< Yaratiliş 45 >

1 Yusuf adamlarının önünde kendini tutamayıp, “Herkesi çıkarın buradan!” diye bağırdı. Kendini kardeşlerine tanıttığında yanında kimse olmasın istiyordu.
Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
2 O kadar yüksek sesle ağladı ki, Mısırlılar ağlayışını işitti. Bu haber firavunun ev halkına da ulaştı.
Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
3 Yusuf kardeşlerine, “Ben Yusuf'um!” dedi, “Babam yaşıyor mu?” Kardeşleri donup kaldı, yanıt veremediler.
Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
4 Yusuf, “Lütfen bana yaklaşın” dedi. Onlar yaklaşınca Yusuf şöyle devam etti: “Mısır'a sattığınız kardeşiniz Yusuf benim.
Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
5 Beni buraya sattığınız için üzülmeyin. Kendinizi suçlamayın. Tanrı insanlığı korumak için beni önden gönderdi.
Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
6 Çünkü iki yıldır ülkede kıtlık var, beş yıl daha sürecek. Kimse çift süremeyecek, ekin biçemeyecek.
Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
7 Tanrı yeryüzünde soyunuzu korumak ve harika biçimde canınızı kurtarmak için beni önünüzden gönderdi.
Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
8 Beni buraya gönderen siz değilsiniz, Tanrı'dır. Beni firavunun başdanışmanı, sarayının efendisi, bütün Mısır ülkesinin yöneticisi yaptı.
“Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
9 Hemen babamın yanına gidin, ona oğlun Yusuf şöyle diyor deyin: ‘Tanrı beni Mısır ülkesine yönetici yaptı. Durma, yanıma gel.
Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
10 Goşen bölgesine yerleşirsin; çocukların, torunların, davarların, sığırların ve sahip olduğun her şeyle birlikte yakınımda olursun.
Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
11 Orada sana bakarım, çünkü kıtlık beş yıl daha sürecek. Yoksa sen de ailen ve sana bağlı olan herkes de perişan olursunuz.’
Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
12 “Hepiniz gözlerinizle görüyorsunuz, kardeşim Benyamin, sen de görüyorsun konuşanın gerçekten ben olduğumu.
“Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
13 Mısır'da ne denli güçlü olduğumu ve bütün gördüklerinizi babama anlatın. Babamı hemen buraya getirin.”
Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
14 Sonra kardeşi Benyamin'in boynuna sarılıp ağladı. Benyamin de ağlayarak ona sarıldı.
Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
15 Yusuf ağlayarak bütün kardeşlerini öptü. Sonra kardeşleri onunla konuşmaya başladı.
Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
16 Yusuf'un kardeşlerinin geldiği haberi firavunun sarayına ulaşınca, firavunla görevlileri hoşnut oldu.
Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
17 Firavun Yusuf'a şöyle dedi: “Kardeşlerine de ki, ‘Hayvanlarınızı yükleyip Kenan ülkesine gidin.
Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
18 Babanızı ve ailelerinizi buraya getirin. Size Mısır'ın en iyi topraklarını vereceğim. Ülkenin kaymağını yiyeceksiniz.’
Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
19 Onlara ayrıca şöyle demeni de buyuruyorum: ‘Çocuklarınızla karılarınız için Mısır'dan arabalar alın, babanızla birlikte buraya gelin.
“Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
20 Gözünüz arkada kalmasın, çünkü Mısır'da en iyi ne varsa sizin olacak.’”
Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
21 İsrail'in oğulları söyleneni yaptı. Firavunun buyruğu üzerine Yusuf onlara araba ve yol için azık verdi.
Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
22 Hepsine birer kat yedek giysi, Benyamin'e ise üç yüz parça gümüşle beş kat yedek giysi verdi.
Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
23 Böylece babasına Mısır'da en iyi ne varsa hepsiyle yüklü on eşek, yolculuk için buğday, ekmek ve azık yüklü on dişi eşek gönderdi.
Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
24 Kardeşlerini yolcu ederken onlara, “Yolda kavga etmeyin” dedi.
Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
25 Yusuf'un kardeşleri Mısır'dan ayrılıp Kenan ülkesine, babaları Yakup'un yanına döndüler.
Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
26 Ona, “Yusuf yaşıyor!” dediler, “Üstelik Mısır'ın yöneticisi olmuş.” Babaları donup kaldı, onlara inanmadı.
Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
27 Yusuf'un kendilerine bütün söylediklerini anlattılar. Kendisini Mısır'a götürmek için Yusuf'un gönderdiği arabaları görünce, Yakup'un keyfi yerine geldi.
Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
28 “Tamam!” dedi, “Oğlum Yusuf yaşıyor. Ölmeden önce gidip onu göreceğim.”
Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”

< Yaratiliş 45 >