< Yuhanna 8 >
1 İsa ise Zeytin Dağı'na gitti.
Koma Yesu anapita ku phiri la Olivi.
2 Ertesi sabah erkenden yine tapınağa döndü. Bütün halk O'nun yanına geliyordu. O da oturup onlara öğretmeye başladı.
Mmamawa Iye anaonekeranso ku Nyumba ya Mulungu kumene anthu onse anamuzungulira ndipo Iye anakhala pansi nawaphunzitsa.
3 Din bilginleri ve Ferisiler, zina ederken yakalanmış bir kadın getirdiler. Kadını orta yere çıkararak İsa'ya, “Öğretmen, bu kadın tam zina ederken yakalandı” dediler.
Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi anabweretsa mkazi amene anagwidwa akuchita chigololo. Iwo anamuyimiritsa patsogolo pa anthu ndipo
anati kwa Yesu, “Aphunzitsi, mkazi uyu tinamugwira akuchita chigololo.
5 “Musa, Yasa'da bize böyle kadınların taşlanmasını buyurdu, sen ne dersin?”
Mʼmalamulo a Mose anatilamulira kuti akazi otere tiwagende ndi miyala. Tsopano Inu mukuti chiyani?”
6 Bunları İsa'yı denemek amacıyla söylüyorlardı; O'nu suçlayabilmek için bir neden arıyorlardı. İsa eğilmiş, parmağıyla toprağa yazı yazıyordu.
Iwo anagwiritsa ntchito funsoli ngati msampha, ndi cholinga choti apeze chifukwa cha kumuneneza Iye. Koma Yesu anawerama pansi ndi kuyamba kulemba pa dothi ndi chala chake.
7 Durmadan aynı soruyu sormaları üzerine doğruldu ve, “İçinizde kim günahsızsa, ilk taşı o atsın!” dedi.
Pamene iwo anapitirira kumufunsa, Iye anaweramuka ndipo anawawuza kuti, “Ngati wina wa inu alipo wopanda tchimo, ayambe iyeyo kumugenda ndi miyala mkaziyu.”
8 Sonra yine eğildi, toprağa yazmaya başladı.
Iye anaweramanso pansi ndi kulemba pa dothi.
9 Bunu işittikleri zaman, başta yaşlılar olmak üzere, birer birer dışarı çıkıp İsa'yı yalnız bıraktılar. Kadın ise orta yerde duruyordu.
Iwo atamva izi anayamba kuchoka mmodzimmodzi, akuluakulu poyamba, mpaka Yesu anatsala yekha ndi mkaziyo atayimirira pomwepo.
10 İsa doğrulup ona, “Kadın, nerede onlar? Hiçbiri seni yargılamadı mı?” diye sordu.
Yesu anaweramuka ndipo anamufunsa iye kuti, “Akuluakulu aja ali kuti? Kodi palibe amene wakutsutsa?”
11 Kadın, “Hiçbiri, Efendim” dedi. İsa, “Ben de seni yargılamıyorum” dedi. “Git, artık bundan sonra günah işleme!”
Iye anati, “Ambuye, palibe ndi mmodzi yemwe.” “Inenso sindikukutsutsa iwe. Pita kuyambira tsopano usakachimwenso.”
12 İsa yine halka seslenip şöyle dedi: “Ben dünyanın ışığıyım. Benim ardımdan gelen, asla karanlıkta yürümez, yaşam ışığına sahip olur.”
Yesu atayankhulanso kwa anthu, anati, “Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi. Aliyense amene anditsata Ine sadzayenda mu mdima, koma adzakhala ndi kuwala kotsogolera anthu ku moyo.”
13 Ferisiler, “Sen kendin için tanıklık ediyorsun, tanıklığın geçerli değil” dediler.
Afarisi anamutsutsa Iye nati, “Iwe ukudzichitira umboni wa Iwe mwini, umboni wako siwoona.”
