< Galatyalilar 2 >
1 On dört yıl aradan sonra Titus'u da yanıma alıp Barnaba'yla birlikte yine Yeruşalim'e gittim.
Kenaka, patatha zaka khumi ndi zinayi, ndinapitanso ku Yerusalemu, nthawi iyi ndinapita ndi Barnaba. Ndinatenganso Tito kuti apite nafe.
2 Vahiy uyarınca gittim. Boş yere koşmayayım ya da koşmuş olmayayım diye, öteki uluslar arasında yaydığım Müjde'yi özel olarak ileri gelenlere sundum.
Ine ndinapita chifukwa Mulungu anachita kundionetsera kuti ndipite ndipo ndinakakumana ndi atsogoleri mu msonkhano mwamseri ndi kuwafotokozera Uthenga Wabwino umene ndimalalikira pakati pa anthu a mitundu ina. Ndinachita zimenezi kuti ndikhale ndi chitsimikizo kuopa kuti mwina ndinathamanga kapena ndimathamanga liwiro pachabe.
3 Benimle birlikte olan Titus bile Grek olmasına karşın sünnet edilmeye zorlanmadı.
Komatu ngakhale Tito, amene anali nane sanakakamizidwe kuti achite mdulidwe, ngakhale iyeyo anali Mgriki.
4 Ne var ki, İsa Mesih'te sahip olduğumuz özgürlüğü el altından öğrenmek ve böylece bizi köleleştirmek için gizlice aramıza sızan sahte kardeşler vardı.
Nkhani iyi inayambika chifukwa abale ena achinyengo amene analowerera pakati pathu kuti adzaone za ufulu umene tili nawo mwa Khristu Yesu ndikuti atisandutse akapolo.
5 Müjde gerçeği sürekli sizinle kalsın diye bir an bile onlara boyun eğip teslim olmadık.
Ife sitinawagonjere ndi pangʼono pomwe, nʼcholinga chakuti choonadi cha Uthenga Wabwino chikhalebe ndi ife.
6 Ama ileri gelenler –ne oldukları bence önemli değil, Tanrı insanlar arasında ayrım yapmaz– evet, bu ileri gelenler söylediklerime bir şey katmadılar.
Koma kunena za aja ankaoneka ngati ofunika kwambiri, chimene iwo anali sichisintha kanthu kwa ine; chifukwa Mulungu alibe tsankho, iwowo sanawonjezepo kanthu pa uthenga wanga.
7 Tam tersine, Müjde'yi sünnetlilere bildirme işi nasıl Petrus'a verildiyse, sünnetsizlere bildirme işinin de bana verildiğini gördüler.
Makamaka anaona kuti ine ndinapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa anthu a mitundu ina monga momwe Petro anapatsidwa ntchito yolalikira Uthenga Wabwino kwa Ayuda.
8 Çünkü sünnetlilere elçilik etmesi için Petrus'ta etkin olan Tanrı, öteki uluslara elçilik etmem için bende de etkin oldu.
Pakuti Mulungu, amene amagwira ntchito mu utumiki wa Petro monga mtumwi kwa Ayuda, amagwiranso ntchito mu utumiki wanga monga mtumiki kwa anthu a mitundu ina.
9 Topluluğun direkleri sayılan Yakup, Kefas ve Yuhanna bana bağışlanan lütfu sezince paydaşlığımızın işareti olarak bana ve Barnaba'ya sağ ellerini uzattılar. Öteki uluslara bizlerin, Yahudiler'e kendilerinin gitmesini uygun gördüler.
Yakobo, Petro ndi Yohane, amene ankatengedwa ngati mizati, atazindikira chisomo chimene chinapatsidwa kwa ine, anagwirana chanza ndi ine ndi Barnaba kusonyeza chiyanjano chathu. Iwo anavomereza kuti ife tipite kwa anthu a mitundu ina ndipo iwo apite kwa Ayuda.
10 Ancak yoksulları anımsamamızı istediler. Zaten ben de bunu yapmaya gayret ediyordum.
Chimene iwo anapempha ndi chakuti ife tipitirize kukumbukira osauka, chinthu chimene ine ndinali okonzeka kuchichita.
11 Ne var ki, Kefas Antakya'ya geldiği zaman, suçlu olduğu için ona açıkça karşı geldim.
Petro atafika ku Antiokeya, ine ndinamudzudzula pa gulu chifukwa anapezeka wolakwa.
12 Çünkü Yakup'un yanından bazı adamlar gelmeden önce Kefas öteki uluslardan olanlarla birlikte yemek yerdi. Ama o adamlar gelince sünnet yanlılarından korkarak sünnetsizlerden uzaklaştı, onlarla yemek yemez oldu.
