< Eyüp 38 >
1 RAB kasırganın içinden Eyüp'ü şöyle yanıtladı:
Apo Yehova anamuyankha Yobu mʼkamvuluvulu. Ndipo anati:
2 “Bilgisizce sözlerle Tasarımı karartan bu adam kim?
“Kodi uyu ndani amene akusokoneza uphungu wanga poyankhula mawu opanda nzeru?
3 Şimdi erkek gibi kuşağını beline vur da, Ben sorayım, sen anlat.
Onetsa chamuna; ndikufunsa ndipo undiyankhe.
4 “Ben dünyanın temelini atarken sen neredeydin? Anlıyorsan söyle.
“Kodi unali kuti pamene ndinkayika maziko a dziko lapansi? Ndiwuze ngati ukudziwa.
5 Kim saptadı onun ölçülerini? Kuşkusuz biliyorsun! Kim çekti ipi üzerine?
Ndani amene analemba malire ake? Ndithudi iwe ukudziwa! Ndani amene anayeza ndi chingwe dzikoli?
6 Neyin üstüne yapıldı temelleri? Kim koydu köşe taşını,
Kodi maziko ake anawakumba potani, kapena ndani anayika mwala wake wapangodya,
7 Sabah yıldızları birlikte şarkı söylerken, İlahi varlıklar sevinçle çığrışırken?
pamene nyenyezi za kummawa zinkayimba pamodzi ndipo angelo onse a Mulungu ankafuwula mokondwa?
8 “Denizin ardından kapıları kim kapadı, Ana rahminden fışkırdığı zaman;
“Kodi ndani amene anatsekera nyanja pamene inkalengedwa, pamene inkachita ngati kutumphuka pansi pa dziko,
9 Ona bulutları giysi, Koyu karanlığı kundak yaptığım,
pamene ndinasandutsa mitambo kukhala chovala chake ndi kuyikulunga mu mdima wandiweyani,
10 Sınırını koyduğum, Kapılarıyla sürgülerini yerleştirdiğim,
pamene ndinayilembera malire ake ndikuyikira zitseko ndi mipiringidzo yake.
11 ‘Buraya kadar gelip öteye geçmeyeceksin, Gururlu dalgaların şurada duracak’ dediğim zaman?
Pamene ndinati, ‘Ufike mpaka apa ndipo usapitirire apa ndiye pamene mafunde ako amphamvuwo azilekezera?’
12 “Sen ömründe sabaha buyruk verdin mi, Şafağa yerini gösterdin mi;
“Kodi chibadwire chako unalamulapo dzuwa kuti lituluke mmawa, kapena kuti mʼbandakucha ukhalepo pa nthawi yake,
13 Yeryüzünün uçlarını tutsun, Oradaki kötüler silkilip atılsın diye?
kuti kuwalako kuwunikire dziko lonse lapansi ndi kuthamangitsa anthu oyipa?
14 Mühür basılan balçık gibi biçim değiştirir yeryüzü, Giysi kıvrımları gibi göze çarpar.
Chifukwa cha kuwala kwa usana mapiri ndi zigwa zimaonekera bwino ngati zilembo za chidindo pa mtapo; zimaonekera bwino ngati makwinya a chovala.
15 Kötülerin ışıkları alınır, Kalkan kolları kırılır.
Kuwala kwa dzuwako sikuwafikira anthu oyipa, ndipo dzanja lawo silingathe kuchita kanthu.
16 “Denizin kaynaklarına vardın mı, Gezdin mi enginin diplerinde?
“Kodi unayendapo pansi penipeni pa nyanja kapena pa magwero ake ozama?
17 Ölüm kapıları sana gösterildi mi? Gördün mü ölüm gölgesinin kapılarını?
Kodi anakuonetsapo zipata za imfa? Kodi unaonako ku dziko la anthu akufa kumene kuli mdima wandiweyani?
18 Dünyanın genişliğini kavradın mı? Anlat bana, bütün bunları biliyorsan.
Kodi kukula kwa dziko lapansi umakudziwa? Undiwuze ngati ukuzidziwa zonsezi.
19 “Işığın bulunduğu yerin yolu nerede? Ya karanlık, onun yeri neresi?
“Kodi njira yopita kumene kumakhala kuwala ili kuti? Nanga mdima umakhala kuti?
20 Onları yerlerine götürebilir misin? Evlerinin yolunu biliyor musun?
Kodi iwe ungathe kuziperekeza kwawoko zimenezi? Kodi ukuyidziwa njira yopita kwawoko?
