< Yeşaya 62 >

1 Zaferi ışık gibi parlayıncaya, Kurtuluşu meşale gibi yanıncaya dek Siyon uğruna susmayacak, Yeruşalim uğruna sessiz kalmayacağım.
Chifukwa chokonda Ziyoni sindidzakhala chete, chifukwa chokonda Yerusalemu sindidzakhala chete, mpaka chilungamo chake chitaoneka poyera ngati kuwala, ndi chipulumutso chake chitaoneka ngati sakali yoyaka.
2 Uluslar senin zaferini, Bütün krallar görkemini görecek. RAB'bin kendi ağzıyla belirlediği yeni bir adla anılacaksın.
Mitundu ya anthu idzaona iwe utapambana pa nkhondo ndipo mafumu onse adzaona ulemerero wako. Adzakuyitanira dzina latsopano limene adzakupatse ndi Yehova.
3 RAB'bin elinde güzellik tacı, Tanrın'ın elinde krallık sarığı olacaksın.
Udzakhala ngati chipewa chaulemerero mʼdzanja la Yehova, ndi ngati nduwira yaufumu mʼdzanja la Mulungu wako.
4 Artık sana “Terk edilmiş”, Ülkene “Virane” denmeyecek; Bunun yerine sana “Sevdiğim”, Ülkene “Evli” denecek. Çünkü RAB seni seviyor, Ülken de evli sayılacak.
Sadzakutchanso “Wosiyidwa,” ndipo dziko lako silidzatchedwanso “Chipululu.” Koma dzina lako latsopano lidzakhala “Ndakondwera naye.” Ndipo dziko lako lidzatchedwa “Wokwatiwa.” Chifukwa Yehova akukondwera nawe, ndipo adzakhala ngati mwamuna wa dziko lako.
5 Bir delikanlı bir kızla nasıl evlenirse, Oğulların da seninle öyle evlenecek. Güvey gelinle nasıl sevinirse, Tanrın da seninle öyle sevinecek.
Monga mnyamata amakwatira namwali, momwenso mmisiri wodzakumanga adzakukwatira; monga mkwati amakondwera ndi mkwatibwi, chonchonso Mulungu adzakondwera nawe.
6 Ey Yeruşalim, surlarına bekçiler diktim, Gece gündüz hiç susmayacaklar. Ey RAB'be sözünü anımsatanlar, Yeruşalim'i pekiştirene, Onu yeryüzünün övüncü kılana dek Durup dinlenmeden RAB'be yakarın, O'na rahat vermeyin.
Iwe Yerusalemu, pa malinga ako ndayikapo alonda; sadzakhala chete usana kapena usiku. Inu amene mumakumbutsa Yehova za malonjezo ake musapumule.
7
Musamupatse mpata wopuma mpaka atakhazikitsa Yerusalemu kukhala mzinda umene dziko lapansi lidzawutamande.
8 RAB sağ elini, güçlü kolunu kaldırıp ant içti: “Tahılını bir daha düşmanlarına yedirmeyeceğim, Emek verdiğin yeni şarabı yabancılar içmeyecek.
Yehova analumbira atakweza dzanja lake. Anati, “Sindidzaperekanso tirigu wako kuti akhale chakudya cha adani ako, ndipo alendo sadzamwanso vinyo wako watsopano pakuti unamuvutikira.
9 Tahılı devşiren yiyecek Ve RAB'be övgüler sunacak. Üzümü toplayan, Şarabını kutsal avlularımda içecek.”
Koma amene amakakolola ndiwo amene adzadye buledi ndi kutamanda Yehova, ndipo amene amasonkhanitsa pamodzi mphesa ndiwo amene adzamwe vinyo mʼmabwalo a Nyumba yanga.”
10 Geçin, geçin kent kapılarından! Halkın yolunu açın! Toprak yığıp yol yapın, Taşları ayıklayın, uluslar için sancak dikin!
Tulukani, dutsani pa zipata! Konzerani anthu njira. Lambulani, lambulani msewu waukulu! Chotsani miyala. Kwezani mbendera kuti mitundu ya anthu izione.
11 RAB çağrısını dünyanın dört bucağına duyurdu: “Siyon kızına, ‘İşte kurtuluşun geliyor’ deyin, ‘Ücreti kendisiyle birlikte, ödülü önündedir.’”
Yehova walengeza ku dziko lonse lapansi kuti, Awuzeni anthu a ku Yerusalemu kuti, “Taonani, chipulumutso chanu chikubwera; Yehova akubwera ndi mphotho yake akubwera nazo zokuyenerani.”
12 Siyon halkına, “RAB'bin fidyeyle kurtardığı kutsal halk” diyecekler. Ve sen Yeruşalim, “Aranan, terk edilmemiş kent” diye anılacaksın.
Iwo adzatchedwa Anthu Opatulika, owomboledwa a Yehova; ndipo adzakutchani “Okondwa a Yehova” “Mzinda umene Yehova sanawusiye.”

< Yeşaya 62 >