< Yeşaya 14 >
1 Çünkü RAB Yakup soyuna acıyacak, İsrail halkını yine seçip Topraklarına yerleştirecek. Yabancılar da Yakup soyuna katılıp onlara bağlanacak.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Uluslar İsrail halkını İsrail topraklarına götürecekler. İsrail halkı RAB'bin verdiği topraklarda onları Erkek ve kadın köle olarak sahiplenecek. Kendisini tutsak edenleri tutsak edecek, Kendisini ezenlere egemen olacak.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 RAB İsrail halkını acıdan, sıkıntıdan Ve yaptığı ağır işlerden kurtardığı gün
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Babil Kralı'nı alaya alarak, “Halkı ezenin nasıl da sonu geldi!” diyecekler, “Zorbalığı nasıl da sona erdi!”
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 RAB kötülerin değneğini, Egemenlerin asasını kırdı.
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 O asa ki, halklara gazapla vurdukça vurdu, Ulusları öfkeyle, dinmeyen zulümle yönetti.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Bütün dünya esenlik ve barış içinde Sevinçle haykırıyor.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Lübnan'ın çam ve sedir ağaçları bile Kralın yok oluşuna seviniyor. “Onun ölümünden beri kimse bizi kesmeye gelmiyor” diyorlar.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Toprağın altındaki ölüler diyarı Babil Kralı'nı karşılamak için sabırsızlanıyor. Onun gelişi ölüleri, Dünyanın eski önderlerini heyecanlandırıyor; Ulusları yönetmiş kralları Tahtlarından ayağa kaldırıyor. (Sheol )
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol )
10 Hepsi ona seslenip diyecekler ki, “Sen de bizim gibi gücünü yitirdin, Bize benzedin.”
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Görkemin de çenklerinin sesi de Ölüler diyarına indirildi. Altında kurtlar kaynaşacak, Üstünü kurtçuklar kaplayacak. (Sheol )
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol )
12 Ey parlak yıldız, seherin oğlu, Göklerden nasıl da düştün! Ey ulusları ezip geçen, Nasıl da yere yıkıldın!
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 İçinden, “Göklere çıkacağım” dedin, “Tahtımı Tanrı'nın yıldızlarından daha yükseğe koyacağım; İlahların toplandığı dağda, Safon'un doruğunda oturacağım.
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Bulutların üstüne çıkacak, Kendimi Yüceler Yücesi'yle eşit kılacağım.”
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Ancak ölüler diyarına, Ölüm çukurunun dibine İndirilmiş bulunuyorsun. (Sheol )
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol )
16 Seni görenler bakıp bakıp şöyle düşünecekler: “Dünyayı sarsan, ülkeleri titreten, Yeryüzünü çöle çeviren, Kentleri yerle bir eden, Tutsakları evlerine salıvermeyen adam bu mu?”
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Ulusların bütün kralları tek tek, Görkemli mezarlarda yatıyor.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Ama sen reddedilen bir dal gibi Mezarından dışarı atıldın; Bedenleri kılıçla delinip Ölüm çukurunun dibine atılmış ölülerle örtülüsün; Ayak altında çiğnenen leş gibisin.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Ülkeni harap edip halkını katlettiğin için Başkaları gibi gömülmeyeceksin. Kötülük yapan soy bir daha anılmayacak.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Atalarının suçundan ötürü Babil Kralı'nın oğullarını boğazlamak için yer hazırlayın. Kalkıp dünyayı sahiplenmesinler, Yeryüzünü kentlerle doldurmasınlar.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 “Babil halkına karşı harekete geçeceğim” Diyor Her Şeye Egemen RAB, “Babil'in adını, sağ kalanlarını, Oğullarını, torunlarını dünyadan sileceğim.” Böyle diyor RAB.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 “Babil'i baykuş yuvasına, bataklığa çevirecek, Yıkım süpürgesiyle süpüreceğim” Diyor Her Şeye Egemen RAB.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Her Şeye Egemen RAB ant içerek şöyle dedi: “Düşündüğüm gibi olacak, Tasarladığım gibi gerçekleşecek.
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Asurlular'ı kendi ülkemde ezecek, Dağlarımda çiğneyeceğim. Halkım Asur'un boyunduruğundan, Omuzlarındaki yükten kurtulacak.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 İşte bütün dünya için belirlenen tasarı budur. Bütün uluslara karşı elim kalkmış durumda.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Her Şeye Egemen RAB'bin tasarısını kim boşa çıkarabilir? Kalkmış durumdaki elini kim indirebilir?”
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 Kral Ahaz'ın öldüğü yıl gelen bildiri:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Ey Filistliler, sizi döven değnek kırıldı diye sevinmeyin. Çünkü yılanın kökünden engerek türeyecek, Onun ürünü uçan yılan olacak.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Yoksulların en yoksulu doyacak, Düşkünler güvenlikte yatacak. Ama sizin kökünüzü kıtlıkla kurutacağım, Sağ kalanlarınız da ölecek.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Ulumaya başla ey kapı! Ey kent, feryat et! Ey Filistliler, eridiniz baştan başa. Kuzeyden toz duman yükseliyor, Düşman askerleri sıra sıra geliyor.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 O ulusun elçilerine ne yanıt verilecek? “RAB Siyon'un temelini attı, Halkının düşkünleri oraya sığınacak” denecek.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”