< Yaratiliş 4 >

1 Adem karısı Havva ile yattı. Havva hamile kaldı ve Kayin'i doğurdu. “RAB'bin yardımıyla bir oğul dünyaya getirdim” dedi.
Adamu anagona malo amodzi ndi Hava mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Kaini, ndipo anati, “Ndi thandizo la Yehova ndapeza mwana wamwamuna.”
2 Daha sonra Kayin'in kardeşi Habil'i doğurdu. Habil çoban oldu, Kayin ise çiftçi.
Kenaka anabereka mʼbale wake Abele. Abele anali woweta nkhosa ndipo Kaini anali mlimi.
3 Günler geçti. Bir gün Kayin toprağın ürünlerinden RAB'be sunu getirdi.
Patapita nthawi, Kaini anatenga zipatso za ku munda nakazipereka kwa Yehova monga nsembe.
4 Habil de sürüsünde ilk doğan hayvanlardan bazılarını, özellikle de yağlarını getirdi. RAB Habil'i ve sunusunu kabul etti.
Nayenso Abele anatenga ana ankhosa oyamba kubadwa pamodzi ndi mafuta ake nakazipereka ngati nsembe kwa Yehova. Yehova anakondwera ndi Abele ndi nsembe yake.
5 Kayin'le sunusunu ise reddetti. Kayin çok öfkelendi, suratını astı.
Koma sanakondwere ndi Kaini ndi nsembe yake. Kotero Kaini anakwiya kwambiri ndipo nkhope yake inagwa.
6 RAB Kayin'e, “Niçin öfkelendin?” diye sordu, “Niçin surat astın?
Choncho Yehova anati kwa Kaini, “Chifukwa chiyani wakwiya ndipo bwanji nkhope yako yagwa?
7 Doğru olanı yapsan, seni kabul etmez miyim? Ancak doğru olanı yapmazsan, günah kapıda pusuya yatmış, seni bekliyor. Ona egemen olmalısın.”
Ukanachita zabwino sindikanakulandira kodi? Koma tsopano wachita zoyipa ndipo tchimo likukudikira pa khomo pako, likufuna kukugwira; koma iwe uyenera kugonjetsa tchimolo.”
8 Kayin kardeşi Habil'e, “Haydi, tarlaya gidelim” dedi. Tarlada birlikteyken kardeşine saldırıp onu öldürdü.
Tsiku lina Kaini anati kwa mʼbale wake Abele, “Tiye tipite ku munda.” Ndipo ali ku mundako, Kaini anawukira mʼbale wake namupha.
9 RAB Kayin'e, “Kardeşin Habil nerede?” diye sordu. Kayin, “Bilmiyorum, kardeşimin bekçisi miyim ben?” diye karşılık verdi.
Ndipo Yehova anamufunsa Kaini kuti, “Ali kuti mʼbale wako Abele?” Iye anayankha kuti, “Sindikudziwa. Kodi ine ndine wosunga mʼbale wanga?”
10 RAB, “Ne yaptın?” dedi, “Kardeşinin kanı topraktan bana sesleniyor.
Yehova anati, “Kodi wachita chiyani? Tamvera! Magazi a mʼbale wako akulirira kwa Ine kuchokera mʼnthaka.
11 Artık döktüğün kardeş kanını içmek için ağzını açan toprağın laneti altındasın.
Ndipo tsopano ndiwe wotembereredwa ndipo wachotsedwa mʼdziko limene nthaka yake inatsekula pakamwa pake kulandira magazi a mʼbale wako amene unakhetsa.
12 İşlediğin toprak bundan böyle sana ürün vermeyecek. Yeryüzünde aylak aylak dolaşacaksın.”
Udzalima munda koma nthakayo sidzakupatsanso zokolola zake. Udzakhala wosakhazikika; womangoyendayenda pa dziko lapansi.”
13 Kayin, “Cezam kaldıramayacağım kadar ağır” diye karşılık verdi,
Kaini anati kwa Yehova, “Chilango changa ndi chachikulu kuposera mphamvu zanga.
14 “Bugün beni bu topraklardan kovdun. Artık huzurundan uzak kalacak, yeryüzünde aylak aylak dolaşacağım. Kim bulsa öldürecek beni.”
Lero mukundipirikitsa pa dziko ndi pamaso panu; ndidzakhala wosakhazikika, woyendayenda, ndipo aliyense amene adzandipeze adzandipha.”
