< Yeremya 52 >

1 Sidkiya yirmi bir yaşında kral oldu ve Yeruşalim'de on bir yıl krallık yaptı. Annesi Livnalı Yeremya'nın kızı Hamutal'dı.
Zedekiya anali wa zaka 21 pamene analowa ufumu, ndipo analamulira zaka 11 ku Yerusalemu. Amayi ake anali Hamutali mwana wa Yeremiya wa ku Libina.
2 Yehoyakim gibi Sidkiya da RAB'bin gözünde kötü olanı yaptı.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova, monga momwe anachitira Yehoyakimu.
3 RAB Yeruşalim'le Yahuda'ya öfkelendiği için onları huzurundan attı. Sidkiya Babil Kralı'na karşı ayaklandı.
Chifukwa cha zonse zimene zinachitika ku Yerusalemu ndi ku Yuda Yehova anakwiyira anthu ake mpaka kuwachotsa pamaso pake. Tsono Zedekiya anawukira mfumu ya ku Babuloni.
4 Sidkiya'nın krallığının dokuzuncu yılında, onuncu ayın onuncu günü, Babil Kralı Nebukadnessar bütün ordusuyla Yeruşalim önlerine gelip ordugah kurdu. Kentin çevresine rampa yaptılar.
Choncho mʼchaka cha chisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku la khumi, Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anabwera ndi ankhondo ake onse kudzathira nkhondo Yerusalemu. Anamanga misasa ndi mitumbira yankhondo kunja kuzungulira mzindawo.
5 Kral Sidkiya'nın krallığının on birinci yılına kadar kent kuşatma altında kaldı.
Mzindawo unazingidwa mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha ulamuliro wa Mfumu Zedekiya.
6 Dördüncü ayın dokuzuncu günü kentte kıtlık öyle şiddetlendi ki, halk bir lokma ekmek bulamaz oldu.
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi wachinayi njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti munalibe chakudya choti anthu nʼkudya.
7 Sonunda kentin surlarında bir gedik açıldı. Kildaniler kenti çepeçevre kuşatmış olmasına karşın, bütün askerler gece kral bahçesinin yolundan iki duvarın arasındaki kapıdan kaçarak Arava yoluna çıktılar.
Tsono linga la mzindawo linabowoledwa, ndipo ankhondo onse anathawa. Iwo anatuluka mu mzindamo usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri a pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Ndipo anathawira ku Araba,
8 Ama Kildani ordusu Kral Sidkiya'nın ardına düşerek Eriha ovalarında ona yetişti. Sidkiya'nın bütün ordusu dağıldı.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
9 Kral Sidkiya yakalanıp Hama topraklarında, Rivla'da Babil Kralı'nın huzuruna çıkarıldı. Babil Kralı onun hakkında karar verdi.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula mʼdziko la Hamati, kumene anagamula mlandu wake.
10 Sidkiya'nın gözü önünde oğullarını, sonra da bütün Yahuda önderlerini öldürttü.
Ku Ribulako mfumu ya ku Babuloni inapha ana aamuna a Zedekiya iyeyo akuona; ndiponso inapha akuluakulu onse a ku Yuda.
11 Sidkiya'nın gözlerini oydu, zincire vurup Babil'e götürdü. Sidkiya öldüğü güne dek cezaevinde tutuldu.
Ndipo inamukolowola maso Zedekiya, ndi kumumanga ndi maunyolo a mkuwa nʼkupita naye ku Babuloni kumene inakamuyika mʼndende kuti akhalemo moyo wake wonse.
12 Babil Kralı Nebukadnessar'ın krallığının on dokuzuncu yılında, beşinci ayın onuncu günü muhafız birliği komutanı, Babil Kralı'nın görevlisi Nebuzaradan Yeruşalim'e girdi.
Mwezi wachisanu, pa tsiku lakhumi, chaka cha 19 cha ulamuliro wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo a mfumu, amene amatumikira mfumu ya ku Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
13 RAB'bin Tapınağı'nı, sarayı ve Yeruşalim'deki bütün evleri ateşe verip önemli yapıları yaktı.
Ndipo anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse.
