< Yeremya 11 >
1 RAB Yeremya'ya şöyle seslendi:
Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 “Bu antlaşmanın koşullarını dinle. Yahuda halkına ve Yeruşalim'de yaşayanlara açıkla.
“Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
3 Onlara diyeceksin ki, ‘İsrail'in Tanrısı RAB şöyle diyor: Bu antlaşmanın koşullarına uymayan lanet altındadır!
Awuze kuti Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ‘adzakhala wotembereredwa munthu amene samvera mawu a pangano ili.
4 Atalarınızı Mısır'dan, demir eritme ocağından çıkardığımda bu antlaşmaya bağlı kalmalarını buyurdum. Onlara dedim ki: Sözümü dinleyin, buyurduğum her şeyi yerine getirin. Böylece siz benim halkım olursunuz, ben de sizin Tanrınız olurum.
Awa anali mawu amene ndinalamulira makolo anu nditawatulutsa mu Igupto, kuchoka mʼngʼanjo yamoto.’ Ine ndinati, ‘Mverani Ine ndi kuchita chilichonse chimene ndakulamulirani. Mukatero mudzakhala anthu anga ndi Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
5 İşte o zaman süt ve bal akan ülkeyi –bugün sizin olan ülkeyi– atalarınıza vereceğime ilişkin içtiğim andı yerine getirmiş olacağım.’” “Amin, ya RAB” diye karşılık verdim.
Tsono Ine ndidzakwaniritsa lumbiro lomwe ndinalumbira kwa makolo anu kuti ndidzawapatsa dziko loyenda mkaka ndi uchi,’ dziko lomwe inu lero mukukhalamo.” Tsono Ine ndinayankha kuti, “Ameni, Yehova.”
6 RAB şöyle dedi: “Söyleyeceğim her şeyi Yahuda kentlerinde, Yeruşalim sokaklarında duyur: ‘Bu antlaşmanın koşullarını dinleyin, onlara uyun.
Yehova anandiwuza kuti, “Lengeza mawu onsewa mʼmizinda yonse ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu: ‘Mverani mawu a pangano ili ndi kuzitsatira.
7 Atalarınızı Mısır'dan çıkardığım günden bu yana sözümü dinlemeleri için onları defalarca uyardım.
Kuyambira nthawi imene ndinatulutsa makolo anu ku Igupto mpaka lero, ndakhala ndi kuwachenjeza kawirikawiri kuti, ‘Mverani Ine.’
8 Ama dinlemediler, kulak asmadılar. Bunun yerine kötü yüreklerinin inadı uyarınca davrandılar. Ben de uymalarını buyurduğum, ama uymadıkları bu antlaşmada açıklanan bütün lanetleri başlarına getirdim.’”
Koma sanamvere kapena kulabadirako. Aliyense anawumirira kuchita zoyipa za mʼmitima yawo. Ngakhale ndinawalamulira kuti asunge pangano langa koma iwo sanasunge. Choncho ndinawalanga monga ndinaneneramo.’”
9 RAB bana dedi ki, “Yahuda halkıyla Yeruşalim'de yaşayanlar bana düzen kuruyorlar.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Anthu a ku Yuda ndi ku Yerusalemu andiwukira.
10 Sözlerimi dinlemek istemeyen atalarının suçlarına döndüler. Başka ilahların ardınca gidip onlara taptılar. İsrail halkıyla Yahuda halkı, atalarıyla yaptığım antlaşmayı bozdu.
Abwereranso ku machimo a makolo awo, amene anakana kumvera mawu anga. Akutsata milungu ina ndi kumayitumikira. Aisraeli ndi Ayuda aphwanya pangano limene ndinachita ndi makolo awo.
11 Bu yüzden RAB, ‘Kaçıp kurtulamayacakları bir yıkım getireceğim başlarına’ diyor, ‘Bana yakarsalar da onları dinlemeyeceğim.
Choncho Yehova akuti, ‘Ndidzawagwetsera mavuto amene sadzatha kuwalewa. Ngakhale adzandilirire, sindidzawamvera.
12 Yahuda kentlerinde oturan halk da Yeruşalim'de yaşayanlar da gidip buhur yaktıkları ilahlara yalvaracaklar. Ama yıkım geldiğinde, bu ilahlar onlara yardım edemez.
Anthu a mʼmizinda ya Yuda ndi anthu a ku Yerusalemu adzapita ndi kukalirira milungu imene ankayifukizira lubani, koma milunguyo sidzawathandiza ndi pangʼono pomwe mavuto akadzafika.
13 Kentlerinin sayısı kadar ilahın var, ey Yahuda! O utanılası ilaha, Baal'a buhur yakmak için Yeruşalim sokaklarının sayısı kadar sunak kurdunuz.’
Iwe Yuda, uli ndi milungu yochuluka ngati chiwerengero cha mizinda yako; chiwerengero cha maguwa ansembe amene umafukizirapo lubani kwa Baala chili ngati misewu ya mu Yerusalemu.’
14 “Sana gelince, ey Yeremya, bu halk için yalvarma; ne yakar ne de dilekte bulun. Sıkıntılı zamanlarında beni çağırdıklarında onları dinlemeyeceğim.
“Tsono iwe Yeremiya usawapempherere anthu amenewa ngakhale kuwadandaulira kapena kuwapepesera, chifukwa sindidzawamvera akadzandiyitana pa nthawi ya mavuto awo.
15 “Sevgilim kötü düzenler kuruyor, Öyleyse tapınağımda işi ne? Adaklar ve kutsanmış et uğrayacağın felaketi önleyebilir mi? Felaket gelince sevinecek misin?”
“Kodi anthu anga okondedwa akudzachita chiyani mʼNyumba yanga? Kodi suja iwowa amachita zoyipa zambiri? Kodi mungathe kupulumuka, tsoka osakugwerani chifukwa cha nsembe zanuzo?”
16 RAB sana meyvesi ve biçimi güzel, Yaprağı bol zeytin ağacı adını vermişti. Ama güçlü fırtına koptuğunda Ağacı tutuşturacak; Dalları kırılacak.
Kale Yehova ankakutchani mtengo wa olivi wa masamba obiriwira, wokhala ndi zipatso zokongola. Koma tsopano adzawutentha ndi mkuntho wamkokomo ndipo nthambi zake zidzapserera.
17 Seni dikmiş olan Her Şeye Egemen RAB, Başına felaket getirmeye karar verdi. Çünkü İsrail ve Yahuda halkları Kötülük yaptı, Baal'a buhur yakarak beni öfkelendirdiler.
Yehova Wamphamvuzonse, amene anakudzalani, walamula kuti mavuto akugwereni. Inu a banja la Yuda ndi a banja la Israeli munachitira Yehova zoyipa ndi kumukwiyitsa pamene munkapereka nsembe zanu kwa Baala.
18 Benim için kurdukları düzeni RAB bana açıkladı. Haberim vardı, çünkü ne yaptıklarını bana gösterdi.
Yehova anandiwululira ndipo ndinadziwa. Iye anatsekula maso anga kuti ndione chiwembu chawocho.
19 Kesime götürülen uysal bir kuzu gibiydim. Bana düzen kurduklarını anlamamıştım. Şöyle diyorlardı: “Ağacı da meyvesini de yok edelim, Bir daha adı anılmasın diye Onu yaşayanlar diyarından kesip atalım.”
Ndinali ngati mwana wankhosa wofatsa amene akupita naye kukamupha; sindinkadziwa kuti chiwembu chimene ankakonzekeracho chinkaloza ine. Iwo amati: “Tiyeni timuphe munthu ameneyu kuti dzina lake lisadzakumbukiridwenso.”
20 Adaletle yargılayan, Yüreği ve düşünceyi sınayan, Her Şeye Egemen RAB, Davamı senin eline bırakıyorum. Onlardan alacağın öcü göreyim!
Koma, Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumaweruza molungama ndi kuyesa mitima ndi maganizo, lolani kuti ine ndione kuti mwawalipsira, pakuti mlandu wanga ndawupereka mʼmanja mwanu.
21 “Seni öldürmek isteyen Anatot halkı için RAB diyor ki, ‘Onlar, RAB'bin adına peygamberlik etme, yoksa seni öldürürüz diyorlardı.’
“Nʼchifukwa chake Yehova akunena za anthu a ku Anatoti amene akufuna kuwononga moyo wako namanena kuti, ‘Usanenere mʼdzina la Yehova, ukatero ife tidzakupha ndi manja athu,’
22 Her Şeye Egemen RAB, ‘Onları cezalandıracağım’ diyor, ‘Gençleri kılıçtan geçirilecek, oğullarıyla kızları kıtlıktan ölecek.
koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ine ndidzawalanga. Achinyamata awo adzaphedwa ndi lupanga, ana awo aamuna ndi aakazi adzafa ndi njala.
23 Sağ kalan olmayacak. Cezalandırılacakları yıl Anatot halkının başına felaket getireceğim.’”
Sipadzakhala otsala ndi mmodzi yemwe, chifukwa ndidzalanga anthu a ku Anatoti chikadzafika chaka chawo cha chilango.’”