< Eyüp 17 >

1 “Yaşama gücüm tükendi, günlerim kısaldı, Mezar gözlüyor beni.
“Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
2 Çevremi alaycılar kuşatmış, Gözümü onların aşağılamasıyla açıp kapıyorum.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
3 “Ey Tanrı, kefilim ol kendine karşı, Başka kim var bana güvence verecek?
“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
4 Çünkü onların aklını anlayışa kapadın, Bu yüzden onları zafere kavuşturmayacaksın.
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
5 Para için dostlarını satan adamın Çocuklarının gözünün feri söner.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
6 “Tanrı beni insanların diline düşürdü, Yüzüme tükürmekteler.
“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
7 Kederden gözümün feri söndü, Kollarım bacaklarım çırpı gibi.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
8 Dürüst insanlar buna şaşıyor, Suçsuzlar tanrısızlara saldırıyor.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
9 Doğrular kendi yolunu tutuyor, Elleri temiz olanlar gittikçe güçleniyor.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
10 “Ama siz, hepiniz gelin yine deneyin! Aranızda bir bilge bulamayacağım.
“Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Günlerim geçti, tasarılarım, Dileklerim suya düştü.
Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Bu insanlar geceyi gündüze çeviriyorlar, Karanlığa ‘Işık yakındır’ diyorlar.
Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Ölüler diyarını evim diye gözlüyorsam, Yatağımı karanlığa seriyorsam, (Sheol h7585)
Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
14 Çukura ‘Babam’, Kurda ‘Annem, kızkardeşim’ diyorsam,
ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 Umudum nerede? Kim benim için umut görebilir?
tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
16 Umut benimle ölüler diyarına mı inecek? Toprağa birlikte mi gireceğiz?” (Sheol h7585)
Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)

< Eyüp 17 >