< Yeşaya 23 >

1 Sur Kenti'yle ilgili bildiri: Ey ticaret gemileri, feryat edin! Çünkü Sur Kenti evleriyle, Limanlarıyla birlikte yok oldu. Kittim'den size haber geldi.
Uthenga wonena za Turo: Lirani mofuwula, inu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi: pakuti mzinda wa Turo wawonongedwa ndipo mulibe nyumba kapena dooko. Zimenezi anazimva pochokera ku Kitimu.
2 Ey kıyı halkı ve denizcilerin zenginleştirdiği Sayda tüccarları, susun!
Khalani chete inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja, inu amalonda a ku Sidoni, iwe amene unalemera ndi anthu oyenda pa nyanja.
3 Şihor'un tahılı, Nil'in ürünü Denizleri aşar, Sur'a gelir sağlardı. Ulusların kârı ona akardı.
Pa nyanja zazikulu panabwera tirigu wa ku Sihori; zokolola za ku Nailo, ndipo munachita malonda ndi anthu a mitundu ina.
4 Utan, ey Sayda, ey deniz kıyısındaki kale! Çünkü deniz sana sesleniyor: “Ne doğum ağrısı çektim, ne de doğurdum. Ne delikanlılar büyüttüm, ne de kızlar.”
Chita manyazi, iwe Sidimu pakuti nyanja yayankhula, linga la ku nyanja (Turo) layankhula kuti, “Sindinamvepo zowawa za kubereka kapena kuberekapo mwana; sindinalerepo ana aamuna kapena kulera ana aakazi.”
5 Sur'un haberi Mısır'a ulaşınca, Yüreği burkulacak insanların.
Mawuwa akadzamveka ku Igupto, iwo adzachita mantha akadzamva kuti Turo wawonongeka.
6 Tarşiş'e geçin, ey kıyıda oturanlar, Feryat edin.
Wolokerani ku Tarisisi, lirani mofuwula, inu anthu okhala mʼmbali mwa nyanja.
7 Uzak ülkeleri yurt edinmiş, Eğlenceye düşkün halkınız, Eski, tarihsel kentiniz bu mu?
Kodi uwu si mzinda wachisangalalo uja, mzinda wakalekale, umene anthu ake ankapita kukakhala ku mayiko akutali?
8 Taçlar giydiren Sur'a karşı bu işi kim tasarladı? O kent ki, tüccarları prenslerdi, İş adamları dünyanın saygın kişileriydi.
Kodi ndani anakonza zimenezi kuti zigwere Turo, mzinda umene unakhazikitsa mizinda ina, mzinda umene amalonda ake ndi akalonga ndi otchuka pa dziko lapansi?
9 Görkeminin sonucu olan gururunu kırmak, Dünyaca ünlü bütün saygın kişilerini alçaltmak için Her Şeye Egemen RAB tasarladı bunu.
Yehova Wamphamvuzonse anakonza zimenezi kuti athetse kunyada kwawo ndi kutsitsa anthu otchuka a pa dziko lapansi.
10 Kendi topraklarını Nil gibi basıp geç, Ey Tarşiş kızı, artık engel yok.
Mubalalike mʼdziko mwanu ngati mtsinje wa Nailo inu anthu a ku Tarisisi, pakuti mulibenso chokutetezani.
11 RAB denizin üzerine elini uzatıp ülkeleri titretti, Kenan kalelerinin yıkılmasını buyurdu.
Yehova watambasula dzanja lake kuloza ku nyanja ndipo wagwedeza maufumu ake. Iye walamula kuti Kanaani agwetse malinga ake.
12 “Eğlencen sona erdi, ey Sayda, erden kız!” dedi, “Kirletildin. Kalk, Kittim'e geç, Orada bile rahat yüzü görmeyeceksin.”
Iye anati, “Simudzakondwanso konse, inu anthu opanikizidwa a ku Sidoni, tsopano wamphwanyidwa! “Ngakhale muwolokere ku Kitimu, kumeneko simukapezako mpumulo.”
13 Kildan ülkesine bak! O halk yok artık. Asurlular onların ülkesini yabanıl hayvanlara verdi, Kuşatma kuleleri diktiler, saraylarını soydular, Ülkeyi viraneye çevirdiler.
Onani dziko la Ababuloni, anthu amenewa tsopano atheratu! Asiriya asandutsa Turo kukhala malo a zirombo za ku chipululu; anamanga nsanja zawo za nkhondo, anagumula malinga ake ndipo anawasandutsa bwinja.
14 Feryat edin, ey ticaret gemileri! Çünkü sığınağınız harap oldu.
Lirani mofuwula, inu anthu oyendetsa sitima za pa madzi za ku Tarisisi; chifukwa malinga ako agwetsedwa!
15 Bundan sonra Sur Kenti yetmiş yıl, bir kralın ömrü süresince unutulacak. Yetmiş yıl bitince, fahişe için bestelenen türküdeki gibi Sur'a şöyle denecek:
Pa nthawi imeneyo Turo adzayiwalika pa zaka 70, amene ndi masiku a moyo wa mfumu. Koma potsiriza pa zaka 70 zimenezi, Turo adzakhala ngati mkazi wachiwerewere woyimbidwa mu nyimbo:
16 “Bir lir al, dolaş kenti, Ey sen, unutulmuş fahişe! Güzel çal seni anımsamaları için, Türkü üstüne türkü söyle.”
“Tenga zeze wako uzungulire mzinda, iwe mkazi wachiwerewere woyiwalika; imba zeze mokometsera, imba nyimbo zambiri, kuti anthu akukumbukire.”
17 Yetmiş yıl geçince RAB Sur'la ilgilenecek, ama Sur para için yine fahişeliğe dönecek. Dünyanın bütün krallıklarıyla fahişelik edecek.
Pakutha pa zaka 70, Yehova adzachitapo kanthu pa Turo. Iye adzabwerera ku ntchito yake yakale monga mkazi wachiwerewere ndipo adzachita zachiwerewere ndi maufumu onse a dziko lapansi.
18 Kentin ticaretten ve fuhuştan kazandıkları RAB'be adanacak. Bunlar biriktirilmeyecek, hazineye konmayacak. Ticaretten kazandıklarını doyuncaya dek yesinler, güzel güzel giyinsinler diye RAB'bin önünde yaşayanlara verilecek.
Koma phindu lake ndi malipiro ake adzazipereka kwa Yehova; sadzazikundika kapena kuzisunga. Phindu lake lidzapita kwa mtumiki wa Yehova kuti agule zakudya zambiri ndi zovala zokongola.

< Yeşaya 23 >