< Yeşaya 26 >
1 O gün Yahuda'da şu ilahi söylenecek: Güçlü bir kentimiz var. Çünkü Tanrı'nın kurtarışı Kente sur ve duvar gibidir.
Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi. Tili ndi mzinda wolimba. Mulungu amawuteteza ndi zipupa ndi malinga.
2 Açın kentin kapılarını, Sadık kalan doğru ulus içeri girsin.
Tsekulani zipata za mzinda kuti mtundu wolungama ndi wokhulupirika ulowemo.
3 Sana güvendiği için Düşüncelerinde sarsılmaz olanı Tam bir esenlik içinde korursun.
Inu mudzamupatsa munthu wa mtima wokhazikika mtendere weniweni.
4 RAB'be sonsuza dek güvenin, Çünkü RAB, evet RAB sonsuza dek kalıcı kayadır.
Mudalireni Yehova mpaka muyaya, chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
5 Yüksekte oturanı alçaltır, Yüce kenti yıkar, Yerle bir eder.
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba, iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula, amagumula makoma ake ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
6 O kent ayak altında, Mazlumların ayakları, Yoksulların adımları altında çiğnenecek.
Mapazi a anthu akuwupondereza, mapazi a anthu oponderezedwa, mapazi anthu osauka.
7 Doğru adamın yolu düzdür, Ey Dürüst Olan, doğru adamın yolunu sen düzlersin.
Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza, Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
8 Evet, ya RAB, ilkelerinin çizdiği yolda sana umut bağladık, Adın ve ünündür yüreğimizin dileği,
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama, ife timayembekezera Inu; mitima yathu imakhumba kukumbukira ndi kulemekeza dzina lanu.
9 Geceleri canım sana susar, Evet, içimde ruhum seni özler; Çünkü senin ilkelerin yeryüzünde oldukça, Orada oturanlar doğruluğu öğrenir.
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse; nthawi yammawa ndimafunafuna Inu. Pamene muweruza dziko lapansi anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
10 Kötüler lütfedilse bile doğruluğu öğrenmez. Dürüstlüğün egemen olduğu diyarda haksızlık eder, RAB'bin büyüklüğünü görmezler.
Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa, saphunzira chilungamo. Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo, ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
11 Ya RAB, elin yükseldi, ama görmüyorlar, Halkın için gösterdiğin gayreti görüp utansınlar. Evet, düşmanların için yaktığın ateş onları yiyip bitirecek.
Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange, koma iwo sakuliona dzanjalo. Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu; ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.
12 Ya RAB, bizi esenliğe çıkaracak sensin, Çünkü ne yaptıysak hepsi senin başarındır.
Yehova, mumatipatsa mtendere; ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
13 Ey Tanrımız RAB, senden başka efendiler bizi yönetti, Ama yalnız sana, senin adına yakaracağız.
Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu, koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
14 O efendiler öldü, artık yaşamıyorlar, Dirilmeyecek onlar. Çünkü onları cezalandırıp yok ettin, Anılmalarına son verdin.
Iwo tsopano sadzadzukanso; mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga; palibenso amene amawakumbukira.
15 Ulusu çoğalttın, ya RAB, Evet, ulusu çoğalttın ve yüceltildin. Her yönde ülkenin sınırlarını genişlettin.
Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu; mwauchulukitsa ndithu ndipo mwalandirapo ulemu; mwaukuza mbali zonse za dziko.
16 Ya RAB, sıkıntıdayken seni aradılar. Onları terbiye ettiğinde sessizce yakararak içlerini döktüler.
Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso; pamene munawalanga, iwo anapemphera kwa Inu.
17 Doğum vakti yaklaşan gebe kadın Çektiği sancıdan ötürü nasıl kıvranır, feryat ederse, Senin önünde biz de öyle olduk, ya RAB.
Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu, ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
18 Gebe kaldık, kıvrandık, Rüzgardan başka bir şey doğurmadık sanki. Ne dünyaya kurtuluş sağlayabildik, Ne de dünyada yaşayanları yaşama kavuşturabildik.
Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana, koma sitinapindulepo kanthu, kapena kupulumutsa dziko lapansi; sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.
19 Ama senin ölülerin yaşayacak, Bedenleri dirilecek. Ey sizler, toprak altında yatanlar, Uyanın, ezgiler söyleyin. Çünkü senin çiyin sabah çiyine benzer, Toprak ölülerini yaşama kavuşturacak.
Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo; matupi awo adzadzuka. Iwo amene ali ku fumbi tsopano adzadzuka ndi kuyimba mosangalala. Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera, momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.
20 Haydi halkım, iç odalarınıza girip Ardınızdan kapılarınızı kapatın, RAB'bin öfkesi geçene dek kısa süre gizlenin.
Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu ndipo mukadzitsekere; mukabisale kwa kanthawi kochepa mpaka ukali wake utatha.
21 Çünkü dünyada yaşayanları Suçlarından ötürü cezalandırmak için RAB bulunduğu yerden geliyor. Dünya üzerine dökülen kanı açığa vuracak, Öldürülenleri artık saklamayacak.
Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala; akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo. Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo; dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.