14 Muhafız birliği komutanı önderliğindeki Kildani ordusu Yeruşalim'i çevreleyen bütün surları yıktı.
Tsono gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene linali ndi mtsogoleri wa ankhondo a mfumu uja linagwetsa malinga onse ozungulira Yerusalemu.
15 Komutan Nebuzaradan yoksullardan bazılarını, kentte sağ kalanları, Babil Kralı'nın safına geçen kaçakları ve zanaatçıları sürgün etti.
Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, anthu aluso pamodzi ndi amene anadzipereka kale kwa mfumu ya ku Babuloni kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
16 Ancak bağcılık, çiftçilik yapsınlar diye bazı yoksulları orada bıraktı.
Komabe Nebuzaradani mtsogoleri wa ankhondo anasiya anthu ena onse osaukitsitsa a mʼdzikomo kuti azigwira ntchito mʼminda ya mpesa ndi minda ina.
17 Kildaniler RAB'bin Tapınağı'ndaki tunç sütunları, ayaklıkları, tunç havuzu parçalayıp tunçları Babil'e götürdüler.
Ababuloni anaphwanya nsanamira za mkuwa, maphaka ndi chimbiya chamkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova. Anatenga mkuwa wonsewo nʼkupita nazo ku Babuloni.
18 Tapınak törenlerinde kullanılan kovaları, kürekleri, fitil maşalarını, çanakları, tabakları, bütün tunç eşyaları aldılar.
Ankhondowo anatenganso mbiya, zochotsera phulusa, zozimitsira nyale, mbale zofukizira lubani, zikho pamodzi ndi ziwiya zina zonse za mkuwa zimene ankagwiritsira ntchito mʼNyumba ya Yehova.
19 Muhafız birliği komutanı saf altın ve gümüş tasları, buhurdanları, çanakları, kovaları, kandillikleri, tabakları, dökmelik sunu taslarını alıp götürdü.
Nebuzaradani uja anatenganso mabeseni, ziwiya zosonkhapo moto, mbale zowazira madzi, zoyikapo nyale, zipande zofukizira lubani ndi zikho ndi zina zonse zagolide ndi siliva.
20 RAB'bin Tapınağı için Kral Süleyman'ın yaptırmış olduğu iki sütun, havuz ve altındaki on iki tunç boğa heykeliyle ayaklıklar için hesapsız tunç harcanmıştı.
Nsanamira ziwiri zija, chimbiya, maphaka ndi ngʼombe khumi ndi ziwiri za mkuwa zochirikizira chimbiyacho zimene mfumu Solomoni anapangira Nyumba ya Yehova kulemera kwake kunali kosawerengeka.
21 Her sütun on sekiz arşın yüksekliğindeydi, çevresi on iki arşındı. Her birinin kalınlığı dört parmaktı, içi boştu.
Nsanamira imodzi kutalika kwake kunali mamita asanu ndi atatu, akazunguliza chingwe inali mamita asanu ndi theka; mʼkati mwake munali bowo ndipo kuchindikala kwake kunali zala zinayi.
22 Üzerinde tunç bir başlık vardı. Başlığın yüksekliği beş arşındı, çevresi tunçtan ağ ve nar motifleriyle bezenmişti. Öbür sütun da nar motifleriyle süslenmişti ve ötekine benziyordu.
Pamwamba pa nsanamira iliyonse panali mutu wamkuwa umene kutalika kwake kunali mamita awiri. Pozungulira pake panali ukonde ndi makangadza, zonsezo za mkuwa. Nsanamira inayo inalinso ndi makangadza ake ndipo inali yofanana ndi inzake ija.
23 Yanlarda doksan altı nar motifi vardı. Başlığı çevreleyen ağ motifinin üzerinde toplam yüz nar motifi bulunuyordu.
Mʼmbali mwake munali makangadza 96; makangadza onse pamodzi analipo 100 kuzungulira ukonde onse.