Pakuti asanafike anthu otumidwa ndi Yakobo, iye ankadya pamodzi ndi anthu a mitundu ina. Koma atafika, iyeyo anachoka pakati pa anthuwo nakakhala pa yekha chifukwa ankaopa anthu a mʼgulu la mdulidwe.
13 Öbür Yahudiler de onun gibi ikiyüzlülük ettiler. Sonunda Barnaba bile onların ikiyüzlülüğüne kapıldı.
Ayuda enanso anamutsata pochita zachinyengozi, kotero kuti ngakhale Barnaba anasocheretsedwa chifukwa cha chinyengo chawocho.
14 Müjde gerçeğine uygun davranmadıklarını görünce hepsinin önünde Kefas'a şöyle dedim: “Yahudi olduğun halde Yahudi gibi değil, öteki uluslardan biri gibi yaşıyorsun, nasıl olur da ulusları Yahudi gibi yaşamaya zorlarsın?
Koma nditaona kuti iwo sankachita molingana ndi choonadi cha Uthenga Wabwino, ndinawuza Petro pamaso pa anthu onse kuti, “Iwe ndiwe Myuda koma ukukhala ngati munthu wa mtundu wina, osati Myuda. Nanga nʼchifukwa chiyani ukukakamiza anthu a mitundu ina kuti akhale ngati Ayuda?
15 Doğuştan Yahudi olan bizler öteki uluslardan olan ‘günahlılar’ değiliz.
“Ife amene ndife Ayuda mwachibadwa, osati anthu a mitundu ina ochimwa,
16 Yine de insanın Kutsal Yasa'nın gereklerini yaparak değil, İsa Mesih'e iman ederek aklandığını biliyoruz. Bunun için biz de Yasa'nın gereklerini yaparak değil, Mesih'e iman ederek aklanalım diye Mesih İsa'ya iman ettik. Çünkü hiç kimse Yasa'nın gereklerini yaparak aklanmaz.
tikudziwa kuti munthu salungamitsidwa pochita ntchito za lamulo koma ndi chikhulupiriro mwa Yesu Khristu. Chomwecho, ifenso tinakhulupirira Khristu Yesu kuti tilungamitsidwe mwachikhulupiriro mwa Khristu ndipo osati pochita ntchito za lamulo, chifukwa palibe amene adzalungamitsidwa pochita ntchito za lamulo.
17 Mesih'te aklanmak isterken kendimiz günahlı çıkarsak, Mesih günahın yardakçısı mı olur? Kesinlikle hayır!
“Tsono ngati ife, pamene tikufuna kulungamitsidwa mwa Khristu, zikuonekeratu poyera kuti ndifenso ochimwa, kodi zikutanthauza kuti Khristu amalimbikitsa uchimo? Ayi. Nʼkosatheka!
18 Yıktığımı yeniden kurarsam, yasayı çiğnediğimi kanıtlamış olurum.
Ngati ine ndimanganso chimene ndinachigumula, ndikuonetsa kuti ndine wophwanya lamulo.
19 Çünkü ben Tanrı için yaşamak üzere Yasa aracılığıyla Yasa karşısında öldüm.
“Pakuti pamene ndinayesera kutsatira lamulo, lamulolo linandionetsa kuti ndine wochimwa. Choncho ndinasiya kutsatira lamulo kuti ndikhale ndi moyo kwa Mulungu.
20 Mesih'le birlikte çarmıha gerildim. Artık ben yaşamıyorum, Mesih bende yaşıyor. Şimdi bedende sürdürdüğüm yaşamı, beni seven ve benim için kendini feda eden Tanrı Oğlu'na imanla sürdürüyorum.
Ndinapachikidwa pa mtanda pamodzi ndi Khristu, kotero kuti sindinenso amene ndili ndi moyo, koma ndi Khristu amene ali ndi moyo mwa ine. Moyo umene ndili nawo tsopano mʼthupi lino, ndi moyo mwachikhulupiriro mwa Mwana wa Mulungu, amene anandikonda nadzipereka yekha chifukwa cha ine.
21 Tanrı'nın lütfunu geçersiz saymış değilim. Çünkü aklanma Yasa aracılığıyla sağlanabilseydi, o zaman Mesih boş yere ölmüş olurdu.”
Ine sindikukankhira kumbali chisomo cha Mulungu, chifukwa ngati chilungamo chikanapezeka pochita ntchito za lamulo, ndiye kuti Khristu anafa pachabe.”