14 İsa onlara şu karşılığı verdi: “Kendim için tanıklık etsem bile tanıklığım geçerlidir. Çünkü nereden geldiğimi ve nereye gideceğimi biliyorum. Oysa siz nereden geldiğimi, nereye gideceğimi bilmiyorsunuz.
Yesu anayankha kuti, “Ngakhale Ine ndidzichitire umboni, umboni wangawu ndi woona, pakuti Ine ndikudziwa kumene ndinachokera ndi kumene ndikupita. Koma inu simukudziwa ndi pangʼono pomwe kumene ndinachokera kapena kumene ndikupita.
15 Siz insan gözüyle yargılıyorsunuz. Ben kimseyi yargılamam.
Inu mumaweruza potsata maganizo a anthu chabe. Ine sindiweruza munthu wina aliyense.
16 Yargılasam bile benim yargım doğrudur. Çünkü ben yalnız değilim, ben ve beni gönderen Baba, birlikte yargılarız.
Koma Ine ndikati ndiweruze, ndimaweruza molondola, chifukwa Ine sindili ndekha koma ndili ndi Atate amene anandituma.
17 Yasanızda da, ‘İki kişinin tanıklığı geçerlidir’ diye yazılmıştır.
Mʼmalamulo anu munalembedwa kuti umboni wa anthu awiri ndi wovomerezeka.
18 Kendim için tanıklık eden bir ben varım, bir de beni gönderen Baba benim için tanıklık ediyor.”
Ine ndikudzichitira ndekha umboni; ndipo mboni inanso ndi Atate amene anandituma.”
19 O zaman O'na, “Baban nerede?” diye sordular. İsa şu karşılığı verdi: “Siz ne beni tanırsınız, ne de Babam'ı. Beni tanısaydınız, Babam'ı da tanırdınız.”
Kenaka iwo anamufunsa Iye kuti, “Kodi Atate anuwo ali kuti?” Yesu anayankha kuti, “Inu simundidziwa Ine. Atate anganso simuwadziwa. Mukanandidziwa Ine, mukanawadziwanso Atate anga.”
20 İsa bu sözleri tapınakta öğretirken, bağış toplanan yerde söyledi. Kimse O'nu yakalamadı. Çünkü saati henüz gelmemişti.
Iye anayankhula mawu awa pamene amaphunzitsa Nyumba ya Mulungu pafupi ndi malo amene amaponyapo zopereka. Komabe palibe amene anamugwira Iye, chifukwa nthawi yake inali isanakwane.
21 İsa yine onlara, “Ben gidiyorum. Beni arayacaksınız ve günahınızın içinde öleceksiniz. Benim gideceğim yere siz gelemezsiniz” dedi.
Kenakanso Yesu anawawuza kuti, “Ine ndikupita, ndipo mudzandifunafuna, koma mudzafa muli mʼmachimo anu. Kumene ndikupita, inu simungabwereko.”
22 Yahudi yetkililer, “Yoksa kendini mi öldürecek?” dediler. “Çünkü, ‘Benim gideceğim yere siz gelemezsiniz’ diyor.”
Izi zinachititsa Ayuda kufunsa kuti, “Kodi adzadzipha yekha? Kodi ndicho chifukwa chake akuti, ‘Kumene ndikupita, inu simungabwereko?’”
23 İsa onlara, “Siz aşağıdansınız, ben yukarıdanım” dedi. “Siz bu dünyadansınız, ben bu dünyadan değilim.
Koma Iye anapitiriza kuti, “Inu ndi ochokera pansi pano. Ine ndine wochokera kumwamba. Inu ndinu anthu a dziko la pansi. Ine sindine wa dziko lapansi lino.
24 İşte bu nedenle size, ‘Günahlarınızın içinde öleceksiniz’ dedim. Benim O olduğuma iman etmezseniz, günahlarınızın içinde öleceksiniz.”
Ine ndinakuwuzani kuti mudzafera mʼmachimo anu ngati simukhulupirira kuti Ine Ndine. Ndithu inu mudzafera mʼmachimo anu.”
