< Hoşea 12 >
1 Efrayim rüzgarı güdüyor, Doğu rüzgarının ardına düşüyor bütün gün; Yalanı, zorbalığı artıyor. Asur'la antlaşma yapıyor, Mısır'a zeytinyağı gönderiyor.
Efereimu amadya mpweya; tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa. Amachita mgwirizano ndi Asiriya ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.
2 RAB'bin davası var Yahuda'yla, Yakup soyunu izlediği yola göre cezalandıracak, Yaptıklarının karşılığını verecek.
Yehova akuyimba mlandu Yuda; Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake, adzamulanga molingana ndi ntchito zake.
3 Yakup ana rahminde kardeşinin topuğunu tuttu, Büyüyünce Tanrı'yla güreşti.
Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake; iye atakula analimbana ndi Mulungu.
4 Melekle güreşip yendi, Ağladı, kutsanmak istedi. Tanrı'yı Beytel'de buldu, RAB, Her Şeye Egemen Tanrı bizimle orada konuştu, O RAB diye anılır.
Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana; analira napempha kuti amukomere mtima. Mulungu anakumana naye ku Beteli ndipo anayankhula naye kumeneko,
Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Yehova ndiye dzina lake lotchuka!
6 Bu yüzden Tanrın'a dön sen, Sevgiye, adalete sarıl, Sürekli Tanrın'ı bekle.
Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu; pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama, ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.
7 Efrayim tüccardır, Hileli terazi kullanır, Aldatmayı sever.
Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo; iyeyo amakonda kubera anthu.
8 “Çok zengin oldum” diye böbürlenir, “Varlığa kavuştum, Çok emek çektim, Günah denecek bir suç bulamayacaklar bende.”
Efereimu amadzitama ponena kuti, “Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri. Palibe amene angandiloze chala chifukwa cha kulemera kwanga.”
9 “Ama seni Mısır'dan çıkaran Tanrın RAB benim. Bayram günlerindeki gibi, Seni yine çadırlarda oturtacağım.
“Ine ndine Yehova Mulungu wako amene ndinakutulutsa mu Igupto. Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti, monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.
10 Peygamberlere de söyledim, Çok görümler sağladım, Onlar aracılığıyla örnekler verdim.”
Ndinayankhula ndi aneneri, ndinawaonetsa masomphenya ambiri, ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”
11 Kötülük mü var Gilat'ta? Gerçekten değersiz bir halk! Gilgal'da sığır üstüne sığır kurban ediyorlar, Sunakları sürülmüş tarladaki taş yığınlarını andırıyor.
Kodi Giliyadi ndi woyipa? Anthu ake ndi achabechabe! Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala? Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala mʼmunda molimidwa.
12 Yakup Aram'a kaçtı, İsrail bir karı için kul oldu, Koyun güttü.
Yakobo anathawira ku dziko la Aramu, Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi, ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.
13 RAB İsrail'i bir peygamber aracılığıyla Mısır'dan çıkardı, Yine bir peygamber korudu onları.
Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto; kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.
14 Ama Efrayim Tanrı'yı aşırı öfkelendirdi. Rab döktükleri kanın hesabını soracak, Aşağılamalarının karşılığını verecek.
Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri. Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa. Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.