< Yeşaya 60 >
1 “Kalk, parla; Çünkü Işığın geliyor, RAB'bin yüceliği üzerine doğuyor.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Dünyayı karanlık, halkları koyu karanlık örtüyor; Oysa RAB senin üzerine doğacak, Yüceliği üzerinde görünecek.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Uluslar senin Işığına, Krallar üzerine doğan aydınlığa gelecek.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 “Başını kaldır da çevrene bir bak, Hepsi toplanmış sana geliyor. Oğulların uzaktan geliyor, Kızların kucakta taşınıyor.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Bunu görünce yüzün parlayacak, Yüreğin heyecandan hızlı hızlı çarpacak; Çünkü denizin zenginlikleri senin olacak, Ulusların serveti sana akacak.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 “Deve sürüleri, Midyan'ın ve Efa'nın deve yavruları Senin topraklarını dolduracak. Bütün Saba halkı geliyor, Altın ve günnük getiriyor, RAB'bin erdemlerini ilan ediyorlar.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Kedar'ın bütün sürüleri sana gelecek, Nevayot'un koçları senin buyruğunda olacak, Sunağımın üzerinde kabul edilen sunular olarak sunulacak. Böylece görkemli tapınağımı daha görkemli kılacağım.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 “Nedir bunlar, bulut gibi, Yuvalarına yaklaşan güvercinler gibi süzülüp gelenler?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Bana umut bağlayan kıyı halklarının, Ticaret gemileri öncülüğünde Senin çocuklarını altınlarıyla, gümüşleriyle birlikte Tanrın RAB'bin adı için, İsrail'in Kutsalı için Uzaktan getiren gemileridir bunlar. RAB seni görkemli kıldı.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 “Yabancılar senin surlarını onaracak, Kralları sana hizmet edecek. Öfkelendiğimde seni cezalandırdıysam da, Kabul ettiğimde sana merhamet göstereceğim.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Kapıların hep açık duracak, Ulusların serveti ve zafer alayları ardında yürütülen yenik krallar Gece gündüz açık kalan bu kapılardan girsin diye.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Çünkü sana kulluk etmeyen ulus ya da krallık yok olacak, Evet, o uluslar tam bir yıkıma uğrayacak.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 “Lübnan'ın görkemi olan çam, köknar ve selvi ağaçları, Tapınağımı süslemek için hep birlikte sana taşınacak. Ayak bastığım yeri görkemli kılacağım.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Seni ezenlerin çocukları Gelip önünde eğilecekler; Seni hor görenlerin hepsi, ‘RAB'bin kenti, İsrail'in Kutsalı'nın Siyon'u’ Diyerek ayaklarına kapanacaklar.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 “Kimsenin uğramadığı, terk edilmiş, Nefret edilen bir yer olduğun halde Seni sonsuz bir övünç kaynağı, Bütün kuşakların sevinci kılacağım.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Uluslar ve krallıklar Bir anne gibi seni emzirecekler. O zaman bileceksin ki, seni kurtaran RAB, Seni fidyeyle kurtaran, Yakup'un Güçlüsü benim.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Sana tunç yerine altın, Demir yerine gümüş, ağaç yerine tunç, Taş yerine demir getireceğim. Barışı yöneticin, doğruluğu önderin yapacağım.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 Ülkenden şiddet, sınır boylarından Soygun ve yıkım haberleri duyulmayacak artık. Surlarına Kurtuluş, kapılarına Övgü adını vereceksin.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 “Gündüz ışığın güneş olmayacak artık, Ay da aydınlatmayacak seni; Çünkü RAB sonsuz ışığın, Tanrın görkemin olacak.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Artık güneşin batmayacak, ayın çekilmeyecek, Çünkü RAB sonsuz ışığın olacak, Sona erecek yas günlerin.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Halkının hepsi doğru kişiler olacak; El emeğim, görkemimi göstermek için diktiğim fidan, Ülkeyi sonsuza dek mülk edinecek.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 En küçük ailen bini bulacak, Sayıca en az olanı koca bir ulus olacak. Ben RAB, zamanı gelince bunu hızlandıracağım.”
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”