< Yeşaya 63 >
1 Edom'dan, Bosra'dan Al giysiler içinde bu gelen kim? Göz kamaştırıcı giysiler içinde, Büyük güçle yürüyen kim? “O benim! Adaleti duyuran, Kurtarmaya gücü olan.”
Kodi ndani uyo akubwera kuchokera ku Edomu, atavala zovala za ku Bozira za madontho ofiira? Kodi uyu ndani, amene wavala zovala zokongola, akuyenda mwa mphamvu zake? “Ndi Ineyo, woyankhula zachilungamo ndiponso wamphamvu zopulumutsa.”
2 Giysilerin neden kırmızı? Üstün başın neden çukurda üzüm çiğneyen biri gibi kızıla bulanmış?
Nanga bwanji zovala zanu zili psuu, ngati za munthu wofinya mphesa?
3 “Çukurda üzümü tek başıma çiğnedim, Yanımda halklardan kimse yoktu. Öfkeyle çiğnedim onları, Gazapla ayaklarımın altına aldım. Kanları giysilerime sıçradı, bütün elbisemi kirletti.
“Ndapondereza ndekha anthu a mitundu ina ngati mphesa, palibe ndi mmodzi yemwe anali nane. Ndinawapondereza ndili wokwiya ndipo ndinawapondereza ndili ndi ukali; magazi awo anadothera pa zovala zanga, ndipo zovala zanga zonse zinathimbirira.
4 Çünkü öç alma günü yüreğimdeydi, Halkımı kurtaracağım yıl gelmişti.
Pakuti ndinatsimikiza mu mtima mwanga kuti lafika tsiku lolipsira anthu anga; ndipo chaka cha kuwomboledwa kwanga chafika.
5 Baktım, yardım edecek kimse yoktu, Destek verecek kimsenin olmayışına şaştım; Gücüm kurtuluş sağladı, Gazabım bana destek oldu.
Ndinayangʼana ndipo panalibe munthu wondithandiza. Ndinadabwa kwambiri kuti panalibe wondichirikiza; choncho ndinapambana ndi mphamvu zanga, ndipo mkwiyo wanga unandilimbitsa.
6 Öfkeyle halkları çiğnedim, Onları gazapla sarhoş ettim, Yere akıttım kanlarını.”
Ndinapondereza mitundu ya anthu ndili wokwiya; ndipo ndinawasakaza ndipo ndinathira magazi awo pansi.”
7 Şefkati ve iyiliği uyarınca Bizim için yaptıklarından, evet, İsrail halkı için yaptığı bütün iyiliklerinden ötürü RAB'bin iyiliklerini ve övülesi işlerini anacağım.
Ndidzafotokoza za kukoma mtima kwa Yehova, ntchito zimene Iye ayenera kutamandidwa. Ndidzatamanda Yehova chifukwa cha zonse zimene watichitira. Inde, mwa chifundo ndi kukoma mtima kwake Yehova wachitira nyumba ya Israeli zinthu zabwino zambiri.
8 RAB dedi ki, “Onlar kuşkusuz benim halkım, Beni aldatmayacak çocuklardır.” Böylece onların Kurtarıcısı oldu.
Yehova anati, “Ndithu awa ndi anthu anga, ana anga amene sadzandinyenga Ine.” Choncho anawapulumutsa.
9 Sıkıntı çektiklerinde O da sıkıntı çekti. Huzurundan çıkan melek onları kurtardı. Sevgisi ve merhametinden ötürü onları kurtardı, Geçmişte onları sürekli yüklenip taşıdı.
Iyenso anasautsidwa mʼmasautso awo onse, ndipo mngelo wochokera kwa Iye anawapulumutsa. Mwa chikondi ndi chifundo chake iye anawapulumutsa, anawanyamula ndikuwatenga kuyambira kale lomwe.
10 Ama başkaldırıp O'nun Kutsal Ruhu'nu incittiler. O da düşmanları olup onlara karşı savaştı.
Komabe iwo anawukira ndi kumvetsa chisoni Mzimu Woyera. Motero Yehova anatembenuka nakhala mdani wawo ndipo Iye mwini anamenyana nawo.
11 Sonra halkı eski günleri, Musa'nın dönemini anımsadı. “Çobanlarıyla birlikte onları denizden geçiren, Kutsal Ruhu'nu aralarına yerleştiren, Görkemli gücüyle Musa'nın sağında yol alan, Sonsuz onur kazanmak için önlerinde suları yaran, Bir at nasıl tökezlemeden kırdan geçerse Onları deniz yatağından öyle geçiren RAB nerede?” Diye sordular.
Pamenepo anthu ake anakumbukira masiku amakedzana, masiku a Mose mtumiki wake; ndipo anafunsa kuti, “Ali kuti Yehova amene anawawolotsa pa nyanja, pamodzi ndi Mose mʼbusa wawo? Ali kuti Iye amene anayika Mzimu Woyera pakati pawo?
Ali kuti amene anachita zinthu zodabwitsa ndi mphamvu zake zazikulu kudzera mwa Mose? Ali kuti amene anagawa madzi pa nyanja anthu ake akuona, kuti dzina lake limveke mpaka muyaya,
amene anawayendetsa pa nyanja yozama? Monga kavalo woyendayenda mʼchipululu, iwo sanapunthwe;
14 Ovaya götürülen sürü gibi RAB'bin Ruhu onları rahata kavuşturdu. İşte adını onurlandırmak için Halkına böyle yol gösterdi.
Mzimu Woyera unawapumulitsa ngati mmene ngʼombe zimapumulira. Umu ndi mmene Inu munatsogolera anthu anu kuti dzina lanu lilemekezeke.”
15 Ya RAB, gökten bak, Kutsal, görkemli ve yüce yerinden bizi gör! Gayretin, gücün nerede? Gönlündeki özlem ve merhameti Bizden esirgedin.
Inu Yehova amene muli kumwambako, pa mpando wanu wolemekezeka, wopatulika ndi waulemerero, tiyangʼaneni ife. Kodi changu chanu ndi mphamvu zanu zili kuti? Simukutionetsanso kukoma mtima kwanu ndi chifundo chanu.
16 Babamız sensin. İbrahim bizi tanımasa da, İsrail bizi kabul etmese de, Babamız'sın, ya RAB, Ezelden beri adın “Kurtarıcımız”dır.
Koma Inu ndinu Atate athu, ngakhale Abrahamu satidziwa kapena Israeli kutivomereza ife; Inu Yehova, ndinu Atate athu, kuyambira kale dzina lanu ndinu Mpulumutsi wathu.
17 Ya RAB, neden bizi yolundan saptırıyor, İnatçı kılıyor, Senden korkmamızı engelliyorsun? Kulların uğruna, Mirasın olan oymakların uğruna geri dön.
Chifukwa chiyani, Inu Yehova, mukutisocheretsa pa njira zanu? Bwanji mukutilola kuti tikhale owuma mitima kotero kuti sitikukuopaninso? Bwererani chifukwa cha atumiki anu; mafuko a anthu amene ali cholowa chanu.
18 Kutsal halkın kısa süre tapınağına sahip oldu, Ama düşmanlarımız onu çiğnedi.
Anthu anu atangokhala pa malo anu opatulika pa kanthawi kochepa, adani athu anasakaza malo anu opatulika.
19 Öteden beri yönetmediğin, Sana ait olmayan bir halk gibi olduk.
Ife tili ngati anthu amene simunawalamulirepo ngati iwo amene sanakhalepo anthu anu.