< Yaratiliş 32 >

1 Yakup yoluna devam ederken, Tanrı'nın melekleriyle karşılaştı.
Nayenso Yakobo analowera njira yake, ndipo angelo a Mulungu anakumana naye.
2 Onları görünce, “Tanrı'nın ordugahı bu” diyerek oraya Mahanayim adını verdi.
Pamene Yakobo anawaona anati, “Ili ndi gulu la Mulungu.” Choncho anawatcha malowo Mahanaimu.
3 Yakup Edom topraklarında, Seir ülkesinde yaşayan ağabeyi Esav'a önceden haberciler gönderdi.
Yakobo anatumiza amithenga ake kwa mʼbale wake Esau ku dera la Seiri, dziko la Edomu.
4 Onlara şu buyruğu verdi: “Efendim Esav'a şöyle deyin: Kulun Yakup diyor ki, ‘Şimdiye kadar Lavan'ın yanında konuk olarak kaldım.
Anawalangiza kuti, “Zimene mukanene ndi izi kwa mbuye wanga Esau: ‘Mtumiki wanu Yakobo akuti, Ine ndakhala ndi kukhala ndi Labani mpaka tsopano.
5 Öküzlere, eşeklere, davarlara, erkek ve kadın kölelere sahip oldum. Efendimi hoşnut etmek için önceden haber gönderiyorum.’”
Ndili ndi ngʼombe, abulu, nkhosa ndi mbuzi, antchito aamuna ndi aakazi. Tsopano ndikutumiza mawu amenewa kwa mbuye wanga, kuti mundikomere mtima.’”
6 Haberciler geri dönüp Yakup'a, “Ağabeyin Esav'ın yanına gittik” dediler, “Dört yüz adamla seni karşılamaya geliyor.”
Pamene amithenga aja anabwerera kwa Yakobo, anati, “Tinapita kwa mʼbale wanu Esau, ndipo tsopano iye akubwera kudzakumana nanu. Ali ndi anthu 400.”
7 Yakup çok korktu, sıkıldı. Yanındaki adamları, davarları, sığırları, develeri iki gruba ayırdı.
Yakobo anali ndi mantha ndi nkhawa yayikulu kwambiri. Tsono anagawa anthu onse amene anali naye, ndiponso nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi ngamira mʼmagulu awiri.
8 “Esav gelir, bir gruba saldırırsa, hiç değilse öteki grup kurtulur” diye düşündü.
Mʼmaganizo ake iye ankanena kuti, “Ngati Esau atabwera ndi kuthira nkhondo gulu limodzi, gulu lina lotsalalo likhoza kupulumuka.”
9 Sonra şöyle dua etti: “Ey atam İbrahim'in, babam İshak'ın Tanrısı RAB! Bana, ‘Ülkene, akrabalarının yanına dön, seni başarılı kılacağım’ diye söz verdin.
Pamenepo Yakobo anapemphera, “Haa, Mulungu wa kholo langa Abrahamu, Mulungu wa abambo anga Isake, Aa Yehova amene munati kwa ine, ‘Bwerera ku dziko la kwanu ndi kwa abale ako, ndipo ndidzakuchitira zabwino.’
10 Bana gösterdiğin bunca iyiliğe, güvene layık değilim. Şeria Irmağı'nı geçtiğimde değneğimden başka bir şeyim yoktu. Şimdi iki orduyla döndüm.
Ine siwoyenera kulandira kukoma mtima kwanu ndi kukhulupirika kwanu kumene mwaonetsa wantchito wanu. Ndinali ndi ndodo yokha pamene ndinawoloka Yorodani uyu koma tsopano ndili ndi magulu awiri.
11 Yalvarırım, beni ağabeyim Esav'dan koru. Gelip bana, çocuklarla annelerine saldırmasından korkuyorum.
Ndipulumutseni mʼdzanja la mʼbale wanga Esau, popeza ndikuopa kuti mwina akubwera kudzandithira nkhondo pamodzi ndi akazi ndi ana omwe.
12 ‘Seni kesinlikle başarılı kılacağım, soyunu denizin kumu gibi sayılamayacak kadar çoğaltacağım’ diye söz vermiştin bana.”
Paja Inu munandilonjeza kuti simudzalephera kundichitira zabwino ndi kuti zidzukulu zanga zidzakhala zosawerengeka ngati mchenga wa ku nyanja.”
13 Yakup geceyi orada geçirdi. Birlikte getirdiği hayvanlardan ağabeyi Esav'a armağan olarak iki yüz keçi, yirmi teke, iki yüz koyun, yirmi koç, yavrularıyla birlikte otuz dişi deve, kırk inek, on boğa, yirmi dişi, on erkek eşek ayırdı.
Iye anagona pomwepo usiku umenewo. Pambuyo pake anasankhula pa chuma chimene anali nacho zinthu izi ngati mphatso za Esau, mʼbale wake:
Anasankhula mbuzi zazikazi 200 ndi atonde makumi awiri, nkhosa zazikazi 200 ndi nkhosa zazimuna makumi awiri,
ngamira za mkaka 30 ndi ana awo, ngʼombe zazikazi 40 ndi zazimuna khumi, ndipo abulu aakazi makumi awiri ndi abulu aamuna khumi.
16 Bunları ayrı sürüler halinde kölelerine teslim ederek, “Önümden gidin, sürüler arasında boşluk bırakın” dedi.
Iye anazipereka kwa antchito ake kuti azikuse, gulu lililonse pa lokha, ndipo anati kwa antchito akewo, “Tsogolani ndipo muonetsetse kuti pali mpata pakati pa gulu ndi gulu linzake.”
