< Eyüp 11 >

1 Naamalı Sofar şöyle yanıtladı:
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,
2 “Bunca söz yanıtsız mı kalsın? Çok konuşan haklı mı sayılsın?
“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa? Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
3 Saçmalıkların karşısında sussun mu insanlar? Sen alay edince kimse seni utandırmasın mı?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku? Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
4 Tanrı'ya, ‘İnancım arıdır’ diyorsun, ‘Senin gözünde temizim.’
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
5 Ama keşke Tanrı konuşsa, Sana karşı ağzını açsa da,
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
6 Bilgeliğin sırlarını bildirse! Çünkü bilgelik çok yönlüdür. Bil ki, Tanrı günahlarından bazılarını unuttu bile.
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake, pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri. Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.
7 “Tanrı'nın derin sırlarını anlayabilir misin? Her Şeye Gücü Yeten'in sınırlarına ulaşabilir misin?
“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu? Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
8 Onlar gökler kadar yüksektir, ne yapabilirsin? Ölüler diyarından derindir, nasıl anlayabilirsin? (Sheol h7585)
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani? Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani? (Sheol h7585)
9 Ölçüleri yeryüzünden uzun, Denizden geniştir.
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.
10 “Gelip seni hapsetse, mahkemeye çağırsa, Kim O'na engel olabilir?
“Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Çünkü O yalancıları tanır, Kötülüğü görür de dikkate almaz mı?
Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo; akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Ne zaman yaban eşeği insan doğurursa, Aptal da o zaman sağduyulu olur.
Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.
13 “O'na yüreğini adar, Ellerini açarsan,
“Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 İşlediğin günahı kendinden uzaklaştırır, Çadırında haksızlığa yer vermezsen,
ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 Utanmadan başını kaldırır, Sağlam ve korkusuz olabilirsin.
udzatukula mutu wako wosachita manyazi; udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Sıkıntılarını unutur, Akıp gitmiş sular gibi anarsın onları.
Udzayiwala ndithu zowawa zako, zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 Yaşamın öğlen güneşinden daha parlak olur, Karanlık sabaha döner.
Moyo wako udzawala kupambana usana, ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 Güven duyarsın, çünkü umudun olur, Çevrene bakıp güvenlik içinde yatarsın.
Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo; ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Uzanırsın, korkutan olmaz, Birçokları senden lütuf diler.
Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 Ama kötülerin gözlerinin feri sönecek, Kaçacak yer bulamayacaklar, Tek umutları son soluklarını vermek olacak.”
Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza, ndipo adzasowa njira yothawirapo; chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

< Eyüp 11 >