15 Bunun üzerine RAB, “Seni kim öldürürse, ondan yedi kez öç alınacak” dedi. Kimse bulup öldürmesin diye Kayin'in üzerine bir nişan koydu.
Koma Yehova anamuwuza kuti, “Sizidzatero ayi; aliyense amene adzaphe Kaini adzalangidwa ndi kulipiritsidwa kasanu ndi kawiri.” Pamenepo Yehova anayika chizindikiro pa Kaini kuti aliyense womupeza asamuphe.
16 Kayin RAB'bin huzurundan ayrıldı. Aden bahçesinin doğusunda, Nod topraklarına yerleşti.
Ndipo Kaini anachoka pamaso pa Yehova nakakhala ku dziko la Nodi, kummawa kwa Edeni.
17 Kayin karısıyla yattı. Karısı hamile kaldı ve Hanok'u doğurdu. Kayin o sırada bir kent kurmaktaydı. Kente oğlu Hanok'un adını verdi.
Kaini anagona malo amodzi ndi mkazi wake ndipo mkaziyo anakhala woyembekezera nabala Enoki. Kaini nthawi imeneyo nʼkuti akumanga mzinda ndipo anawutcha dzina la mwana wake Enoki.
18 Hanok'tan İrat oldu. İrat'tan Mehuyael, Mehuyael'den Metuşael, Metuşael'den Lemek oldu.
Enoki anabereka Iradi; Iradi anabereka Mehuyaeli, ndipo Mehuyaeli anabereka Metusela, ndipo Metusela anabereka Lameki.
19 Lemek iki kadınla evlendi. Birinin adı Âda, öbürünün ise Silla'ydı.
Lameki anakwatira akazi awiri, wina dzina lake linali Ada ndi winayo dzina lake linali Zila.
20 Âda Yaval'ı doğurdu. Yaval sürü sahibi göçebelerin atasıydı.
Ada anabereka Yabala; iyeyu anali kholo la onse okhala mʼmatenti ndi oweta ziweto.
21 Kardeşinin adı Yuval'dı. Yuval lir ve ney çalanların atasıydı.
Dzina la mʼbale wake linali Yubala; iyeyu anali kholo la onse oyimba zeze ndi chitoliro.
22 Silla Tuval-Kayin'i doğurdu. Tuval-Kayin tunç ve demirden çeşitli kesici aletler yapardı. Tuval-Kayin'in kızkardeşi Naama'ydı.
Zila nayenso anali ndi mwana wamwamuna, dzina lake Tubala-Kaini. Iyeyu anali kholo la amisiri onse osula zida za mkuwa ndi chitsulo. Mlongo wake wa Tubala-Kaini anali Naama.
23 Lemek karılarına şöyle dedi: “Ey Âda ve Silla, beni dinleyin, Ey Lemek'in karıları, sözlerime kulak verin. Beni yaraladığı için Bir adam öldürdüm, Beni hırpaladığı için Bir genci öldürdüm.
Lameki anawuza akazi akewo kuti, “Ada ndi Zila, ndimvereni; inu akazi anga imvani mawu anga. Ine ndinapha munthu chifukwa anandipweteka. Ndinapha mnyamatayo chifukwa anandimenya.
24 Kayin'in yedi kez öcü alınacaksa, Lemek'in yetmiş yedi kez öcü alınmalı.”
Ngati wopha Kaini amulipsira kasanu nʼkawiri, ndiye kuti wopha ine Lameki adzamulipsira kokwanira 77.”
25 Adem karısıyla yine yattı. Havva bir erkek çocuk doğurdu. “Tanrı Kayin'in öldürdüğü Habil'in yerine bana başka bir oğul bağışladı” diyerek çocuğa Şit adını verdi.
Adamu anagonanso malo amodzi ndi mkazi wake, ndipo anabereka mwana wamwamuna namutcha Seti, kutanthauza kuti, “Mulungu wandipatsa mwana wina mʼmalo mwa Abele, popeza Kaini anamupha.”
26 Şit'in de bir oğlu oldu, adını Enoş koydu. O zaman insanlar RAB'bi adıyla çağırmaya başladı.
Seti naye anali ndi mwana wa mwamuna, ndipo anamutcha Enosi. Pa nthawi imeneyi anthu anayamba kupemphera mʼdzina la Yehova.

< Yaratiliş 4 >