25 O'na, “Sen kimsin?” diye sordular. İsa, “Başlangıçtan beri size ne söyledimse, O'yum” dedi.
Iwo anafunsa kuti, “Ndinu ndani?” Yesu anayankha kuti, “Monga Ine ndakhala ndikunena nthawi yonseyi,
26 “Sizinle ilgili söyleyecek ve sizleri yargılayacak çok şeyim var. Beni gönderen gerçektir. Ben O'ndan işittiklerimi dünyaya bildiriyorum.”
ndili ndi zambiri zoti ndinene zoweruza inu. Koma Iye amene anandituma ndi woona, ndipo chimene Ine ndamva kuchokera kwa Iye, ndi chimene ndimaliwuza dziko lapansi.”
27 İsa'nın kendilerine Baba'dan söz ettiğini anlamadılar.
Iwo sanazindikire kuti Iye amawawuza za Atate ake.
28 Bu nedenle İsa şöyle dedi: “İnsanoğlu'nu yukarı kaldırdığınız zaman benim O olduğumu, kendiliğimden hiçbir şey yapmadığımı, ama tıpkı Baba'nın bana öğrettiği gibi konuştuğumu anlayacaksınız.
Choncho Yesu anati, “Inu mukadzapachika Mwana wa Munthu, pamenepo mudzadziwa kuti Ine Ndine. Mudzadziwa kuti sindichita kalikonse pa Ine ndekha koma ndimayankhula zokhazo zimene Atate anandiphunzitsa.
29 Beni gönderen benimledir, O beni yalnız bırakmadı. Çünkü ben her zaman O'nu hoşnut edeni yaparım.”
Iye amene anandituma Ine ali nane pamodzi. Iye sanandisiye ndekha popeza nthawi zonse ndimachita zomwe zimamukondweretsa Iye.”
30 Bu sözler üzerine birçokları O'na iman etti.
Pamene Iye ankayankhula zimenezi, ambiri anamukhulupirira.
31 İsa kendisine iman etmiş olan Yahudiler'e, “Eğer benim sözüme bağlı kalırsanız, gerçekten öğrencilerim olursunuz. Gerçeği bileceksiniz ve gerçek sizi özgür kılacak” dedi.
Kwa Ayuda amene anamukhulupirira, Yesu anati, “Ngati inu mutsatira chiphunzitso changa, ndithu ndinu ophunzira anga.
Tsono mudzadziwa choonadi, ndipo choonadicho chidzakumasulani.”
33 “Biz İbrahim'in soyundanız” diye karşılık verdiler, “Hiçbir zaman kimseye kölelik etmedik. Nasıl oluyor da sen, ‘Özgür olacaksınız’ diyorsun?”
Iwo anamuyankha Iye kuti, “Ife ndife zidzukulu za Abrahamu ndipo sitinakhalepo akapolo a wina aliyense. Kodi mukunena bwanji kuti, ‘Ife tidzamasulidwa?’”
34 İsa, “Size doğrusunu söyleyeyim, günah işleyen herkes günahın kölesidir” dedi.
Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wochita tchimo ndi kapolo wa tchimolo.
35 “Köle ev halkının sürekli bir üyesi değildir, ama oğul sürekli üyesidir. (aiōn )
Pajatu kapolo alibe malo wokhazikika mʼbanja, koma mwana ndi wa mʼbanjamo nthawi zonse. (aiōn )
36 Bunun için, Oğul sizi özgür kılarsa, gerçekten özgür olursunuz.
Nʼchifukwa chake ngati Mwana adzakumasulani, mudzakhala mfulu ndithu.
37 İbrahim'in soyundan olduğunuzu biliyorum. Yine de beni öldürmek istiyorsunuz. Çünkü yüreğinizde sözüme yer vermiyorsunuz.
Ine ndikudziwa kuti inu ndinu zidzukulu za Abrahamu. Chonsecho inu mwakonzeka kundipha Ine, chifukwa mawu anga alibe malo mwa inu.
