< Yeşaya 54 >

1 “Çocuk doğurmayan ey kısır kadın, Sevinç çığlıkları at; Ey doğum ağrısı nedir bilmeyen sen, Sevinçle haykır, bağır. Çünkü terk edilmiş kadının, Evli kadından daha çok çocuğu olacaktır” diyor RAB.
“Sangalala, iwe mayi wosabala, iwe amene sunabalepo mwana; imba nyimbo, ndi kufuwula mwachimwemwe, iwe amene sunamvepo ululu wa pobereka; chifukwa mkazi wosiyidwa adzakhala ndi ana ambiri kuposa mkazi wokwatiwa,” akutero Yehova.
2 “Çadırının alanını genişlet, Perdelerini uzat, çekinme. Gergi iplerini de uzat, kazıklarını sağlamlaştır.
Kulitsa malo omangapo tenti yako, tambasula kwambiri nsalu zake, usaleke; talikitsa zingwe zako, limbitsa zikhomo zako.
3 Çünkü sağa sola yayılacaksın, Soyundan gelenler ulusları mülk edinecek, Issız kentlere yerleşecek.
Pakuti udzasendeza malire ako kumanja ndi kumanzere; ndipo zidzukulu zako zidzalanda dziko la anthu a mitundu ina ndipo zidzakhala mʼmizinda yawo yosiyidwa.
4 “Korkma, ayıplanmayacaksın, Utanma, aşağılanmayacaksın. Unutacaksın gençliğinde yaşadığın utancı, Dulluk ayıbını artık anmayacaksın.
“Usachite mantha; sadzakunyozanso. Usakhumudwe; sudzapeputsidwanso. Udzayiwala za manyazi zimene zinakuchitikira nthawi ya unyamata wako ndipo za manyazi zimene zinakuchitikira pa nthawi ya umasiye wako sudzazikumbukanso.
5 Çünkü kocan, seni yaratandır. O'nun adı Her Şeye Egemen RAB'dir, İsrail'in Kutsalı'dır seni kurtaran. O'na bütün dünyanın Tanrısı denir.”
Pakuti Mlengi wako ali ngati mwamuna wako, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse. Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wanu; dzina lake ndi Mulungu wa dziko lonse lapansi.
6 Tanrın diyor ki, “RAB seni terk edilmiş, Ruhu kederli bir kadın, Genç yaşta evlenip sonra dışlanmış Bir kadın olarak çağırıyor:
Yehova wakuyitananso, uli ngati mkazi wosiyidwa ndi wodzaza ndi chisoni mu mtima, mkazi amene anakwatiwa pa unyamata wake kenaka nʼkukanidwa,” akutero Mulungu wako.
7 ‘Bir an için seni terk ettim, Ama büyük sevecenlikle geri getireceğim.
“Kwa kanthawi kochepa, Ine ndinakusiya, koma ndidzakutenganso chifukwa ndimakukonda kwambiri.
8 Bir anlık taşkın öfkeyle senden yüz çevirmiştim, Ama sonsuz sadakatle sana sevecenlik göstereceğim.’” Seni kurtaran RAB böyle diyor.
Ndinakufulatira kwa kanthawi kochepa ndili wokwiya kwambiri. Koma ndi kukoma mtima kwanga kwa muyaya, ndidzakuchitira chifundo,” akutero Yehova Mpulumutsi wako.
9 “Bu benim için Nuh tufanı gibidir. Nuh tufanının bir daha yeryüzünü Kaplamayacağına nasıl ant içtimse, Sana öfkelenmeyeceğime, Seni azarlamayacağıma da ant içiyorum.
“Kwa ine zimenezi zili ngati mmene zinalili mʼnthawi ya Nowa. Monga ndinalumbira nthawi imeneyo kuti sindidzawononganso dziko lapansi ndi madzi. Kotero tsopano ndalumbira kuti sindidzakupseraninso mtima, sindidzakudzudzulaninso.
10 Dağlar yerinden kalksa, tepeler sarsılsa da Sadakatim senin üzerinden kalkmaz, Esenlik antlaşmam sarsılmaz” Diyor sana merhamet eden RAB.
Ngakhale mapiri atagwedezeka ndi zitunda kusunthidwa, koma chikondi changa chosasinthika pa iwe sichidzatha. Pangano langa lamtendere silidzasintha,” akutero Yehova amene amakuchitira chifundo.
11 “Ey kasırgaya tutulmuş, Avuntu bulmamış ezik kent! Taşlarını koyu harçla yerine koyacak, Temellerini laciverttaşıyla atacağım.
“Iwe mzinda wozunzika, wokunthidwa ndi namondwe ndiponso wopanda wokutonthoza, Ine ndidzakongoletsa miyala yako. Maziko ako ndidzamanga ndi miyala ya safiro.
12 Kale burçlarını yakuttan, Kapılarını mücevherden, Surlarını değerli taşlardan yapacağım.
Ndidzamanga nsanja zako zankhondo ndi miyala yokongola ya rubi. Ndidzamanga zipata zako ndi miyala yonyezimira ngati moto, ndipo linga lako lonse lidzakhala la miyala yamtengowapatali.
13 Bütün çocuklarını ben RAB eğiteceğim, Esenlikleri tam olacak.
Yehova adzaphunzitsa ana ako onse, ndipo ana ako adzakhala ndi mtendere wochuluka.
14 Doğrulukla güçlenecek, Baskıdan uzak olacak, korkmayacaksın. Dehşet senden uzak kalacak, sana yaklaşmayacak.
Udzakhazikika mʼchilungamo chenicheni: Sudzakhalanso wopanikizika, chifukwa sudzaopa kanthu kalikonse. Sudzakhalanso ndi mantha chifukwa manthawo sadzafika pafupi ndi iwe.
15 Sana saldıran olursa, benden olmadığını bil. Sana saldıran herkes önünde yenilgiye uğrayacak.
Ngati wina adzakuthirani nkhondo, si ndine amene ndachititsa; aliyense amene adzalimbana nanu adzagonja chifukwa cha iwe.
16 “İşte, kor halindeki ateşi üfleyen, Amaca uygun silah yapan demirciyi ben yarattım. Yok etsin diye yıkıcıyı da ben yarattım.
“Taona, ndi Ine amene ndinalenga munthu wosula zitsulo amene amakoleza moto wamakala ndi kusula zida zoti azigwiritse ntchito. Ndipo ndine amene ndinalenga munthu wosakaza kuti awononge;
17 Ama sana karşı yapılan hiçbir silah işe yaramayacak, Mahkemede seni suçlayan her dili Suçlu çıkaracaksın. RAB'be kulluk edenlerin mirası şudur: Onların gönenci bendendir” diyor RAB.
palibe chida chopangidwa ndi mdani chimene chidzakupweteke, ndipo onse okuneneza pa mlandu udzawatsutsa. Umu ndimo adzapezekere atumiki a Yehova. Chipambano chawo chichokera kwa Ine,” akutero Yehova.

< Yeşaya 54 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark