< Eyüp 30 >

1 “Ama şimdi, yaşı benden küçük olanlar Benimle alay etmekte, Oysa babalarını sürümün köpeklerinin Yanına koymaya tenezzül etmezdim.
“Koma tsopano akundinyoza, ana angʼonoangʼono kwa ine, anthu amene makolo awo sindikanawalola kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
2 Çünkü güçleri tükenmişti, Bileklerinin gücü ne işime yarardı?
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine, pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
3 Yoksulluktan, açlıktan bitkindiler, Akşam çölde, ıssız çorak yerlerde kök kemiriyorlardı.
Anali atatheratu kuwonda ndi njala, ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi, mʼchipululu usiku.
4 Çalılıklarda karapazı topluyor, Retem kökü yiyorlardı.
Ankathyola therere ndi masamba owawa, ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
5 Toplumdan kovuluyorlardı, İnsanlar hırsızmışlar gibi onlara bağırıyordu.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo, akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
6 Korkunç vadilerde, yerdeki deliklerde, Kaya kovuklarında yaşıyorlardı.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma, pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
7 Çalıların arasında anırır, Çalı altında birbirine sokulurlardı.
Ankalira ngati nyama kuthengo ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
8 Aptalların, adı sanı belirsiz insanların çocuklarıydılar, Ülkeden kovulmuşlardı.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina, anathamangitsidwa mʼdziko.
9 “Şimdiyse destan oldum dillerine, Ağızlarına doladılar beni.
“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe; ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Benden tiksiniyor, uzak duruyorlar, Yüzüme tükürmekten çekinmiyorlar.
Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa; akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Tanrı ipimi çözüp beni alçalttığı için Dizginsiz davranmaya başladılar bana.
Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa, iwowo analekeratu kundiopa.
12 Sağımdaki ayak takımı üzerime yürüyor, Ayaklarımı kaydırıyor, Bana karşı rampalar kuruyorlar.
Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane; andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda, andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Yolumu kesiyor, Kimseden yardım görmeden Beni yok etmeye çalışıyorlar.
Iwo anditsekera njira; akufuna kundichititsa ngozi, popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Koca bir gedikten girer gibi ilerliyor, Yıkıntılar arasından üzerime yuvarlanıyorlar.
Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka, iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Dehşet çöktü üzerime, Onurum rüzgara kapılmış gibi uçtu, Mutluluğum bulut gibi geçip gitti.
Zoopsa zandithetsa mphamvu; ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo, chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.
16 “Şimdi tükeniyorum, Acı günler beni ele geçirdi.
“Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo; ndili mʼmasiku amasautso.
17 Geceleri kemiklerim sızlıyor, Beni kemiren acılar hiç durmuyor.
Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti zowawa zanga sizikuleka.
18 Tanrı'nın şiddeti Üzerimdeki giysiye dönüştü, Gömleğimin yakası gibi beni sıkıyor.
Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa; Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Beni çamura fırlattı, Toza, küle döndüm.
Wandiponya mʼmatope, ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.
20 “Sana yakarıyorum, ama yanıt vermiyorsun, Ayağa kalktığımda gözünü bana dikiyorsun.
“Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha; ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Bana acımasız davranıyor, Bileğinin gücüyle beni eziyorsun.
Inuyo mumandichitira zankhanza; mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Beni kaldırıp rüzgara bindiriyorsun, Fırtınanın içinde darma duman ediyorsun.
Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo; mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Biliyorum, beni ölüme, Bütün canlıların toplanacağı yere götüreceksin.
Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa, kumalo kumene amoyo onse adzapitako.
24 “Kuşkusuz düşenin dostu olmaz, Felakete uğrayıp yardım istediğinde.
“Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima, amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Sıkıntıya düşenler için ağlamaz mıydım? Yoksullar için üzülmez miydim?
Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto? Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Ama ben iyilik beklerken kötülük geldi, Işık umarken karanlık geldi.
Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera; pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 İçim kaynıyor, rahatım yok, Önümde acı günler var.
Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka; ndili mʼmasiku amasautso.
28 Yaslı yaslı dolaşıyorum, güneş yok, Topluluk içinde kalkıp feryat ediyorum.
Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa; ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Çakallarla kardeş, Baykuşlarla arkadaş oldum.
Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe, mnzawo wa akadzidzi.
30 Derim karardı, soyuluyor, Kemiklerim ateşten yanıyor.
Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka; thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Lirimin sesi yas feryadına, Neyimin sesi ağlayanların sesine döndü.
Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro, ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

< Eyüp 30 >