< Eyüp 34 >

1 Elihu konuşmasına şöyle devam etti:
Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,
2 “Ey bilgeler, sözlerimi dinleyin, Kulak verin bana, ey bilgi sahipleri.
“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru; tcherani khutu inu anthu ophunzira.
3 Çünkü damak nasıl yemeği tadarsa, Kulak da sözleri sınar.
Pakuti khutu limayesa mawu monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.
4 Gelin, doğruyu seçelim, İyiyi birlikte öğrenelim.
Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera; tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.
5 “Çünkü Eyüp, ‘Ben suçsuzum’ diyor, ‘Tanrı hakkımı elimden aldı.
“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa, koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.
6 Haklı olduğum halde yalancı sayılıyorum, Suçsuz olduğum halde okunla yaraladın beni.’
Ngakhale ndine wolungama mtima, akundiyesa wabodza; ngakhale ndine wosachimwa, mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’
7 Eyüp gibisi var mı? Alayı su gibi içiyor!
Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani, amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?
8 Kötülük yapanlarla dostluk edip geziyor, Kötülerle aynı yolda yürüyor.
Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa; amayanjana ndi anthu oyipa mtima.
9 Çünkü, ‘Tanrı'yı hoşnut etmeye çalışmak İnsana yarar getirmez’ diyor.
Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’
10 “Bu yüzden, ey sağduyulu insanlar, beni dinleyin! Tanrı kötülük yapar mı, Her Şeye Gücü Yeten haksızlık eder mi? Asla!
“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu. Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe, Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.
11 Çünkü O herkese yaptığının karşılığını öder, Hak ettiğini başına getirir.
Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake; Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.
12 Tanrı kesinlikle kötülük etmez, Her Şeye Gücü Yeten adaleti saptırmaz.
Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa, kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.
13 Kim yeryüzünü O'na emanet etti? Kim O'nu bütün dünyanın başına atadı?
Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani? Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?
14 Eğer niyet eder de Ruhunu ve soluğunu geri çekerse,
Mulungu akanakhala ndi maganizo oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,
15 Bütün insanlık bir anda yok olur, İnsan yine toprağa döner.
zamoyo zonse zikanawonongekeratu ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.
16 “Aklın varsa dinle, Kulak ver sözlerime.
“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi; mvetserani zimene ndikunena.
17 Adaletten nefret eden hiç hüküm sürebilir mi? Adil ve güçlü olanı suçlayacak mısın?
Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira? Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?
18 Krallara, ‘Değersizsiniz’, Soylulara, ‘Kötüsünüz’ diyen,
Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’ ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’
19 Önderlere ayrıcalık tanımayan, Zengini yoksuldan çok önemsemeyen O değil mi? Çünkü hepsi O'nun ellerinin işidir.
Iye sakondera akalonga ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka, pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?
20 Gece yarısı bir anda ölürler, Herkes sarsılır, ölüp gider, Güçlüler de insan eli değmeden alınıp götürülür.
Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku; anthu amachita mantha ndipo amamwalira; munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.
21 “Tanrı'nın gözleri insanların yolundan ayrılmaz, Attıkları her adımı görür.
“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu; amaona mayendedwe ake onse.
22 Kötülük yapanların gizlenebileceği Ne karanlık bir yer vardır, ne de ölüm gölgesi.
Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.
23 Yargılanmak için önüne gelsinler diye, Tanrı insanları sorgulamaya pek gerek duymaz.
Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu, kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.
24 Araştırmadan güçlü insanları kırar, Onların yerine başkalarını diker.
Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.
25 Çünkü ne yaptıklarını bilir, Gece onları deviriverir, ezilirler.
Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.
26 Herkesin gözü önünde Kötülükleri yüzünden onları cezalandırır;
Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo, pamalo pamene aliyense akuwaona;
27 Artık O'nun ardından gitmedikleri, Yollarının hiçbirini dikkate almadıkları için.
Chifukwa anasiya kumutsata ndipo sasamaliranso njira zake zonse.
28 Yoksulun feryadını O'na duyurdular; Düşkünlerin feryadını işitti.
Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake, kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.
29 Ama Tanrı sessiz kalırsa kim O'nu suçlayabilir? Yüzünü gizlerse kim O'nu görebilir? Bir ulusa karşı da bir insana karşı da O hep aynıdır,
Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa? Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe? Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,
30 Tanrısız insan krallık etmesin, Halka tuzak kurmasın diye.
kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza, kuti asatchere anthu misampha.
31 “Kimse Tanrı'ya, ‘Suçluyum, artık kötülük yapmayacağım’ dedi mi,
“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti, ‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,
32 ‘Göremediğimi sen bana öğret, Haksızlık ettimse, bir daha etmem?’
ndiphunzitseni zimene sindikuziona ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’
33 O'nu reddettiğin halde, Senin keyfince mi seni ödüllendirmeli? Çünkü karar verecek olan sensin, ben değil, Öyleyse anlat bana bildiğini.
Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira, pamene inu mukukana kulapa? Chisankho nʼchanu, osati changa; tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.
34 “Sağduyulu insanlar, Beni dinleyen bilgeler diyecekler ki,
“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana, anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,
35 ‘Eyüp bilgisizce konuşuyor, Sözlerinin değeri yok.’
‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru; mawu ake ndi opanda fundo.’
36 Kötü biri gibi yanıtladığı için Keşke Eyüp'ün sınanması sonsuza dek sürse!
Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!
37 Çünkü günahına isyan da ekliyor, Önümüzde alay edercesine el çırpıyor, Tanrı'ya karşı konuştukça konuşuyor.”
Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira; amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu, ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

< Eyüp 34 >