< Hoşea 9 >

1 Ey İsrail, öteki halklar gibi sevinme, coşma! Çünkü kendi Tanrın'a vefasızlık ederek zina ettin, Harman yerlerinin tümünde zina kazancına gönül verdin.
Iwe Israeli, usakondwere; monga imachitira mitundu ina. Pakuti wakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wako; umakonda malipiro a chiwerewere pa malo aliwonse opunthira tirigu.
2 Ama harman yeri, şarap teknesi halkı doyurmayacak, Yeni şarap umutları boşa çıkacak.
Malo opunthira tirigu ndi malo opsinyira mphesa sadzadyetsa anthu; adzasowa vinyo watsopano.
3 RAB'bin diyarında kalmayacaklar, Mısır'a dönecek Efrayim, Asur'da kirli sayılan şeyleri yiyecekler.
Sadzakhalanso mʼdziko la Yehova. Efereimu adzabwerera ku Igupto ndipo mudzadya chakudya chodetsedwa ku Asiriya.
4 RAB'be şarap sunuları dökmeyecekler, O'nu hoşnut etmeyecek kurbanları. Kurbanları yas yemeğine dönecek, Kirli sayılacak onları yiyenlerin hepsi. Yalnız kendi karınlarını doyuracak yiyecekleri, RAB'bin Tapınağı'na girmeyecek.
Iwo sadzaperekanso chopereka cha chakumwa kwa Yehova, kapena nsembe zawo kuti akondweretse Yehovayo. Nsembe zotere zidzakhala kwa iwo ngati chakudya cha anamfedwa; onse akudya chakudya chimenechi adzakhala odetsedwa. Chakudya ichi chidzakhala chodya okha, sichidzalowa mʼnyumba ya Yehova.
5 Ne yapacaksınız dinsel bayramlarda, RAB'bin bayram gününde?
Kodi mudzachita chiyani pa tsiku la maphwando anu oyikika; pa masiku a zikondwerero za Yehova?
6 Yıkımdan kaçsalar bile, Mısır bir araya toplayacak onları, Mof gömecek. Değerli gümüş eşyalarını yabanıl otlar saracak, Diken bitecek çadırlarında.
Ngakhale iwo atathawa chiwonongeko, Igupto adzawasonkhanitsa, ndipo Mefisi adzawayika mʼmanda. Khwisa adzamera pa ziwiya zawo zasiliva, ndipo minga idzamera mʼmatenti awo.
7 Onların ceza günleri geldi, Hesap günleri çattı. Bunu bilsin İsrail! Suçunuzun çokluğundan, Düşmanlığınızın büyüklüğü yüzünden, Peygamber aptal, ruhsal insan deli sayıldı.
Masiku achilango akubwera, masiku obwezera ali pafupi. Israeli adziwe zimenezi. Chifukwa machimo anu ndi ochuluka kwambiri ndipo udani wanu pa Mulungu ndi waukulu kwambiri. Mneneri amamuyesa chitsiru, munthu wanzeru za kwa Mulungu ngati wamisala.
8 Peygamber Tanrım'ın yanısıra Efrayim'e gözcülük eder, Ama tuzak kurulmuş bütün yollarına, Düşmanlık var Tanrı'nın Tapınağı'nda.
Mneneri pamodzi ndi Mulungu wanga ndiwo alonda a Efereimu, koma mneneri amutchera misampha mʼnjira zake zonse, ndipo udani ukumudikira mʼnyumba ya Mulungu wake.
9 Alabildiğine yozlaştılar, Giva'da olduğu gibi. Tanrı suçlarını anımsayacak, Günahlarının cezasını verecek.
Iwo azama mu zachinyengo monga masiku a Gibeya. Mulungu adzakumbukira zolakwa zawo ndipo adzawalanga chifukwa cha machimo awo.
10 “İsrail çölde Bir salkım üzüm gibi geldi bana, Atalarıysa incir ağacının ilk ürünü gibi. Ama Baal-Peor'a geldiklerinde Utanç dolu puta adadılar kendilerini, Sevdikleri şey kadar iğrenç oldular.
“Pamene ndinamupeza Israeli zinali ngati kupeza mphesa mʼchipululu. Nditaona makolo anu, zinali ngati ndikuona nkhuyu zoyambirira kupsa. Koma atafika ku Baala Peori, anadzipereka ku fano lija lochititsa manyazi ndipo anakhala onyansa ngati chinthu chimene anachikondacho.
11 Efrayim'in görkemi bir kuş gibi uçup gidecek, Ne doğum ne gebelik olacak, kimse gebe kalmayacak.
Ulemerero wa Efereimu udzawuluka ngati mbalame. Sipadzakhalanso kubereka ana, kuyembekezera kapena kutenga pathupi.
12 Çocuklarını büyütseler bile, Çocuklarından edeceğim onları, Kimse kalmayıncaya dek; Evet, vay başlarına, Onları terk ettiğimde!
Ngakhale atalera ana ndidzachititsa kuti mwana aliyense amwalire. Tsoka kwa anthuwo pamene Ine ndidzawafulatira!
13 Efrayim'i, Sur Kenti gibi, Güzel bir yere kurulmuş gördüm. Ama Efrayim çocuklarını celladın önüne götürecek.”
Ndaona Efereimu ngati Turo, atadzalidwa pa nthaka ya chonde. Koma Efereimu adzatsogolera ana ake kuti akaphedwe.”
14 Ya RAB, ver onlara ne vereceksen! Düşük yapan rahimler, sütsüz memeler ver.
Inu Yehova, muwapatse. Kodi mudzawapatsa chiyani? Apatseni mimba yomangopita padera ndi mawere owuma.
15 “Gilgal'daki kötülükleri yüzünden, Nefret ettim orada onlardan. İşledikleri günahlardan ötürü, Onları evimden kovacağım. Artık sevmeyeceğim onları, Bütün önderleri asidir.
“Chifukwa cha zoyipa zawo zonse ku Giligala, Ine ndinawada kumeneko. Chifukwa cha machitidwe awo auchimo, ndidzawapirikitsa mʼnyumba yanga. Sindidzawakondanso; atsogoleri awo onse ndi owukira.
16 Vuruldu Efrayim, Kökleri kurudu, Meyve vermeyecekler artık. Çocuk doğursalar bile, Rahimlerinin değerli meyvelerini öldüreceğim.”
Efereimu wathedwa, mizu yake yauma sakubalanso zipatso. Ngakhale atabereka ana, Ine ndidzapha ana awo okondedwawo.”
17 Reddedecek Tanrım onları, Çünkü O'nu dinlemediler, Uluslar arasında dolaşıp duracaklar.
Mulungu wanga adzawakana chifukwa sanamumvere Iye; adzakhala oyendayenda pakati pa anthu a mitundu ina.

< Hoşea 9 >