21 Bilmediğin şey yok zaten, Çünkü onlarla aynı zamanda doğmuştun! O kadar yaşlısın!
Ndithu, iwe ukuyidziwa, poti paja nthawi imeneyo nʼkuti utabadwa kale! Wakhala ndi moyo zaka zambiridi!
22 “Karın ambarlarına girdin mi, Dolunun ambarlarını gördün mü?
“Kodi unalowamo mʼnyumba zosungira chisanu chowundana kapena unayionapo nyumba yosungira matalala,
23 Ben onları sıkıntılı günler için, Kavga ve savaş günleri için saklıyorum.
zimene ndazisungira nthawi ya mavuto ndi nthawi yomenyana ndi ya nkhondo?
24 Nerede ışığın dağıtıldığı, Doğu rüzgarının yeryüzüne saçıldığı yere giden yol?
Kodi umadziwa njira ya kumene kumachokera chingʼaningʼani kapena njira ya kumene kumachokera mphepo ya kummawa imene ili pa dziko lonse lapansi?
25 Kim sellere kanal, Yıldırımlara yol açtı;
Kodi ndani amene amakonza ngalande za mvula, nanga ndani anakonza njira yoyendamo mphenzi,
26 Kimsenin yaşamadığı toprakları, İnsanın bulunmadığı çölü sulasın diye;
kuthirira madzi dziko limene sikukhala munthu, chipululu chopandamo munthu,
27 Kurak ve ıssız yeri doyursun, Ot bitirsin diye?
kukhutitsa nthaka yowuma yagwaa ndi kumeretsamo udzu?
28 Yağmurun babası var mı? Çiy damlalarını kim yarattı?
Kodi mvula ili ndi abambo ake? Nanga madzi a mame anawabereka ndani?
29 Buz kimin rahminden çıktı? Göklerden düşen kırağıyı kim doğurdu,
Kodi madzi owundana anawabereka ndani? Ndani amene anabereka chisanu chochokera kumwamba
30 Sular taş gibi katılaşıp Enginin yüzü donunca?
pamene madzi amawuma gwaa ngati mwala, pamene madzi a pa nyanja amazizira, nalimba kuti gwaa?
31 “Ülker yıldızlarını bağlayabilir misin? Oryon'un bağlarını çözebilir misin?
“Kodi iwe ungayimitse kuyenda kwa nyenyezi? Kodi ungathe kuletsa kuyenda kwa nsangwe ndi akamwiniatsatana?
32 Mevsimlerinde çıkartabilir misin takımyıldızları? Büyük ve Küçük Ayı'ya yol gösterebilir misin?
Kodi ungathe kuwongolera nyenyezi pa nyengo yake kapena kutsogolera nyenyezi yayikulu ya chimbalangondo pamodzi ndi ana ake?
33 Biliyor musun göklerin yasalarını? Tanrı'nın yönetimini yeryüzünde kurabilir misin?
Kodi malamulo a mlengalenga umawadziwa? Kodi ungathe kukhazikitsa ulamuliro wa Mulungu pa dziko lapansi?
34 “Başına bol yağmur yağsın diye Bulutlara sesini duyurabilir misin?
“Kodi iwe ungathe kulamula mitambo kuti igwetse mvula ya chigumula?
35 Varıp da, ‘Buradayız’ desinler diye, Şimşekleri gönderebilir misin?
Kodi ungathe kutumiza zingʼaningʼani kuti zingʼanime? Kodi zimabwera pamaso pako ndi kuti, ‘Tili pano?’
36 Kim mısırturnasına bilgelik, Horoza anlayış verdi?
Kodi ndani anayika nzeru mu mtima, ndani analonga mʼmaganizo nzeru zomvetsa zinthu?
37 Kimin bulutları sayacak bilgisi var? Kim göklerin tulumlarını boşaltabilir,
Wanzeru ndani amene angathe kuwerenga mitambo? Ndani angathe kupendeketsa mitsuko ya madzi akuthambo
38 Toprak sertleşip Parçaları birbirine yapışınca?
pamene fumbi limasanduka matope, ndipo matopewo amawumbika?
39 “Dişi aslanlar için sen avlanabilir misin, Genç aslanların karnını doyurabilir misin,
“Kodi ndani amawusakira chakudya mkango waukazi ndi kukhutitsa misona ya mikango
40 İnlerine sindikleri, Çalılıkta pusuya yattıkları zaman?
pamene ili khale mʼmapanga mwawo kapena pamene ikubisala pa tchire?
41 Kuzguna yiyeceğini kim sağlıyor, Yavruları Tanrı'ya feryat edip Açlıktan kıvrandığı zaman?
Kodi amamupatsa khwangwala chakudya chake ndani pamene ana ake akulirira kwa Mulungu ndi kumayendayenda chifukwa chosowa zakudya?