< Yeşaya 57 >

1 Doğru kişi ölüp gidiyor, Kimsenin umurunda değil. Sadık adamlar da göçüp gidiyor; Kimse doğru kişinin göçüp gitmekle Kötülükten kurtulduğunun farkında değil.
Anthu olungama amafa, ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake; anthu odzipereka amatengedwa, ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake. Anthu olungama amatengedwa kuti tsoka lisawagwere.
2 Doğru kişi esenliğe kavuşur, Doğru yolda yürümüş olan mezarında rahat uyur.
Iwo amene amakhala moyo wolungama amafa mwamtendere; amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.
3 Ama siz, ey falcı kadının çocukları, Fahişelik ve zina edenlerin soyu, buraya gelin!
“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa, inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
4 Siz kiminle alay ediyorsunuz? Kime dudak büküyor, dil çıkarıyorsunuz? Ağaçlar arasında, bol yapraklı her ağacın altında Şehvetle yanıp tutuşan, Vadilerde, kaya kovuklarında çocuklarını kurban eden, İsyan torunları, yalan soyu değil misiniz siz?
Kodi inu mukuseka yani? Kodi mukumunena ndani ndi kupotoza pakamwa panu? Kodi inu si ana owukira, zidzukulu za anthu abodza?
5
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu, ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri. Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
6 Sizin payınız Vadinin düzgün taşlarından yapılan putlardır, Evet, sizin nasibiniz onlardır! Onlara dökmelik sunular döktünüz, Tahıl sunuları sundunuz. Bütün bunlardan sonra sizi cezalandırmaktan çekineceğimi mi sanıyorsunuz?
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu. Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo, ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya. Kodi zimenezi zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
7 Yatağınızı ulu, yüksek dağa serdiniz, Oraya bile kurban kesmeye gidiyorsunuz.
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali. Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
8 Kapılarınızın, sövelerinizin arkasına İğrenç simgeler koydunuz. Beni bıraktınız, Yataklarınızı ardına kadar açıp içine girdiniz, Oynaşlarınızla anlaşıp birlikte yatmaya can atıyorsunuz. Onların çıplaklığını seyrettiniz.
Mʼnyumba mwanu mwayika mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu. Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu. Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu, ndiye mwazilipira kuti mugone nazo. Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
9 Çeşit çeşit hoş kokular sürünüp ilah Molek'e yağ götürdünüz. Elçilerinizi ta uzaklara gönderdiniz, Ölüler diyarına dek alçalttınız kendinizi. (Sheol h7585)
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta ndi zonunkhira zochuluka. Munachita kutumiza akazembe anu kutali; inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko! (Sheol h7585)
10 Uzun yolculuklar sizi yorduğu halde, “Pes ettim” demediniz. Gücünüzü tazeleyip durdunuz, Bu nedenle de tükenmediniz.
Inu mumatopa ndi maulendo anu, koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’ Munapezako kumeneko zokhumba zanu nʼchifukwa chake simunalefuke.
11 “Sizi kaygılandıran, korkutan kim ki, Bana ihanet ediyor, beni anmıyor, Yüreğinizde bana yer vermiyorsunuz? Benden korkmamanızın nedeni Uzun zamandır suskun kalışım değil mi?
“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa, kotero kuti mwakhala mukundinamiza, ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe, kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine? Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Sözde doğruluğunuzu da yaptıklarınızı da ilan edeceğim, Bunların size yararı olmayacak.
Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama, ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Feryat ettiğinizde Topladığınız putlar sizi kurtarsın bakalım! Rüzgar hepsini silip süpürecek, Bir soluk onları alıp götürecek. Bana sığınansa ülkeyi mülk edinecek, Kutsal dağımı miras alacak.”
Pamene mufuwula kupempha thandizo, mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni! Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo, mpweya chabe udzawulutsa mafanowo. Koma munthu amene amadalira ine adzalandira dziko lokhalamo. Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”
14 RAB diyor ki, “Toprak yığıp yol yapın, Halkımın yolundaki engelleri kaldırın.”
Ndipo panamveka mawu akuti, “Undani, undani, konzani msewu! Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Yüce ve görkemli Olan, Sonsuzlukta yaşayan, adı Kutsal Olan diyor ki, “Yüksek ve kutsal yerde yaşadığım halde, Alçakgönüllülerle, ezilenlerle birlikteyim. Yüreklerini sevindirmek için ezilenlerin yanındayım.
Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse, amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo, akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika, koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Çünkü sonsuza dek davacı ve öfkeli olacak değilim, Öyle olsa, yarattığım canlarla ruhlar karşımda dayanamazdı.
Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya kapena kuwapsera mtima nthawi zonse, popeza kuti ndinalenga anthu anga ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Haksız kazanç suçuna öfkelenip halkı cezalandırdım, Öfkeyle yüzümü çevirdim onlardan. Ne var ki, inatla kendi yollarından gittiler.
Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera; ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya, koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 “Yaptıklarını gördüm, Ama onları iyileştirip yol göstereceğim. Karşılık olarak hem onları Hem de aralarında yas tutanları avutacağım.
Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa; kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19 Dudaklardan övgü sözleri döktüreceğim. Uzaktakine de yakındakine de Tam esenlik olsun” diyor RAB, “Hepsini iyileştireceğim.”
anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo. Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,” “Ndipo ndidzawachiritsa.” Akutero Yehova.
20 Ama kötüler çalkalanan deniz gibidir, O deniz ki, rahat duramaz, suları çamur ve pislik savurur.
Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka, yosatha kukhala bata, mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 “Kötülere esenlik yoktur” diyor Tanrım.
“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

< Yeşaya 57 >