< Hagay 2 >

1 Yedinci ayın yirmi birinci günü RAB Peygamber Hagay aracılığıyla şöyle seslendi:
Pa tsiku la 21 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, Yehova anayankhula kudzera mwa mneneri Hagai kuti:
2 “Şealtiel'in torunu Yahuda Valisi Zerubbabil'e, Yehosadak oğlu Başkâhin Yeşu'ya ve sürgünden dönen halka de ki,
“Yankhula kwa Zerubabeli mwana wa Sealatieli, bwanamkubwa wa Yuda, kwa Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe, ndi kwa anthu onse otsala. Afunse kuti,
3 ‘Aranızda bu tapınağı önceki görkemiyle gören kaldı mı? Şimdi size nasıl görünüyor? Bir hiç olarak görünmüyor mu?
‘Kodi alipo amene watsala pakati panu amene anaona ulemerero wakale wa Nyumba iyi? Nanga tsopano ikuoneka motani kwa inu? Kodi sikuoneka ngati yopanda pake kwa inu?
4 Şimdi sen, ey Zerubbabil, yüreklen!’ RAB böyle diyor. ‘Ey Yehosadak oğlu Başkâhin Yeşu, yüreklen! Ey ülke halkı, yüreklen!’ RAB böyle diyor. ‘İşi sürdürün. Çünkü ben sizinle birlikteyim.’ Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.
Iwe Zerubabeli, limba mtima tsopano,’ akutero Yehova. ‘Limba mtima, iwe Yoswa mwana wa Yehozadaki, mkulu wa ansembe. Limbani mtima, anthu nonse a mʼdziko,’ akutero Yehova, ‘ndipo gwirani ntchito. Pakuti ine ndili nanu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
5 ‘Mısır'dan çıktığınızda, size bu konuda söz verdim. Ruhum aranızdadır. Korkmayın!’
‘Izi ndi zimene ndinapangana nanu pamene munkatuluka ku Igupto. Ndipo Mzimu wanga uli pakati panu. Musachite mantha.’
6 “Her Şeye Egemen RAB diyor ki, ‘Kısa zamanda bir kez daha yeri, göğü, denizi, karayı sarsacağım.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakapita nthawi pangʼono ndidzagwedezanso thambo ndi dziko lapansi, nyanja ndi mtunda.
7 Bütün ulusları sarsacağım, değerli eşyalarını buraya getirecekler. Ben de bu tapınağı görkemle dolduracağım.’ Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.
Ndidzagwedeza mitundu yonse ya anthu, ndipo chimene mitundu yonse ya anthu imachifuna chidzabwera, ndipo ndidzaza Nyumba ino ndi ulemerero,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
8 ‘Gümüş de, altın da benim’ diyor Her Şeye Egemen RAB.
‘Siliva yense ndi wanga, golide yense ndi wanganso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 ‘Yeni tapınağın görkemi, öncekinden daha büyük olacak. Buraya esenlik vereceğim.’ Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.”
‘Ulemerero wa nyumba iyi udzaposa ulemerero wa nyumba yoyamba ija,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse. ‘Ndipo pamalo pano ndidzakhazikitsapo mtendere,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
10 Darius'un krallığının ikinci yılında, dokuzuncu ayın yirmi dördüncü günü RAB, Peygamber Hagay'a seslendi:
Chaka chachiwiri cha Dariyo, pa tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi mneneri Hagai kuti:
11 “Her Şeye Egemen RAB diyor ki, ‘Kâhinlere yasayla ilgili şu soruyu sor:
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Funsa ansembe za zimene lamulo likunena:
12 Eğer biri giysisinin kıvrımları arasında kutsanmış et taşır ve o kıvrım ekmeğe, yemeğe, şaraba, zeytinyağına ya da başka bir yiyeceğe değerse, o yiyecek kutsal olur mu?’” Kâhinler, “Hayır” diye yanıtladılar.
Ngati munthu wakulunga nyama yopatulika mu mkanjo wake, ndipo mkanjowo nʼkukhudza buledi kapena msuzi, kapena vinyo, mafuta kapena chakudya cha mtundu wina uliwonse, kodi zimenezo zimasanduka zopatulika?’” Ansembe anayankha kuti, “Ayi.”
13 Hagay konuşmasını şöyle sürdürdü: “Ölüye dokunduğu için kirli sayılan biri, bu yiyeceklerden birine dokunursa, o yiyecek kirlenmiş olur mu?” Kâhinler, “Evet, kirlenmiş olur” diye karşılık verdiler.
