< Yeremya 48 >

1 Moav'a ilişkin: İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB şöyle diyor: “Vay Nevo'nun başına gelenlere! Çünkü viraneye çevrilecek. Kiryatayim utandırılacak, ele geçirilecek. Misgav utandırılacak, kırılıp dökülecek.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Moav artık övülmeyecek, Heşbon'da onun yıkımı için düzen kuracak, ‘Haydi, şu Moav ulusuna son verelim’ diyecekler. Ey Madmen, sen de susturulacaksın, Kılıç kovalayacak seni.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 Horonayim'den feryat duyulacak: ‘Kent mahvoldu, büyük yıkıma uğradı!’
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 “Moav yıkılacak, Yavrularının ağlayışı duyulacak.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 Ağlaya ağlaya çıkıyorlar Luhit Yokuşu'ndan, Horonayim inişinde Yıkımın neden olduğu acı feryatlar duyuluyor.
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Kaçın, canınızı kurtarın! Çölde yaban eşeği gibi koşun!
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 “Evet, başarılarına, mal varlığına güvendiğin için Sen de ele geçirileceksin. İlahın Kemoş da kâhinleri ve görevlileriyle birlikte Sürgün edilecek.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 Yok edici her kente uğrayacak, Tek kent kurtulmayacak. Vadi yerle bir olacak, Yayla altüst edilecek” diyor RAB.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 “Moav toprağına tuz dökün, kısırlaşsın, Kentleri öyle viran olacak ki, Kimse yaşamayacak oralarda.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 Lanet olsun RAB'bin işini savsaklayana! Kılıcını kan dökmekten alıkoyana lanet olsun!
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Moav gençliğinden bu yana güvenlikteydi, Şarap tortusu gibi durgun kaldı, Bir kaptan öbürüne boşaltılmadı, Sürgüne gönderilmedi. O yüzden tadını yitirmedi, kokusu bozulmadı.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 “Ama onu boşaltacak adamları göndereceğim günler geliyor” diyor RAB, “Onu boşaltacaklar. Kaplarını boşaltacak, küplerini paramparça edecekler.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 İsrail halkı güvendiği Beytel'den nasıl utandıysa, Moav da Kemoş ilahından öyle utanacak.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 “Nasıl, ‘Biz yiğidiz, Savaşa hazır askerleriz’ dersiniz?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moav ve kentlerini yerle bir eden, Saldırıya geçti. En seçkin gençleri kesime gidecek. Adı Her Şeye Egemen RAB olan Kral böyle diyor.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 Moav'ın yıkımı yakında geliyor, Uğrayacağı felaket hızla yaklaşıyor.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 Dövünün onun için, Ey çevresinde yaşayan, ününü bilen sizler! ‘Kudret asası, Görkemli değnek nasıl da kırıldı!’ deyin.
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 “Ey Divon Kenti'nde yaşayan halk, Görkeminden in, Kuru toprak üstünde otur. Çünkü Moav'ı yerle bir eden sana da saldıracak, Kalelerini yıkacak.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Ey sen, Aroer'de oturan, Yol kenarında dur da gözle! Kaçan adama, kurtulan kadına, ‘Ne oldu?’ diye sor.
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Moav utandırıldı, darmadağın oldu. Feryat et, haykır! Moav'ın yıkıldığını Arnon Vadisi'nde duyur.
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 “Yayladaki kentler –Holan, Yahas, Mefaat, Divon, Nevo, Beytdivlatayim, Kiryatayim, Beytgamul, Beytmeon, Keriyot, Bosra, uzak yakın bütün Moav kentleri– yargılanacak.
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 Moav'ın boynuzu kesildi, kolu kırıldı” diyor RAB.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 “Moav'ı sarhoş edin, Çünkü RAB'be büyüklük tasladı. Moav kendi kusmuğunda yuvarlanacak, Alay konusu olacak.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 İsrail senin için gülünesi bir ulus mu oldu? Hırsızlar arasında mı yakalandı ki, Ondan söz ettikçe baş sallıyorsun?
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 “Ey Moav'da yaşayanlar, Kentlerinizi terk edip kayalara sığının. Uçurumun ağzında yuvasını yapan Güvercin gibi olun.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 Moav'ın ne denli gururlanıp büyüklendiğini, Kendini ne denli beğendiğini, Kibirlenip küstahlaştığını, Övünüp kabardığını duyduk.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 Küstahlığını biliyorum” diyor RAB, “Övünmesi boşunadır, yaptıkları da.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Bu yüzden Moav için haykıracak, Bütün Moav için feryat edeceğim. Ağlayacağım Kîr-Hereset halkı için.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 Ey Sivma asması, Senin için Yazer halkından çok ağlayacağım. Filizlerin gölü aşıp Yazer'e ulaştı. Yok edici yaz meyvelerini, üzümünü yok etti.
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 Moav'ın meyve bahçelerinden, tarlalarından Sevinç ve neşe yok oldu. Üzüm sıkma çukurlarından şarap akışını durdurdum; Kimse sevinç çığlıklarıyla üzüm ezmiyor, Çığlıklar var, ama sevinç çığlıkları değil.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 “Heşbon ve Elale'nin haykırışları Yahas'a ulaşıyor. Soar'dan Horonayim'e, Eglat-Şelişiya'ya dek çığlıklar yükseliyor. Çünkü Nimrim suları bile kurudu.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Moav'da puta tapılan yerlerde Sunu sunanları, İlahlarına buhur yakanları Yok edeceğim” diyor RAB.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 “Bu yüzden yüreğim ney gibi İnliyor Moav için; Kîr-Hereset halkı için ney gibi İnliyor yüreğim. Çünkü elde ettikleri zenginlik uçup gitti.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 “Herkes saçını sakalını kesecek, Elini yaralayacak, Beline çul saracak.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 Moav damlarında, meydanlarında Yalnız ağlayış var. Çünkü Moav'ı kimsenin beğenmediği Bir kap gibi kırdım” diyor RAB.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 “Nasıl da darmadağın oldu Moav! Nasıl acıyla feryat ediyor! Nasıl da sırtını dönüyor utançtan! Moav çevresindekilere alay konusu, Dehşet verici bir örnek oldu.”
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 RAB diyor ki, “Bakın! Düşman birden çullanan bir kartal gibi Kanatlarını Moav'ın üzerine açacak.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 Keriyot ele geçirilecek, Kaleler alınacak. O gün Moavlı askerlerin yüreği, Doğum sancısı çeken kadının yüreği gibi olacak.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 Moav yıkıma uğrayacak, Halk olmaktan çıkacak; Çünkü RAB'be karşı büyüklük tasladı.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Önünde dehşet, çukur ve tuzak var, Ey Moav halkı!” diyor RAB.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 “Dehşetten kaçan çukura düşecek, Çukurdan çıkan tuzağa yakalanacak; Çünkü Moav'ın üzerine Cezalandırma yılını getireceğim” diyor RAB.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 “Heşbon'un gölgesinde Bitkin düşmüş kaçkınlar. Çünkü Heşbon'dan ateş, Sihon'un ortasından alev çıktı; Moavlılar'ın alınlarını, Kargaşa çıkaranların başlarını yakıp yok etti.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Vay sana, ey Moav! İlah Kemoş'un halkı yok oldu, Oğulların sürgüne gönderildi, Kızların tutsak alındı.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 Ama son günlerde Yine eski gönencine kavuşturacağım Moav'ı” diyor RAB. Moav'ın yargısı burada sona eriyor.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Yeremya 48 >