben ve Gad oymaklarına ve Manaşşe oymağının yarısına da şöyle dedi:
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 “RAB'bin kulu Musa'nın, ‘Tanrınız RAB bu ülkeyi size verip sizi rahata erdirecek’ dediğini anımsayın.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Kadınlarınız, çocuklarınız ve hayvanlarınız Şeria Irmağı'nın doğusunda, Musa'nın size verdiği topraklarda kalsın. Ama sizler, bütün yiğit savaşçılar, silahlı olarak kardeşlerinizden önce ırmağı geçip onlara yardım edin.
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 RAB sizi rahata erdirdiği gibi, onları da rahata erdirecek. Onlar Tanrınız RAB'bin vereceği ülkeyi mülk edindikten sonra siz de mülk edindiğiniz topraklara, RAB'bin kulu Musa'nın Şeria Irmağı'nın doğusunda size verdiği topraklara dönüp oraya yerleşin.”
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Önderler Yeşu'ya, “Bize ne buyurduysan yapacağız” diye karşılık verdiler, “Bizi nereye gönderirsen gideceğiz.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 Her durumda Musa'nın sözünü dinlediğimiz gibi, senin sözünü de dinleyeceğiz. Yeter ki, Musa'yla birlikte olmuş olan Tanrın RAB seninle de birlikte olsun.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Sözünü dinlemeyen, buyruklarına karşı gelip başkaldıran ölümle cezalandırılacaktır. Yeter ki, sen güçlü ve yürekli ol.”
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Yeşu 1 >