< Eyüp 21 >

1 Eyüp şöyle yanıtladı:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Sözümü dikkatle dinleyin, Bana verdiğiniz avuntu bu olsun.
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Bırakın ben de konuşayım, Ben konuştuktan sonra alay edin.
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 “Yakınmam insana mı karşı? Niçin sabırsızlanmayayım?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Bana bakın da şaşın, Elinizi ağzınıza koyun.
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 Bunu düşündükçe içimi korku sarıyor, Bedenimi titreme alıyor.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Kötüler niçin yaşıyor, Yaşlandıkça güçleri artıyor?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Çocukları sapasağlam çevrelerinde, Soyları gözlerinin önünde.
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Evleri güvenlik içinde, korkudan uzak, Tanrı'nın sopası onlara dokunmuyor.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Boğalarının çiftleşmesi hiç boşa çıkmaz, İnekleri hep doğurur, hiç düşük yapmaz.
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Çocuklarını sürü gibi salıverirler, Yavruları oynaşır.
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Tef ve lir eşliğinde şarkı söyler, Ney sesiyle eğlenirler.
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Ömürlerini bolluk içinde geçirir, Esenlik içinde ölüler diyarına inerler. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Tanrı'ya, ‘Bizden uzak dur!’ derler, ‘Yolunu öğrenmek istemiyoruz.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Her Şeye Gücü Yeten kim ki, O'na kulluk edelim? Ne kazancımız olur O'na dua etsek?’
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Ama zenginlikleri kendi ellerinde değil. Kötülerin öğüdü benden uzak olsun.
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 “Kaç kez kötülerin kandili söndü, Başlarına felaket geldi, Tanrı öfkelendiğinde paylarına düşen kederi verdi?
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Kaç kez rüzgarın sürüklediği saman gibi, Kasırganın uçurduğu saman çöpü gibi oldular?
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 ‘Tanrı babaların cezasını çocuklarına çektirir’ diyorsunuz, Kendilerine çektirsin de bilsinler nasıl olduğunu.
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Yıkımlarını kendi gözleriyle görsünler, Her Şeye Gücü Yeten'in gazabını içsinler.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Çünkü sayılı ayları sona erince Geride bıraktıkları aileleri için niye kaygı çeksinler?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 “En yüksektekileri bile yargılayan Tanrı'ya Kim akıl öğretebilir?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Biri gücünün doruğunda ölür, Büsbütün rahat ve kaygısız.
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 Bedeni iyi beslenmiş, İlikleri dolu.
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Ötekiyse acı içinde ölür, İyilik nedir hiç tatmamıştır.
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Toprakta birlikte yatarlar, Üzerlerini kurt kaplar.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 “Bakın, düşüncelerinizi, Bana zarar vermek için kurduğunuz düzenleri biliyorum.
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 ‘Büyük adamın evi nerede?’ diyorsunuz, ‘Kötülerin çadırları nerede?’
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Yolculara hiç sormadınız mı? Anlattıklarına kulak asmadınız mı?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Felaket günü kötü insan esirgenir, Gazap günü ona kurtuluş yolu gösterilir.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Kim davranışını onun yüzüne vurur? Kim yaptığının karşılığını ona ödetir?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Mezarlığa taşınır, Kabri başında nöbet tutulur.
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Vadi toprağı tatlı gelir ona, Herkes ardından gider, Önüsıra gidenlerse sayısızdır.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 “Boş laflarla beni nasıl avutursunuz? Yanıtlarınızdan çıkan tek sonuç yalandır.”
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Eyüp 21 >