< Yaratiliş 43 >

1 Kenan ülkesinde kıtlık şiddetlenmişti.
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 Mısır'dan getirilen buğday tükenince Yakup, oğullarına, “Yine gidin, bize biraz yiyecek alın” dedi.
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 Yahuda, “Adam bizi sıkı sıkı uyardı” diye karşılık verdi, “‘Kardeşiniz sizinle birlikte gelmezse, yüzümü göremezsiniz’ dedi.
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 Kardeşimizi bizimle gönderirsen, gider sana yiyecek alırız.
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 Göndermezsen gitmeyiz. Çünkü o adam, ‘Kardeşinizi birlikte getirmezseniz, yüzümü göremezsiniz’ dedi.”
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 İsrail, “Niçin adama bir kardeşiniz daha olduğunu söyleyerek bana bu kötülüğü yaptınız?” dedi.
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 Şöyle yanıtladılar: “Adam, ‘Babanız hâlâ yaşıyor mu? Başka kardeşiniz var mı?’ diye sordu. Bizimle ve akrabalarımızla ilgili öyle sorular sordu ki, yanıt vermek zorunda kaldık. Kardeşinizi getirin diyeceğini nereden bilebilirdik?”
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 Yahuda, babası İsrail'e, “Çocuğu benimle gönder, gidelim” dedi, “Sen de biz de yavrularımız da ölmez, yaşarız.
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 Ona ben kefil oluyorum. Beni sorumlu say. Eğer onu geri getirmez, önüne çıkarmazsam, ömrümce sana karşı suçlu sayılayım.
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 Çünkü gecikmeseydik, şimdiye dek iki kez gidip gelmiş olurduk.”
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 Bunun üzerine İsrail, “Öyleyse gidin” dedi, “Yalnız, torbalarınıza bu ülkenin en iyi ürünlerinden biraz pelesenk, biraz bal, kitre, laden, fıstık, badem koyun, Mısır'ın yöneticisine armağan olarak götürün.
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 Yanınıza iki kat para alın. Torbalarınızın ağzına konan parayı geri götürün. Belki bir yanlışlık olmuştur.
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 Kardeşinizi alıp gidin, o adamın yanına dönün.
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 Her Şeye Gücü Yeten Tanrı, adamın yüreğine size karşı merhamet koysun da, adam öbür kardeşinizle Benyamin'i size geri versin. Bana gelince, çocuklarımdan yoksun kalacaksam kalayım.”
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 Böylece kardeşler yanlarına armağanlar, iki kat para ve Benyamin'i alarak hemen Mısır'a gidip Yusuf'un huzuruna çıktılar.
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 Yusuf Benyamin'i yanlarında görünce, kâhyasına, “Bu adamları eve götür” dedi, “Bir hayvan kesip hazırla. Çünkü öğlen benimle birlikte yemek yiyecekler.”
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 Kâhya Yusuf'un buyurduğu gibi onları Yusuf'un evine götürdü.
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 Ne var ki kardeşleri Yusuf'un evine götürüldükleri için korktular. “İlk gelişimizde torbalarımıza konan para yüzünden götürülüyoruz galiba!” dediler, “Bize saldırıp egemen olmak, bizi köle edip eşeklerimizi almak istiyor.”
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 Yusuf'un kâhyasına yaklaşıp evin kapısında onunla konuştular:
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 “Aman, efendim!” dediler, “Buraya ilk kez yiyecek satın almaya gelmiştik.
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 Konakladığımız yerde torbalarımızı açınca, bir de baktık ki, paramız eksiksiz olarak torbalarımızın ağzına konmuş. Onu size geri getirdik.
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 Ayrıca yeniden yiyecek almak için yanımıza başka para da aldık. Paraları torbalarımıza kimin koyduğunu bilmiyoruz.”
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 Kâhya, “Merak etmeyin” dedi, “Korkmanıza gerek yok. Parayı Tanrınız, babanızın Tanrısı torbalarınıza koydurmuş. Ben paranızı aldım.” Sonra Şimon'u onlara getirdi.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 Kâhya onları Yusuf'un evine götürüp ayaklarını yıkamaları için su getirdi, eşeklerine yem verdi.
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 Kardeşler öğlene, Yusuf'un geleceği saate kadar armağanlarını hazırladılar. Çünkü orada yemek yiyeceklerini duymuşlardı.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 Yusuf eve gelince, getirdikleri armağanları kendisine sunup önünde yere kapandılar.
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 Yusuf hatırlarını sorduktan sonra, “Bana sözünü ettiğiniz yaşlı babanız iyi mi?” dedi, “Hâlâ yaşıyor mu?”
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 Kardeşleri, “Babamız kulun iyi” diye yanıtladılar, “Hâlâ yaşıyor.” Sonra saygıyla eğilip yere kapandılar.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 Yusuf göz gezdirirken kendisiyle aynı anneden olan kardeşi Benyamin'i gördü. “Bana sözünü ettiğiniz küçük kardeşiniz bu mu?” dedi, “Tanrı sana lütfetsin, oğlum.”
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 Sonra hemen oradan ayrıldı, çünkü kardeşini görünce yüreği sızlamıştı. Ağlayacak bir yer aradı. Odasına girip orada ağladı.
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 Yüzünü yıkadıktan sonra dışarı çıktı. Kendisini toparlayarak, “Yemeği getirin” dedi.
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 Yusuf'a ayrı, kardeşlerine ayrı, Yusuf'la yemek yiyen Mısırlılar'a ayrı hizmet edildi. Çünkü Mısırlılar İbraniler'le birlikte yemek yemez, bunu iğrenç sayarlardı.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 Kardeşleri Yusuf'un önünde büyükten küçüğe doğru yaş sırasına göre oturdular. Şaşkın şaşkın birbirlerine baktılar.
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 Yusuf'un masasından onlara yemek dağıtıldı. Benyamin'in payı ötekilerden beş kat fazlaydı. İçtiler, birlikte hoş vakit geçirdiler.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.

< Yaratiliş 43 >