17 Birinci köleye buyruk verdi: “Ağabeyim Esav'la karşılaştığında, ‘Sahibin kim, nereye gidiyorsun? Önündeki bu hayvanlar kimin?’ diye sorarsa,
Anawuza mnyamata wa gulu loyamba kuti, “Ngati ukumana naye mʼbale wanga Esau nakufunsa kuti, ‘Ndinu antchito a yani, ndipo mukupita kuti? Nanga ziweto zonse zili patsogolo pakozi ndi za yani?’
18 ‘Kulun Yakup'un’ diyeceksin, ‘Efendisi Esav'a armağan olarak gönderiyor. Kendisi de arkamızdan geliyor.’”
Pamenepo ukayankhe kuti, ‘Zimenezi ndi za wantchito wanu, Yakobo, ndipo wazipereka kwa inu, Esau, mbuye wake ngati mphatso. Mtumiki wanuyu akubwera mʼmbuyo mwathumu.’”
19 İkinci ve üçüncü köleye, sürülerin peşinden giden herkese aynı buyruğu verdi: “Esav'la karşılaştığınızda aynı şeyleri söyleyeceksiniz.
Anawuza mawu omwewo kwa wachiwiri, wachitatu ndi ena onse amene ankayenda motsogoza ziwetozo kuti, “Inunso munene zomwezo kwa Esau mukakumana naye.
20 ‘Kulun Yakup arkamızdan geliyor’ diyeceksiniz.” “Önden göndereceğim armağanla onu yatıştırır, sonra kendisini görürüm. Belki beni bağışlar” diye düşünüyordu.
Muzikanena kuti, ‘Wantchito wanu Yakobo akubwera mʼmbuyo mwathumu.’” Popeza anaganiza kuti, “Ndidzamutsitsa mtima ndi mphatso ndazitsogozazi. Apo tsono ndikadzakumana naye, mwina adzandilandira bwino.”
21 Böylece armağanı önden gönderip geceyi konakladığı yerde geçirdi.
Choncho mphatso za Yakobo zinatsogola, koma iye mwini anagona pa msasa pomwepo usiku umenewo.
22 Yakup o gece kalktı; iki karısını, iki cariyesini, on bir oğlunu yanına alıp Yabbuk Irmağı'nın sığ yerinden karşıya geçti.
Usiku umenewo Yakobo anauka natenga akazi ake awiri, antchito ake awiri ndi ana ake aamuna khumi ndi mmodzi nawoloka pa dooko la mtsinje wa Yaboki.
23 Onları geçirdikten sonra sahip olduğu her şeyi de karşıya geçirdi.
Atatha kuwawolotsa pa mtsinjewo anawolotsanso katundu wake yense.
24 Böylece Yakup arkada yalnız kaldı. Bir adam gün ağarıncaya kadar onunla güreşti.
Tsono Yakobo anatsala yekha. Tsono munthu wina anadzalimbana naye mpaka mʼmbandakucha.
25 Yakup'u yenemeyeceğini anlayınca, onun uyluk kemiğinin başına çarptı. Öyle ki, güreşirken Yakup'un uyluk kemiği çıktı.
Pamene munthuyo anaona kuti sangathe kumugonjetsa, anakhudza nyungʼunyu ya pa ntchafu ya Yakobo ndipo inaguluka polimbanapo.
26 Adam, “Bırak beni, gün ağarıyor” dedi. Yakup, “Beni kutsamadıkça seni bırakmam” diye yanıtladı.
Kenaka munthuyo anati, “Ndisiye ndizipita, popeza kunja kukucha.” Koma Yakobo anayankha, “Sindikulolani kupita pokhapokha mutandidalitsa.”
27 Adam, “Adın ne?” diye sordu. “Yakup.”
Munthu uja anamufunsa Yakobo kuti, “Kodi dzina lako ndiwe yani?” Iye anayankha, “Ndine Yakobo.”
28 Adam, “Artık sana Yakup değil, İsrail denecek” dedi, “Çünkü Tanrı'yla, insanlarla güreşip yendin.”
Pamenepo munthuyo anati, “Dzina lako silidzakhalanso Yakobo koma Israeli, chifukwa walimbana ndi Mulungu ndi anthu ndipo wapambana.”
29 Yakup, “Lütfen adını söyler misin?” diye sordu. Ama adam, “Neden adımı soruyorsun?” dedi. Sonra Yakup'u kutsadı.
Yakobo anati, “Chonde, uzeni dzina lanu.” Koma munthuyo anati, “Chifukwa chiyani ukundifunsa dzina?” Kenaka anamudalitsa pomwepo.
30 Yakup, “Tanrı'yla yüzyüze görüştüm, ama canım bağışlandı” diyerek oraya Peniel adını verdi.
Choncho Yakobo anawatcha malowo Penueli, popeza anati, “Ndinaonana ndi Mulungu maso ndi maso koma sindinafe.”
31 Yakup Peniel'den ayrılırken güneş doğdu. Uyluğundan ötürü aksıyordu.
Dzuwa linamutulukira Yakobo pamene amachoka pa Penueli. Tsono ankayenda chotsimphina chifukwa cha nyungʼunyu yake ija.
32 Bu nedenle İsrailliler bugün bile uyluk kemiğinin üzerindeki siniri yemezler. Çünkü Yakup'un uyluk kemiğinin başındaki sinire çarpılmıştı.
Nʼchifukwa chake mpaka lero Aisraeli sadya nyama ya pa nyungʼunyu chifukwa Yakobo anakhudzidwa pa nyungʼunyu.

< Yaratiliş 32 >