< Eyüp 35 >
1 Elihu konuşmasına şöyle devam etti:
Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,
2 “‘Tanrı'nın önünde haklıyım’ diyorsun. Doğru buluyor musun bunu?
“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza? Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’
3 Ama hâlâ, ‘Günah işlemezsem Yararım ne, kazancım ne?’ diye soruyorsun.
Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani, ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’
4 “Ben yanıtlayayım seni Ve arkadaşlarını.
“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu pamodzi ndi abwenzi anu omwe.
5 Göklere bak da gör, Üzerinde yükselen bulutlara göz gezdir.
Yangʼanani kumwamba ndipo muone mitambo imene ili kutali ndi inuyo.
6 Günah işlersen, Tanrı'ya ne zararı olur? İsyanların çoksa ne olur O'na?
Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani? Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?
7 Doğruysan, O'na verdiğin nedir, Ya da ne alır O senin elinden?
Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani? Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?
8 Kötülüğün ancak senin gibi birine zarar verir, Doğruluğun ise yalnız insanoğlu içindir.
Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo, ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.
9 “İnsanlar ağır baskı altında feryat ediyor, Güçlülere karşı yardım istiyor.
“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa; akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.
10 Ama kimse, ‘Nerede Yaratıcım Tanrı?’ demiyor; O Tanrı ki, gece bize ezgiler verir,
Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga, amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,
11 Yeryüzündeki hayvanlardan çok bize öğretir Ve bizi gökteki kuşlardan daha bilge kılar.
amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’
12 Kötülerin gururu yüzünden insanlar feryat ediyor, Ama yanıtlayan yok.
Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.
13 Gerçek şu ki, Tanrı boş feryadı dinlemez, Her Şeye Gücü Yeten bunu önemsemez.
Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake; Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.
14 O'nu görmediğini söylediğin zaman bile Davan O'nun önündedir, bekle;
Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti Iye saona zimene zikuchitika. Iye adzaweruza molungama ngati inu mutamudikira
15 Madem bu öfkeyle şimdi cezalandırmadı, İsyana da pek aldırmaz diyorsun.
ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango, zoyipa zambiri zimene anthu amachita,
16 Bu yüzden Eyüp ağzını boş yere açıyor, Bilgisizce konuştukça konuşuyor.”
abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake, mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”