38 Ben Babam'ın yanında gördüklerimi söylüyorum, siz de babanızdan işittiklerinizi yapıyorsunuz.”
Ine ndikukuwuzani zimene ndaziona pamaso pa Atate, ndipo inu mukuchita zimene mwazimva kwa abambo anu.”
39 “Bizim babamız İbrahim'dir” diye karşılık verdiler. İsa, “İbrahim'in çocukları olsaydınız, İbrahim'in yaptıklarını yapardınız” dedi.
Iwo anayankha kuti, “Ife abambo athu ndi Abrahamu.” Yesu anati, “Inu mukanakhala ana a Abrahamu, bwenzi mukuchita zinthu zimene Abrahamuyo ankachita.
40 “Ama şimdi beni –Tanrı'dan işittiği gerçeği sizlere bildireni– öldürmek istiyorsunuz. İbrahim bunu yapmadı.
Koma mmene zililimu, inu mwatsimikiza kundipha Ine, munthu amene ndinakuwuzani choonadi chimene Ine ndinachimva kuchokera kwa Mulungu. Abrahamu sanachite zinthu zoterezi.
41 Siz babanızın yaptıklarını yapıyorsunuz.” “Biz zinadan doğmadık. Bir tek Babamız var, o da Tanrı'dır” dediler.
Inu mukuchita zinthu zimene abambo anu amachita.” Iwo anatsutsa kuti, “Ife si ana amʼchigololo, Atate amene tili nawo ndi Mulungu yekha.”
42 İsa, “Tanrı Babanız olsaydı, beni severdiniz” dedi. “Çünkü ben Tanrı'dan çıkıp geldim. Kendiliğimden gelmedim, beni O gönderdi.
Yesu anawawuza kuti, “Mulungu akanakhala Atate anu, inu mukanandikonda Ine, pakuti Ine ndinachokera kwa Mulungu ndipo tsopano ndili pano. Ine sindinabwere mwa Ine ndekha.
43 Söylediklerimi neden anlamıyorsunuz? Benim sözümü dinlemeye dayanamıyorsunuz da ondan.
Nʼchifukwa chiyani simukumvetsetsa mawu anga? Chifukwa chake nʼchakuti simungathe kumva zoyankhula zanga.
44 Siz babanız İblis'tensiniz ve babanızın arzularını yerine getirmek istiyorsunuz. O başlangıçtan beri katildi. Gerçeğe bağlı kalmadı. Çünkü onda gerçek yoktur. Yalan söylemesi doğaldır. Çünkü o yalancıdır ve yalanın babasıdır.
Inu ndinu ana a mdierekezi. Iye ndiye abambo anu ndipo mukufuna kuchita zimene abambo anuwo amakhumba. Iye anali wakupha kuyambira pachiyambi, sanasunge choonadi, pakuti mwa iye mulibe choonadi. Pamene Iye anena bodza, amayankhula chiyankhulo chobadwa nacho, popeza ndi wabodza ndipo ndi bambo wa mabodza.
45 Ama ben gerçeği söylüyorum. İşte bunun için bana iman etmiyorsunuz.
Koma chifukwa ndikuwuzani choonadi, inu simukundikhulupirira Ine!
46 Hanginiz bana günahlı olduğumu kanıtlayabilir? Gerçeği söylüyorsam, niçin bana iman etmiyorsunuz?
Ndani mwa inu angatsimikize kuti ndine wochimwa? Ngati Ine ndikunena choonadi, nʼchifukwa chiyani simukundikhulupirira?
47 Tanrı'dan olan, Tanrı'nın sözlerini dinler. İşte siz Tanrı'dan olmadığınız için dinlemiyorsunuz.”
Munthu wochokera kwa Mulungu amamva zimene Mulungu amanena. Chifukwa chimene simumvera nʼchakuti, inuyo sindinu ochokera kwa Mulungu.”
