< Eyüp 12 >

1 Eyüp şöyle yanıtladı:
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 “Kendinizi bir şey sandığınız belli, Ama bilgelik de sizinle birlikte ölecek!
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 Sizin kadar benim de aklım var, Sizden aşağı kalmam. Kim bilmez bunları?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 “Gülünç oldum dostlarıma, Ben ki, Tanrı'ya yakarırdım, yanıtlardı beni. Doğru ve kusursuz adam gülünç oldu.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Kaygısızlar felaketi küçümser, Ayağı kayanı umursamaz.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 Soyguncuların çadırlarında rahatlık var, Tanrı'yı gazaba getirenler güvenlik içinde, Tanrı'ya değil, kendi bileklerine güveniyorlar.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 “Ama şimdi sor hayvanlara, sana öğretsinler, Gökte uçan kuşlara sor, sana anlatsınlar,
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Toprağa söyle, sana öğretsin, Denizdeki balıklara sor, sana bilgi versinler.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Hangisi bilmez Bunu RAB'bin yaptığını?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 Her yaratığın canı, Bütün insanlığın soluğu O'nun elindedir.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Damağın yemeği tattığı gibi Kulak da sözleri denemez mi?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Bilgelik yaşlılarda, Akıl uzun yaşamdadır.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 “Bilgelik ve güç Tanrı'ya özgüdür, O'ndadır öğüt ve akıl.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 O'nun yıktığı onarılamaz, O'nun hapsettiği kişi özgür olamaz.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Suları tutarsa, kuraklık olur, Salıverirse dünyayı sel götürür.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 Güç ve zafer O'na aittir, Aldanan da aldatan da O'nundur.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 Danışmanları çaresiz kılar, Yargıçları çıldırtır.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 Kralların bağladığı bağı çözer, Bellerine kuşak bağlar.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 Kâhinleri çaresiz kılar, Koltuklarında yıllananları devirir.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 Güvenilir danışmanları susturur, Yaşlıların aklını alır.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 Rezalet saçar soylular üzerine, Güçlülerin kuşağını gevşetir.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 Karanlıkların derin sırlarını açar, Ölüm gölgesini aydınlığa çıkarır.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 Ulusları büyütür, ulusları yok eder, Ulusları genişletir, ulusları sürgün eder.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 Dünya önderlerinin aklını başından alır, Yolu izi belirsiz bir çölde dolaştırır onları.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 Karanlıkta el yordamıyla yürür, ışık yüzü görmezler; Sarhoş gibi dolaştırır onları.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.

< Eyüp 12 >