< Yeşaya 6 >

1 Kral Uzziya'nın öldüğü yıl yüce ve görkemli Rab'bi gördüm; tahtta oturuyordu, giysisinin etekleri tapınağı dolduruyordu.
Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova.
2 Üzerinde Seraflar duruyordu; her birinin altı kanadı vardı; ikisiyle yüzlerini, ikisiyle ayaklarını örtüyor, öbür ikisiyle de uçuyorlardı.
Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira.
3 Birbirlerine şöyle sesleniyorlardı: “Her Şeye Egemen RAB Kutsal, kutsal, kutsaldır. Yüceliği bütün dünyayı dolduruyor.”
Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti “Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse. Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”
4 Seraflar'ın sesinden kapı söveleriyle eşikler sarsıldı, tapınak dumanla doldu.
Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.
5 “Vay başıma! Mahvoldum” dedim, “Çünkü dudakları kirli bir adamım, dudakları kirli bir halkın arasında yaşıyorum. Buna karşın Kral'ı, Her Şeye Egemen RAB'bi gözlerimle gördüm.”
Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”
6 Seraflar'dan biri bana doğru uçtu, elinde sunaktan maşayla aldığı bir kor vardı;
Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe.
7 onunla ağzıma dokunarak, “İşte bu kor dudaklarına değdi, suçun silindi, günahın bağışlandı” dedi.
Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”
8 Sonra Rab'bin sesini işittim: “Kimi göndereyim? Bizim için kim gidecek?” diyordu. “Ben! Beni gönder” dedim.
Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?” Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”
9 “Git, bu halka şunu duyur” dedi, “‘Duyacak duyacak, ama anlamayacaksınız, Bakacak bakacak, ama görmeyeceksiniz!
Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa: “‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa; kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’
10 Bu halkın yüreğini duygusuzlaştır, Kulaklarını ağırlaştır, Gözlerini kapat. Öyle ki, gözleri görmesin, Kulakları duymasın, yürekleri anlamasın Ve bana dönüp şifa bulmasınlar.’”
Tsono anthu amenewa uwaphe mtima; uwagonthetse makutu, ndipo uwatseke mʼmaso. Mwina angaone ndi maso awo, angamve ndi makutu awo, angamvetse ndi mitima yawo, kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”
11 “Ne vakte kadar, ya Rab?” diye sordum. Rab yanıtladı: “Kentler viraneye dönüp kimsesiz kalıncaya, Evler ıpıssız oluncaya, Toprak büsbütün kıraçlaşıncaya kadar.
Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?” Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti, “Mpaka mizinda itasanduka mabwinja nʼkusowa wokhalamo, mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo, mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,
12 İnsanları çok uzaklara süreceğim, Ülke bomboş kalacak,
mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali, dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.
13 Halkın onda biri kalsa da ülke mahvolacak. Ama devrildiği zaman kütüğü kalan Yabanıl fıstık ve meşe ağacı gibi, Kutsal soy kütüğünden çıkacak.”
Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko, nachonso chidzawonongedwa. Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu imasiyira chitsa pamene ayidula, chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”

< Yeşaya 6 >