< Yeşaya 13 >
1 Amots oğlu Yeşaya'nın Babil'le ilgili bildirisi:
Uthenga onena za Babuloni umene Yesaya mwana wa Amozi anawulandira:
2 Çıplak dağın tepesine sancak dikin! Savaşçıları yüksek sesle çağırıp El sallayın ki Soylulara ayrılan kapılardan içeri girsinler.
Kwezani mbendera yankhondo pa phiri loti see, muwafuwulire ankhondo; muwakodole kuti adzalowe pa zipata za anthu olemekezeka.
3 RAB seçtiklerine buyruk verdi, O'nun yüceliğiyle övünen yiğitleri Öfkesinin gereğini yapmaya çağırdı.
Ine Yehova, ndalamulira ankhondo anga; ndasonkhanitsa ankhondo anga kuti akhale zida zanga zolangira amene amadzikuza ndi chipambano changa.
4 Dağlardaki kalabalığın gürültüsünü dinleyin! Büyük bir halkın sesini andırıyor. Bir araya gelmiş ulusların Ve krallıkların gümbürtüsünü dinleyin! Her Şeye Egemen RAB bir orduyu savaşa hazırlıyor.
Tamvani phokoso ku mapiri, likumveka ngati phokoso la gulu lalikulu la anthu! Tamvani phokoso pakati pa maufumu, ngati kuti mitundu ya anthu ikusonkhana pamodzi! Yehova Wamphamvuzonse akukhazika asilikali ake mokonzekera kuchita nkhondo.
5 Öfkesinin araçlarıyla uzak bir ülkeden, Dünyanın öbür ucundan Bütün ülkeyi yerle bir etmek üzere geliyor.
Iwo akuchokera ku mayiko akutali, kuchokera kumalekezero a dziko Yehova ali ndi zida zake za nkhondo kuti adzawononge dziko la Babuloni.
6 Feryat edin! Çünkü RAB'bin günü yakındır. Her Şeye Gücü Yeten'in göndereceği yıkım gibi geliyor o gün.
Lirani mofuwula, pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
7 Bu yüzden ellerde derman kalmayacak, Her yürek eriyecek.
Zimenezi zinafowoketsa manja onse, mtima wa munthu aliyense udzachokamo.
8 Herkesi dehşet saracak, Hepsi acı ve ıstırap içinde boğulacak, Doğuran kadın gibi kıvranacak, Şaşkın şaşkın birbirlerine bakacaklar; Yüzleri kızaracak.
Anthu adzagwidwa ndi mantha aakulu, zowawa ndi masautso zidzawagwera; adzamva zowawa zonga amamva mayi pobereka. Adzayangʼanana mwamantha, nkhope zawo zikufiira ngati malawi amoto.
9 İşte RAB'bin acımasız günü geliyor. Ülkeyi viraneye çevirip İçindeki günahkârları ortadan kaldıracağı Gazap ve kızgın öfke dolu gün geliyor.
Taonani, tsiku la Yehova likubwera, tsiku lopanda chisoni, lawukali ndi lamkwiyo; kudzasandutsa dziko kuti likhale chipululu ndi kuwononga anthu ochimwa a mʼmenemo.
10 Gökteki yıldızlarla takımyıldızlar ışımayacak, Doğan güneş kararacak, ay ışığını vermez olacak.
Nyenyezi zakumwamba ndiponso zonse zamlengalenga sizidzaonetsa kuwala kwawo. Dzuwa lidzada potuluka, ndipo mwezi sudzawala konse.
11 RAB diyor ki, “Kötülüğünden ötürü dünyayı, Suçlarından ötürü kötüleri cezalandıracağım. Kibirlilerin küstahlığını sona erdirecek, Zalimlerin gururunu kıracağım.
Ndidzalanga dziko lonse chifukwa cha zolakwa zake, anthu oyipa ndidzawalanga chifukwa cha machimo awo. Ndidzathetsa kunyada kwa odzikuza, ndipo ndidzatsitsa kudzitukumula kwa anthu ankhanza.
12 İnsanı saf altından, Ofir altınından daha ender kılacağım.
Ndidzasandutsa anthu kukhala ovuta kupeza kuposa mmene amasowera golide wabwino. Iwo sazidzapezekapezeka kuposa mmene amasowera golide wa ku Ofiri.
13 Ben, Her Şeye Egemen RAB, Gazaba geldiğim, öfkemin alevlendiği gün Gökleri titreteceğim, yer yerinden oynayacak.
Tsono ndidzagwedeza miyamba ndipo dziko lapansi lidzachoka pa maziko ake. Izi zidzachitika chifukwa cha ukali wa Wamphamvuzonse pa tsiku la mkwiyo wake woopsa.
14 “Herkes kovalanan ceylan gibi, Çobansız koyunlar gibi halkına dönecek, Ülkesine kaçacak.
Ngati mbawala zosakidwa, ngati nkhosa zopanda wozikusa, munthu aliyense adzabwerera kwa anthu akwawo, aliyense adzathawira ku dziko lake.
15 Yakalananın bedeni delik deşik edilecek, Ele geçen kılıçtan geçirilecek.
Aliyense amene atadzapezeke ndi kugwidwa adzaphedwa momubaya ndi lupanga.
16 Yavruları gözleri önünde parçalanacak, Evleri yağmalanacak, Kadınlarının ırzına geçilecek.
Ana awo akhanda adzaphwanyidwa iwo akuona; nyumba zawo zidzafunkhidwa ndipo akazi awo adzagwiriridwa.
17 “Gümüşe değer vermeyen, Altını sevmeyen Medler'i Onlara karşı harekete geçireceğim.
Taona, Ine ndidzadzutsa Amedi amene safuna siliva ndipo sasangalatsidwa ndi golide, kuti amenyane ndi Ababuloni.
18 Oklarıyla gençleri parçalayacak, Bebeklere acımayacak, Çocukları esirgemeyecekler.
Adzapha anyamata ndi mauta awo; sadzachitira chifundo ana ngakhale kumvera chisoni ana akhanda.
19 Ben Tanrı, Sodom ve Gomora'yı nasıl yerle bir ettimse, Kildaniler'in yüce gururu, Krallıkların en güzeli olan Babil'i de yerle bir edeceğim.
Babuloni, ufumu wake ndi waulemerero kuposa mafumu onse. Anthu ake amawunyadira. Koma Yehova adzawuwononga ngati mmene anawonongera Sodomu ndi Gomora.
20 Orada bir daha kimse yaşamayacak, Kuşaklar boyu kimse oturmayacak, Bedeviler çadır kurmayacak, Çobanlar sürülerini dinlendirmeyecek.
Anthu sadzakhalamonso kapena kukhazikikamo pa mibado yonse; palibe Mwarabu amene adzayimike tenti yake, palibe mʼbusa amene adzawetamo ziweto zake.
21 Orası yabanıl hayvanlara barınak olacak, Evler çakallarla dolacak, Baykuşlar yuva yapacak, tekeler oynaşacak orada.
Koma nyama zakuthengo ndizo zidzakhale kumeneko, nyumba zake zidzadzaza ndi nkhandwe; mu mzindamo muzidzakhala akadzidzi, ndipo atonde akuthengo azidzalumphalumphamo.
22 Kalelerinde sırtlanlar, Görkemli saraylarında çakallar uluyacak. Babil'in sonu yaklaştı, günleri uzatılmayacak.”
Mu nsanja zake muzidzalira afisi, mʼnyumba zake zokongola muzidzalira nkhandwe. Nthawi yake yayandikira ndipo masiku ake ali pafupi kutha.