Pamenepo Hagai anati, “Ngati munthu amene anayipitsidwa pokhudza mtembo akhudza chimodzi cha zinthu zimenezi, kodi chinthucho chimayipitsidwa?” Ansembe anayankha kuti, “Inde, chimayipitsidwa.”
14 Bunun üzerine Hagay şöyle dedi: “RAB, ‘Bu halk, bu ulus gözümde böyledir’ diyor, ‘Her yaptıkları, sunakta her sundukları da kirlidir.’”
Pamenepo Hagai anati, “‘Ndi mmene zilili ndi anthu awa ndi dziko ili pamaso panga,’ akutero Yehova. ‘Chilichonse amachita ndiponso chilichonse chimene amapereka nʼchodetsedwa.
15 “‘Bugüne dek olanları iyi düşünün; RAB'bin Tapınağı'nda taş üstüne taş konulmadan önce, yirmi ölçeklik bir tahıl yığınına gelen biri, yalnızca on ölçek bulurdu; şarap teknesinden elli ölçek çıkarmaya varan biri, yalnızca yirmi ölçek bulurdu.
“‘Tsopano muganizire zimenezi kuyambira lero mpaka mʼtsogolo. Ganizirani momwe zinthu zinalili asanayambe kumanga nyumba ya Yehova.
Pamene munthu ankayembekezera miyeso ya tirigu makumi awiri ankangopeza khumi yokha. Munthu akapita kuti akatunge miyeso makumi asanu ya vinyo mu mtsuko, ankangopeza miyeso makumi awiri yokha.
17 Ellerinizin bütün emeğini samyeliyle, küfle, doluyla cezalandırdım. Yine de bana dönmediniz.’ RAB böyle diyor.
Ndinawononga ntchito yonse ya manja anu ndi chinsikwi, chiwawu ndi matalala, komabe inu simunatembenukire kwa Ine,’ akutero Yehova
18 ‘Bugünden, dokuzuncu ayın yirmi dördüncü gününden, RAB'bin Tapınağı'nın temelinin atıldığı günden başlayarak olacakları iyi düşünün.
‘Kuyambira lero tsiku la 24 la mwezi wachisanu ndi chinayi mpaka mʼtsogolo, chonde ganizirani bwino tsiku limene munayika maziko a nyumba ya Yehova. Ganizirani bwino.
19 Ambarda hiç tohum kaldı mı? Asma, incir, nar, zeytin ağaçları bugüne dek ürün verdi mi? “‘Bugünden başlayarak üzerinize bereket yağdıracağım.’”
Kodi mʼnkhokwe mwatsala mbewu? Mpaka lero, mpesa ndi mtengo wa mkuyu, makangadza ndi mtengo wa olivi sizinabereke zipatso. “‘Kuyambira lero mpaka mʼtsogolo ndidzakudalitsani.’”
20 Ayın yirmi dördüncü günü RAB Hagay'a ikinci kez seslendi:
Yehova anayankhula ndi Hagai kachiwiri, pa tsiku la 24 la mwezi kuti:
21 “Yahuda Valisi Zerubbabil'e de ki, ben yeri, göğü sarsmak üzereyim.
“Uza Zerubabeli, bwanamkubwa wa Yuda, kuti ndidzagwedeza thambo ndi dziko lapansi.
22 Kralların tahtlarını devireceğim, yabancı ulusların gücünü yok edeceğim. Savaş arabalarıyla sürücülerini de devireceğim; atlarla binicileri düşecek, hepsi kardeşinin kılıcıyla öldürülecek.
Ndidzagwetsa mipando yaufumu ndi kuwononga mphamvu za maufumu achilendo. Ndidzagubuduza magaleta ndi okwerapo ake; akavalo ndi okwerapo ake adzagwa, aliyense adzaphedwa ndi lupanga la mʼbale wake.
23 “Her Şeye Egemen RAB ‘O gün seni alacağım, ey Şealtiel'in torunu kulum Zerubbabil’ diyor, ‘Ve seni mühür yüzüğü gibi yapacağım. Çünkü ben seni seçtim.’ Böyle diyor Her Şeye Egemen RAB.”
“‘Tsiku limenelo,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndidzakutenga, iwe mtumiki wanga Zerubabeli mwana wa Sealatieli,’ akutero Yehova, ‘ndipo ndidzakusandutsa kukhala mphete yanga yolamulira, pakuti ndasankha iwe,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

< Hagay 2 >