< Yeşaya 44 >
1 “Şimdi, ey kulum Yakup soyu, Seçtiğim İsrail halkı, dinle!
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Seni yaratan, rahimde sana biçim veren, Sana yardım edecek olan RAB şöyle diyor: ‘Korkma, ey kulum Yakup soyu, Ey seçtiğim Yeşurun!
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 “‘Susamış toprağı sulayacak, Kurumuş toprakta dereler akıtacağım. Çocuklarının üzerine Ruhum'u dökecek, Soyunu kutsayacağım.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 Akarsu kıyısında otlar arasında yükselen Kavaklar gibi boy atacaklar.’
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 “Kimi, ‘Ben RAB'be aitim’ diyecek, Kimi Yakup adını alacak, Kimi de eline ‘RAB'be ait’ yazıp İsrail adını benimseyecek.”
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 RAB, İsrail'in Kralı ve Kurtarıcısı, Her Şeye Egemen RAB diyor ki, “İlk ve son benim, Benden başka Tanrı yoktur.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Benim gibi olan var mı? Haber versin. Ezeli halkımı var ettiğimden beri olup bitenleri, Bundan sonra olacakları söyleyip sıralasın, Evet, gelecek olayları bildirsin!
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Yılmayın, korkmayın! Size çok önceden beri söyleyip açıklamadım mı? Tanıklarım sizsiniz. Benden başka Tanrı var mı? Hayır, başka Kaya yok; Ben bir başkasını bilmiyorum.”
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 Putlara biçim verenlerin hepsi boş insanlardır. Değer verdikleri nesneler hiçbir işe yaramaz. Putların tanıkları onlardır; Ne bir şey görür ne de bir şey bilirler. Bunun sonucunda utanç içinde kalacaklar.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 Kim yararsız ilaha biçim vermek, Dökme put yapmak ister?
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Bakın, bu putlarla uğraşanların hepsi utanacak. Onları yapanlar salt insan. Hepsi toplanıp yargılanmaya gelsin. Dehşete düşecek, utanacaklar birlikte.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Demirci aletini alır, Kömür ateşinde çalışır, Çekiçle demire biçim verir. Güçlü koluyla onu işler. Acıkır, güçsüz kalır, su içmeyince tükenir.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Marangoz iple ölçü alır, Tahtayı tebeşirle çizer. Raspayla tahtayı biçimlendirir, Pergelle işaretler, insan biçimi verir. İnsan güzelliğinde, Evde duracak bir put yapar.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 İnsan kendisi için sedir ağaçları keser, Palamut, meşe ağaçları alır. Ormanda kendine bir ağaç seçer. Bir çam diker, ama ağacı büyüten yağmurdur.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Sonra ağaç odun olarak kullanılır. İnsan aldığı odunla hem ısınır, Hem tutuşturup ekmek pişirir, Hem de bir ilah yapıp tapınır. Yaptığı putun önünde yere kapanır.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Odunun bir kısmını yakar, Ateşinde et kızartıp karnını doyurur. Isınınca bir oh çeker, “Isındım, ateşin sıcaklığını duyuyorum” der.
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Artakalan odundan kendine bir ilah, Oyma put yapar; Önünde yere kapanıp ona tapınır, “Beni kurtar, çünkü ilahım sensin” diye yakarır.
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Böyleleri anlamaz, bilmez. Çünkü gözleri de zihinleri de öylesine kapalı ki, Görmez, anlamazlar.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Durup düşünmez, bilmez, Anlamazlar ki şöyle desinler: “Odunun bir kısmını yakıp Ateşinde ekmek pişirdim, et kızartıp yedim. Artakalanından iğrenç bir şey mi yapayım? Bir odun parçasının önünde yere mi kapanayım?”
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Külle besleniyorlar. Aldanan yürekleri onları saptırıyor. Canlarını kurtaramaz, “Sağ elimdeki şu nesne aldatıcı değil mi?” diyemezler.
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 “Ey Yakup soyu, ey İsrail, Söylediklerimi anımsayın, çünkü kulumsunuz. Size ben biçim verdim, kulumsunuz; Seni unutmam, ey İsrail.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 İsyanlarınızı bulut gibi, Günahlarınızı sis gibi sildim. Bana dönün, çünkü sizi kurtardım.”
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 Sevinçle haykırın, ey gökler, Çünkü bunu RAB yaptı. Haykırın, ey yerin derinlikleri. Ey dağlar, ey orman, ormandaki her ağaç, Sevinç çığlıklarına katılın. Çünkü RAB Yakup soyunu kurtararak İsrail'de görkemini gösterdi.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Sizi kurtaran, Size rahimde biçim veren RAB diyor ki, “Her şeyi yaratan, Gökleri yalnız başına geren, Yeryüzünü tek başına seren, Sahte peygamberlerin belirtilerini boşa çıkaran, Falcılarla alay eden, Bilgeleri geri çeviren, Bilgilerini saçmalığa dönüştüren, Kulunun sözlerini yerine getiren, Ulaklarının peygamberlik sözlerini gerçekleştiren, Yeruşalim için, ‘İçinde oturulacak’, Yahuda kentleri için, ‘Yeniden kurulacak, Yıkıntılarını onaracağım’ diyen; Engine, ‘Kuru! Sularını kurutacağım’ diyen, Koreş için, ‘O çobanımdır, Her istediğimi yerine getirecek’, Yeruşalim için, ‘Yeniden kurulacak’, Tapınak için, ‘Temeli atılacak’ diyen RAB benim.”
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”