< Yeremya 19 >

1 RAB bana şöyle dedi: “Git, çömlekçiden bir çömlek satın al. Halkın ve kâhinlerin ileri gelenlerinden birkaçını yanına alıp
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukagule mʼphika wadothi kwa munthu wowumba. Utenge akuluakulu ena a anthuwa ndi ansembe
2 Harsit Kapısı'na yakın Ben-Hinnom Vadisi'ne git. Sana söyleyeceklerimi orada duyur.
ndipo mupite ku Chigwa cha Hinomu chimene chili pafupi ndi pa chipata cha mapale. Pamenepo ukalengeze mawu amene ndikakuwuze.
3 De ki, ‘RAB'bin sözünü dinleyin, ey Yahuda kralları ve Yeruşalim'de yaşayanlar! İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB şöyle diyor: Dinleyin! Buraya, her duyanı şaşkına çevirecek bir felaket göndermek üzereyim.
Ukanene kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu a ku Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu. Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti: Tamverani! Ine ndibweretsa mavuto pa malo pano mwakuti aliyense amene adzamve adzadzidzimuka.
4 Çünkü beni terk ettiler, burayı yabancı bir ülke haline getirdiler. Kendilerinin de atalarıyla Yahuda krallarının da tanımadığı başka ilahlara burada buhur yaktılar, burayı döktükleri suçsuz kanıyla doldurdular.
Pakuti anthu andikana Ine ndipo ayipitsa malo ano. Afukiza lubani pa malo ano kwa milungu imene iwo ngakhale makolo awo ngakhalenso mafumu a ku Yuda sanayidziwe. Iwo adzaza malowa ndi magazi a anthu osalakwa.
5 Çocuklarını ateşte Baal'a kurban etmek için tapınma yerleri kurdular. Böyle bir şey ne buyurdum ne sözünü ettim ne de aklımdan geçirdim.
Amanga nsanja zopembedzerapo Baala, kuperekapo ana awo kuti akhale nsembe zopsereza kwa Baala, chinthu chimene Ine sindinalamule kapena kuchiyankhula, ngakhalenso kuchiganizira.
6 Bundan ötürü buranın artık Tofet ya da Ben-Hinnom Vadisi değil, Kıyım Vadisi diye anılacağı günler geliyor, diyor RAB.
Nʼchifukwa chake taonani, masiku akubwera, akutero Yehova, pamene anthu sadzatchulanso malo ano kuti Tofeti kapena Chigwa cha Hinomu, koma Chophera anthu.
7 Yahuda ve Yeruşalim'in tasarılarını burada boşa çıkaracağım. Onları canlarına susayanların eline verecek, düşmanlarının önünde kılıçla düşüreceğim. Cesetlerini yem olarak yırtıcı kuşlara, yabanıl hayvanlara vereceğim.
“‘Pamalo pano ndidzasokoneza maganizo a anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Ndidzachititsa kuti adani awo awaphe ku nkhondo. Ndidzawakanthitsa kwa anthu amene akuwazonda. Mitembo yawo ndidzayipereka kwa mbalame za mlengalenga ndi zirombo za kutchire kuti ikhale chakudya chawo.
8 Bu kenti viraneye çevirecek, alay konusu edeceğim; oradan her geçen şaşkın şaşkın bakıp başına gelen belalardan ötürü onunla alay edecek.
Mzinda uno ndidzawusakaza ndi kuwusandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyansa. Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo chifukwa cha kuwonongeka kwake.
9 Onlara oğullarının, kızlarının etini yedireceğim. Canlarına susamış düşmanları onları kuşattığında sıkıntıdan birbirlerini yiyecekler.’
Adani awo adzawuzinga mzindawo kufuna kuwapha motero kuti anthu a mʼkatimo adzafika pomadyana wina ndi mnzake. Adzadya ana awo aamuna ndi ana awo aakazi.’
10 “O zaman seninle gidenlerin önünde çömleği kır
“Tsono iwe udzaphwanye mtsukowo anthu amene udzapite nawowo akuona,
11 ve onlara de ki, ‘Her Şeye Egemen RAB şöyle diyor: Çömlekçinin çömleği nasıl kırılıp bir daha onarılamazsa, ben de bu halkı ve bu kenti öyle kıracağım. Ölüleri yer kalmayana dek Tofet'te gömecekler.
ndipo ukawawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti, Ine ndidzaphwanya dziko lino ndi mzinda uno ngati momwe wowumba amaphwanyira mbiya yake ndipo sangathe kuyikonzanso. Adzayika anthu akufa ku Tofeti chifukwa padzasowa malo ena owayika.
12 Bu kente de içinde yaşayanlara da böyle davranacağım, diyor RAB. Bu kenti Tofet gibi yapacağım.
Umu ndi mmene ndidzachitire ndi malo ano pamodzi ndi anthu okhalamo, akutero Yehova. Ndidzasandutsa mzindawu kukhala ngati Tofeti.
13 Yeruşalim'in evleri de Yahuda krallarının sarayları da Tofet gibi kirli sayılacak. Çünkü bu evlerin damlarında gök cisimlerine buhur yaktılar, başka ilahlara dökmelik sunular sundular.’”
Nyumba za mu Yerusalemu ndi za mafumu a ku Yuda ndidzazisandutsa ngati za ku Tofeti chifukwa ndi nyumba zimene pa madenga ake ankafukiza lubani kwa zolengedwa zamlengalenga ndi kuthira nsembe zachakumwa kwa milungu ina.’”
14 Peygamberlik etmesi için RAB'bin Tofet'e gönderdiği Yeremya oradan döndü. RAB'bin Tapınağı'nın avlusunda durup halka şöyle dedi:
Kenaka Yeremiya anabwerako ku Tofeti, kumene Yehova anamutuma kuti akanenere, nakayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Yehova ndi kuwawuza anthu kuti,
15 “İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB diyor ki, ‘İşte bu kente ve çevresindeki köylere sözünü ettiğim bütün felaketleri getireceğim. Çünkü dikbaşlılık edip sözümü dinlemediler.’”
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Tamverani! Ine ndidzabweretsa masautso amene ndinanena aja pa mzinda uno ndi pa mizinda yozungulira, chifukwa anthu ake ndi nkhutukumve ndipo sanamvere mawu anga.’”

< Yeremya 19 >