< Yeremya 25 >
1 Yahuda Kralı Yoşiya oğlu Yehoyakim'in döneminin dördüncü yılında, RAB Yahuda halkıyla ilgili olarak Yeremya'ya seslendi. Nebukadnessar'ın Babil Kralı oluşunun birinci yılıydı bu.
Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
2 Peygamber Yeremya Yahuda halkına ve Yeruşalim'de yaşayanlara RAB'bin sözünü aktararak şöyle dedi:
Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
3 Yirmi üç yıldır, Yahuda Kralı Amon oğlu Yoşiya'nın döneminin on üçüncü yılından bugüne dek, RAB bana sesleniyor. Ben de RAB'bin sözünü defalarca size aktardım, ama dinlemediniz.
Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
4 RAB peygamber kullarını defalarca size gönderdi, ama dinlemediniz, kulak asmadınız.
Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
5 Sizi uyardılar, “Şimdi herkes kötü yolundan, kötü işlerinden dönsün ki, RAB'bin sonsuza dek size ve atalarınıza verdiği toprakta yaşayasınız” dediler,
Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
6 “Kulluk etmek, tapınmak için başka ilahların ardınca gitmeyin; elinizle yaptığınız putlarla beni öfkelendirmeyin ki, ben de size zarar vermeyeyim.”
Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
7 “Ama beni dinlemediniz” diyor RAB, “Sonuç olarak elinizle yaptığınız putlarla beni öfkelendirip kendinizi zarara soktunuz.”
“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
8 Bunun için Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “Madem sözlerimi dinlemediniz,
Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
9 ben de bütün kuzeydeki halkları ve kulum Babil Kralı Nebukadnessar'ı çağırtacağım” diyor RAB, “Onları bu ülkeye de burada yaşayanlarla çevresindeki bütün uluslara da karşı getireceğim. Bu halkı tamamen yok edeceğim, ülkelerini dehşet ve alay konusu edip sonsuz bir viraneye çevireceğim.
ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
10 Sevinç ve neşe sesini, gelin güvey sesini, değirmen taşlarının sesini, kandil ışığını onlardan uzaklaştıracağım.
Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
11 Bütün ülke bir virane, dehşet verici bir yer olacak. Bu uluslar Babil Kralı'na yetmiş yıl kulluk edecekler.
Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
12 “Ama yetmiş yıl dolunca” diyor RAB, “Suçları yüzünden Babil Kralı'yla ulusunu, Kildan ülkesini cezalandıracak, sonsuz bir viranelik haline getireceğim.
“Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
13 O ülke için söylediklerimin hepsini, Yeremya'nın uluslara ettiği bu kitapta yazılı bütün peygamberlik sözlerini ülkenin başına getireceğim.
Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
14 Pek çok ulus, büyük krallar onları köle edinecek. Yaptıklarına ve ellerinden çıkan işe göre karşılık vereceğim onlara.”
Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
15 İsrail'in Tanrısı RAB bana şöyle dedi: “Elimdeki öfke şarabıyla dolu kâseyi al, seni göndereceğim bütün uluslara içir.
Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
16 Şarabı içince sendeleyecek, üzerlerine göndereceğim kılıç yüzünden çıldıracaklar.”
Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
17 Böylece kâseyi RAB'bin elinden alıp beni gönderdiği bütün uluslara içirdim:
Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
18 Bugün olduğu gibi viranelik, dehşet ve alay konusu, lanetlik olsunlar diye Yeruşalim'e, Yahuda kentlerine, krallarıyla önderlerine;
Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
19 Firavunla görevlilerine, önderlerine ve halkına,
Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
20 Mısır'da yaşayan bütün yabancılara; Ûs krallarına, Filist krallarına –Aşkelon'a, Gazze'ye, Ekron'a, Aşdot'tan sağ kalanlara–
ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
21 Edom'a, Moav'a, Ammon'a;
Edomu, Mowabu ndi Amoni.
22 bütün Sur ve Sayda krallarına, deniz aşırı ülkelerin krallarına;
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
23 Dedan'a, Tema'ya, Bûz'a, zülüflerini kesen bütün halklara;
ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
24 Arabistan krallarına, çölde yaşayan yabancı halkın krallarına;
Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
25 Zimri, Elam, Med krallarına;
Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
26 sırasıyla uzak yakın bütün kuzey krallarına, yeryüzündeki bütün ulusların krallarına içirdim. Hepsinden sonra Şeşak Kralı da içecektir.
ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
27 “Sonra onlara de ki, ‘İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB şöyle diyor: Üzerinize salacağım kılıç yüzünden sarhoş olana dek için, kusun, düşüp kalkmayın.’
“Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
28 Eğer kâseyi elinden alır, içmek istemezlerse, de ki, ‘Her Şeye Egemen RAB şöyle diyor: Kesinlikle içeceksiniz!
Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
29 Bana ait olan kentin üzerine felaket getirmeye başlıyorum. Cezasız kalacağınızı mı sanıyorsunuz? Sizi cezasız bırakmayacağım. İşte dünyada yaşayan herkesin üzerine kılıcı çağırıyorum. Her Şeye Egemen RAB böyle diyor.’
Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
30 “Bütün bu peygamberlik sözlerini onlara ilet: “‘Yükseklerden kükreyecek RAB, Kutsal konutundan gürleyecek, Ağılına şiddetle kükreyecek. Dünyada yaşayanların tümüne Üzüm ezenler gibi bağıracak.
“Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
31 Gürültü yeryüzünün dört yanında yankılanacak. Çünkü RAB uluslara dava açacak; Herkesi yargılayacak Ve kötüleri kılıca teslim edecek’” diyor RAB.
Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
32 Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “İşte felaket ulustan ulusa yayılıyor! Dünyanın dört bucağından büyük kasırga kopuyor.”
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
33 O gün RAB dünyayı bir uçtan bir uca öldürülenlerle dolduracak. Onlar için yas tutulmayacak, toplanıp gömülmeyecekler. Toprağın üzerinde gübre gibi kalacaklar.
Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
34 Haykırın, ey çobanlar, Acı acı bağırın! Toprakta yuvarlanın, ey sürü başları! Çünkü boğazlanma zamanınız doldu, Değerli bir kap gibi düşüp parçalanacaksınız.
Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
35 Çobanlar kaçamayacak, Sürü başları kurtulamayacak!
Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
36 Duy çobanların haykırışını, Sürü başlarının bağırışını! RAB onların otlaklarını yok ediyor.
Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
37 RAB'bin kızgın öfkesi yüzünden Güvenlikte oldukları ağıllar yok oldu.
Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
38 İnini terk eden genç aslan gibi, RAB inini bıraktı. Zorbanın kılıcı Ve RAB'bin kızgın öfkesi yüzünden Ülkeleri viraneye döndü.
Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.