< Yeşaya 53 >

1 Verdiğimiz habere kim inandı? RAB'bin gücü kime açıklandı?
Ndani wakhulupirira zimene tanenazi; kapena ndani amene Yehova wamuzindikiritsa mphamvu zake?
2 O RAB'bin önünde bir fidan gibi, Kurak yerdeki kök gibi büyüdü. Bakılacak biçimden, güzellikten yoksundu. Gönlümüzü çeken bir görünüşü de yoktu.
Iye anakula ngati mphukira pamaso pake, ndiponso ngati muzu mʼnthaka yowuma. Iye analibe thupi labwino kapena nkhope yokongola yoti ife nʼkumamuchewukira, analibe maonekedwe woti ife nʼkumamukhumbira.
3 İnsanlarca hor görüldü, Yapayalnız bırakıldı. Acılar adamıydı, hastalığı yakından tanıdı. İnsanların yüz çevirdiği biri gibi hor görüldü, Ona değer vermedik.
Iye ananyozedwa ndi kukanidwa ndi anthu, munthu amene moyo wake unali wamasautso, wozolowera zowawa, ndipo anali ngati munthu amene anzake amaphimba nkhope zawo akamuona. Iye ananyozedwa, ndipo ife sitinamuyese kanthu.
4 Aslında hastalıklarımızı o üstlendi, Acılarımızı o yüklendi. Bizse Tanrı tarafından cezalandırıldığını, Vurulup ezildiğini sandık.
Ndithudi, iye anamva zowawa mʼmalo mwa ife; ndipo anasautsidwa mʼmalo mwathu. Koma ife tinkaganiza kuti ndi Mulungu amene akumulanga, kumukantha ndi kumusautsa.
5 Oysa, bizim isyanlarımız yüzünden onun bedeni deşildi, Bizim suçlarımız yüzünden o eziyet çekti. Esenliğimiz için gerekli olan ceza Ona verildi. Bizler onun yaralarıyla şifa bulduk.
Koma iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, ndipo anamuzunza chifukwa cha zoyipa zathu; iye analangidwa kuti ife tikhale ndi mtendere, ndipo ndi mabala ake ife tinachiritsidwa.
6 Hepimiz koyun gibi yoldan sapmıştık, Her birimiz kendi yoluna döndü. Yine de RAB hepimizin cezasını ona yükledi.
Ife tonse, ngati nkhosa, tasochera, aliyense mwa ife akungodziyendera; ndipo Yehova wamusenzetsa zoyipa zathu zonse.
7 O baskı görüp eziyet çektiyse de Ağzını açmadı. Kesime götürülen kuzu gibi, Kırkıcıların önünde sessizce duran koyun gibi Açmadı ağzını.
Anthu anamuzunza ndi kumusautsa, koma sanayankhule kanthu. Monga mwana wankhosa wopita naye kokamupha amachitira, kapena monga nkhosa imakhalira duu poyimeta, momwemonso iye sanatsekule pakamwa pake.
8 Acımasızca yargılanıp ölüme götürüldü. Halkımın isyanı ve hak ettiği ceza yüzünden Yaşayanlar diyarından atıldı. Onun kuşağından bunu düşünen oldu mu?
Atatha kumugwira mwankhanza ndikumuyimba mlandu, kenaka anapita naye kukamupha. Ndipo ndani amene analabadirako za zidzukulu zake, poona kuti iye anachotsedwa mʼdziko la anthu amoyo? Ndani anaganizirapo poona kuti iye anakanthidwa chifukwa cha zolakwa za anthu anga?
9 Şiddete başvurmadığı, Ağzından hileli söz çıkmadığı halde, Ona kötülerin yanında bir mezar verildi, Ama öldüğünde zenginin yanındaydı.
Anamukonzera manda ake pamodzi ndi anthu oyipa ndipo anamuyika mʼmanda pamodzi ndi anthu achuma, ngakhale kuti iye sanachite za chiwawa, kapena kuyankhula za chinyengo.
10 Ne var ki, RAB onun ezilmesini uygun gördü, Acı çekmesini istedi. Canını suç sunusu olarak sunarsa Soyundan gelenleri görecek ve günleri uzayacak. RAB'bin istemi onun aracılığıyla gerçekleşecek.
Komatu ndi Yehova amene anafuna kuti amuzunze ndi kumusautsa. Yehova anapereka moyo wa mtumiki wake kuti ukhale nsembe yoperekedwa chifukwa cha zolakwa. Tsono iye adzaona zidzukulu zake ndipo adzakhala ndi moyo wautali, ndipo chifuniro cha Yehova chidzachitika mwa iye.
11 Canını feda ettiği için Gördükleriyle hoşnut olacak. Doğru kulum, kendisini kabul eden birçoklarını aklayacak. Çünkü onların suçlarını o üstlendi.
Atatha mazunzo a moyo wake, adzaona kuwala, ndipo adzakhutira. Mwa nzeru zake mtumiki wanga wolungamayo adzalungamitsa anthu ambiri, popeza adzasenza zolakwa zawo.
12 Bundan dolayı ona ünlüler arasında bir pay vereceğim, Ganimeti güçlülerle paylaşacak. Çünkü canını feda etti, başkaldıranlarla bir sayıldı. Pek çoklarının günahını o üzerine aldı, Başkaldıranlar için de yalvardı.
Motero Ine ndidzamupatsa ulemu pamodzi ndi akuluakulu, adzagawana zofunkha ndi ankhondo amphamvu, popeza anapereka moyo wake mpaka kufa, ndipo anamuyika mʼgulu la anthu olakwa kuti akhululukidwe. Pakuti iye anasenza machimo a anthu ambiri, ndipo anawapempherera anthu olakwa.

< Yeşaya 53 >