< Yeşaya 8 >

1 RAB bana şöyle dedi: “Büyük bir levha alıp okunaklı harflerle üzerine, ‘Maher-Şalal-Haş-Baz’ yaz.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Kâhin Uriya ile Yeverekya oğlu Zekeriya'yı kendime güvenilir tanık seçiyorum.”
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 Peygamber olan karım bundan bir süre sonra gebe kaldı ve bir erkek çocuk doğurdu. RAB bana, “Adını ‘Maher-Şalal-Haş-Baz’ koy” dedi,
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 “Çocuk daha ‘Anne, baba’ demesini öğrenmeden, Şam'ın serveti ve Samiriye'nin ganimeti Asur Kralı'na götürülecek.”
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 RAB bana yine seslenip dedi ki,
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 “Bu halk usul usul akan Şiloah sularını reddettiği, Resin'le Remalya'nın oğluyla mutlu olduğu için,
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 ben Rab, Fırat'ın kabaran güçlü sularını –bütün dehşetiyle Asur Kralı'nı– üzerlerine salacağım. Yatağından taşan ırmak, kıyılarını su altında bırakacak.
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 Yahuda'yı kaplayan sular her şeyi silip süpürerek adam boyu yükselecek, ülkeni boydan boya dolduracak, ey İmmanuel!”
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Ey halklar, yıkıma, bozguna uğrayacaksınız. Yeryüzünün en uç köşeleri, kulak verin. Savaşmaya, bozguna uğramaya hazırlanın. Evet, savaşa ve bozguna hazır olun.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 İstediğinizi tasarlayın, hepsi boşa gidecek. İstediğiniz kadar konuşun, hiçbiri gerçekleşmeyecek. Çünkü Tanrı bizimledir.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 RAB beni halkın tuttuğu yoldan gitmeme konusunda şiddetle uyararak şöyle dedi:
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 “Onların entrika dediği her şeye Siz entrika demeyin; Onların korktuğundan korkmayın, yılmayın.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 “Her Şeye Egemen RAB'bi kutsal sayın. Korkunuz, yılgınız O'ndan olsun.
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 Tapınak O olacak. İsrail'in iki krallığı içinse Sürçme taşı ve tökezleme kayası, Yeruşalim'de yaşayanlar için Kapan ve tuzak olacak.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 Birçokları sendeleyip düşecek, parçalanacak, Tuzağa düşüp ele geçecek.”
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Ya RAB, öğrencilerim arasında bildirimi koru, Öğretimi mühürle!
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 Kendini Yakup'un soyundan gizleyen RAB'bi özlemle bekliyorum, umudum O'nda.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Ben ve RAB'bin bana verdiği çocuklar, Siyon Dağı'nda oturan Her Şeye Egemen RAB'bin İsrail'deki belirtileri ve işaretleriyiz.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 Birileri size, “Fısıldaşıp mırıldanan medyumlarla ruh çağıranlara danışın” dediğinde, “Halk kendi Tanrısı'na danışmaz mı; yaşayanlar için ölülere mi danışılır?” deyin.
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 Tanrı'nın öğretisine ve bildirisine dönmek gerek! Böyle düşünmezlerse, onlar için hiç şafak sökmeyecek.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 Aç ve çaresiz, ülkede dolanıp duracaklar. Aç kalınca öfkelenip krallarına, Tanrıları'na lanet edecekler. Yukarıya da
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 dünyaya da baksalar sıkıntıdan, karanlıktan, korkunç karanlıktan başka bir şey görmeyecekler. Kovulacakları yer koyu karanlıktır.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Yeşaya 8 >