24 Muhafız birliği komutanı Nebuzaradan Başkâhin Seraya'yı, Başkâhin Yardımcısı Sefanya'yı ve üç kapı nöbetçisini tutsak aldı.
Mtsogoleri wa ankhondo uja, anagwira Seraya mkulu wa ansembe ndi Zefaniya, wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apachipata.
25 Kentte kalan askerlerin komutanını, kralın yedi danışmanını, ayrıca ülke halkını askere yazan ordu komutanının yazmanını ve ülke halkından kentte bulunan altmış kişiyi tutsak etti.
Mu mzindamo anagwiramo mkulu amene ankalamulira ankhondo, ndi alangizi amfumu asanu ndi awiri. Anagwiranso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo, amene ankalemba anthu mʼdzikomo, pamodzi ndi anthu ena 60 amene anali mu mzindamo.
26 Hepsini Rivla'ya, Babil Kralı'nın yanına götürdü.
Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondoyo anawatenga onse napita nawo kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula.
27 Babil Kralı Hama ülkesinde, Rivla'da onları idam etti. Böylece Yahuda halkı ülkesinden sürülmüş oldu.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloniyo inalamula kuti anthuwo aphedwe. Motero anthu a ku Yuda anapita ku ukapolo, kutali ndi dziko lawo.
28 Nebukadnessar'ın sürgüne götürdüğü halkın sayısı şudur: Yedinci yıl 3 023 Yahudi;
Chiwerengero cha anthu amene Nebukadinezara anawatenga kupita nawo ku ukapolo ndi ichi: Mʼchaka cha chisanu ndi chiwiri cha ulamuliro wake, anatenga Ayuda 3,023;
29 Nebukadnessar'ın on sekizinci yılında Yeruşalim'den 832 kişi;
mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, anatenga anthu 832 kuchokera mu Yerusalemu;
30 yirmi üçüncü yılında, muhafız birliği komutanı Nebuzaradan'ın sürdüğü 745 Yahudi. Hepsi 4 600 kişiydi.
mʼchaka cha 23 cha ulamuliro wa Nebukadinezara, Nebuzaradani, mtsogoleri wa ankhondo a mfumu anagwira Ayuda 745 kupita ku ukapolo. Onse pamodzi analipo anthu 4,600.
31 Yahuda Kralı Yehoyakin'in sürgündeki otuz yedinci yılı Evil-Merodak Babil Kralı oldu. Evil-Merodak o yılın on ikinci ayının yirmi beşinci günü, Yahuda Kralı Yehoyakin'e lütfederek onu cezaevinden çıkardı.
Mʼchaka chimene Evili-Merodaki analowa ufumu wa Babuloni, iye anakomera mtima Yehoyakini mfumu ya ku Yuda, namutulutsa mʼndende. Izi zinachitika pa tsiku la 25 la mwezi wa khumi ndi chiwiri zitatha zaka 37 chitengedwere Yehoyakimu ku ukapolo.
32 Kendisiyle tatlı tatlı konuştu ve ona Babil'deki öteki sürgün krallardan daha üstün bir yer verdi.
Evili-Merodaki anakomera mtima Yehoyakini, namupatsa malo aulemu kuposa mafumu ena amene anali naye ku Babuloni.
33 Yehoyakin cezaevi giysilerini üstünden çıkardı. Yaşadığı sürece Babil Kralı'nın sofrasında yer aldı.
Choncho Yehoyakini analoledwa kuvula zovala zake za ku ndende ndipo tsiku ndi tsiku ankadya ndi mfumu pa moyo wake wonse.
34 Yaşamı boyunca Babil Kralı tarafından günlük yiyeceği sürekli karşılandı.
Tsiku ndi tsiku mfumu ya ku Babuloni inkamupatsa Yehoyakini phoso lake nthawi yonse ya moyo wake, mpaka pa nthawi ya imfa yake.

< Yeremya 52 >