48 Yahudiler O'na şu karşılığı verdiler: “‘Sen, cin çarpmış bir Samiriyeli'sin’ demekte haklı değil miyiz?”
Ayuda anamuyankha Iye kuti, “Kodi ife sitikulondola ponena kuti Inu ndi Msamariya ndi wogwidwa ndi chiwanda?”
49 İsa, “Beni cin çarpmadı” dedi. “Ben Babam'ı onurlandırıyorum, ama siz beni aşağılıyorsunuz.
Yesu anati, “Ine sindinagwidwe ndi chiwanda, koma ndimalemekeza Atate anga, koma inu mukundinyoza.
50 Ben kendimi yüceltmek istemiyorum, ama bunu isteyen ve yargılayan biri vardır.
Ine sindidzifunira ndekha ulemu; koma alipo wina amene amandifunira, ndipo Iyeyo ndiye woweruza.
51 Size doğrusunu söyleyeyim, bir kimse sözüme uyarsa, ölümü asla görmeyecektir.” (aiōn )
Ine ndikukuwuzani choonadi, munthu akasunga mawu anga, sadzafa konse.” (aiōn )
52 Yahudiler, “Seni cin çarptığını şimdi anlıyoruz” dediler. “İbrahim öldü, peygamberler de öldü. Oysa sen, ‘Bir kimse sözüme uyarsa, ölümü asla tatmayacaktır’ diyorsun. (aiōn )
Pamenepo Ayuda anafuwula kuti, “Tsopano ife tadziwadi kuti Inu ndi wogwidwa ndi chiwanda! Abrahamu anafa ndiponso aneneri, koma Inu mukunena kuti, ‘Ngati munthu asunga mawu anga, sadzafa.’ (aiōn )
53 Yoksa sen babamız İbrahim'den üstün müsün? O öldü, peygamberler de öldü. Sen kendini kim sanıyorsun?”
Kodi ndinu wa mkulu kuposa abambo athu Abrahamu? Iye anafa, ndiponso aneneri onse. Inu mukuganiza kuti ndinu yani?”
54 İsa şu karşılığı verdi: “Eğer ben kendimi yüceltirsem, yüceliğim hiçtir. Beni yücelten, ‘Tanrımız’ diye çağırdığınız Babam'dır.
Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndidzilemekeza ndekha, ulemu wangawo ndi wosatanthauza kanthu. Atate anga amene inu mukuti ndi Mulungu wanu, ndiye amene amandilemekeza Ine.
55 Siz O'nu tanımıyorsunuz, ama ben tanıyorum. O'nu tanımadığımı söylersem, sizin gibi yalancı olurum. Ama ben O'nu tanıyor ve sözüne uyuyorum.
Ngakhale kuti inuyo simukumudziwa, Ineyo ndikumudziwa. Ngati Ine nditanena kuti sindikumudziwa, Ineyo nditha kukhala wabodza ngati inuyo, koma Ine ndimamudziwa ndipo ndimasunga mawu ake.
56 Babanız İbrahim günümü göreceği için sevinçle coşmuştu. Gördü ve sevindi.”
Abambo anu Abrahamu anakondwera poyembekezera kubwera kwanga. Iwo anandiona ndipo anasangalala.”
57 Yahudiler, “Sen daha elli yaşında bile değilsin. İbrahim'i de mi gördün?” dediler.
Ayuda anati kwa Iye, “Inu sumunafike nʼkomwe zaka makumi asanu, ndipo mukuti munamuona Abrahamu!”
58 İsa, “Size doğrusunu söyleyeyim, İbrahim doğmadan önce ben varım” dedi.
Yesu anayankha kuti, “Ine ndikukuwuzani choonadi, Abrahamu asanabadwe, Ine Ndine!”
59 O zaman İsa'yı taşlamak için yerden taş aldılar, ama O gizlenip tapınaktan çıktı.
Pamenepo iwo anatola miyala kuti amugende, koma Yesu anabisala, nachoka mozemba mʼNyumba ya Mulungu.