< Ezra 3 >
1 İsrailliler kendi kentlerine yerleştikten sonra, yedinci ay Yeruşalim'de tek vücut halinde toplandılar.
Utafika mwezi wa chisanu ndi chiwiri Aisraeli atakhala kale mʼmidzi yawo, anthu anasonkhana ku Yerusalemu ndi cholinga chimodzi.
2 Yosadak oğlu Yeşu ve kâhin olan kardeşleri, Şealtiel oğlu Zerubbabil'le kardeşleri İsrail'in Tanrısı'nın sunağını yeniden kurdular. Amaçları, Tanrı adamı Musa'nın yasası uyarınca, sunağın üzerinde yakmalık sunular sunmaktı.
Kenaka Yesuwa mwana wa Yozadaki ndi ansembe anzake pamodzi ndi Zerubabeli mwana wa Sealatieli ndi abale ake anayamba kumanga guwa lansembe la Mulungu wa Israeli. Anatero pofuna kuti aziperekapo nsembe zopsereza monga analembera mʼbuku la Mose, munthu wa Mulungu uja.
3 Çevrelerinde yaşayan halklardan korkmalarına karşın, sunağı eski temeli üzerine yeniden kurdular. Üzerinde RAB'be sabah, akşam öngörülen yakmalık sunuları sundular.
Ndi mantha ndi mantha chifukwa cha anthu a mʼmayikomo, iwo anamanga guwalo pa maziko ake akale, ndipo anapereka nsembe zopsereza kwa Mulungu pa guwapo mmawa ndi madzulo.
4 Sonra yazılanlara uygun biçimde Çardak Bayramı'nı kutladılar. Kural uyarınca, her gün için belirlenen sayıya göre, yakmalık sunuları sundular.
Ankasunga tsiku la chikondwerero cha misasa monga momwe zinalembedwera. Ankaperekanso nsembe za tsiku ndi tsiku monga mwa chiwerengero chake potsata mwambo wake wa tsiku ndi tsiku monga zinalembedwa.
5 Bundan sonra da günlük yakmalık sunuyu, Yeni Ay sunularını, RAB'bin belirlediği bütün kutsal bayramların sunularını ve RAB'be gönülden verilen sunuları sundular.
Pambuyo pake, ankapereka nsembe zopsereza, nsembe zopereka pa nthawi ya mwezi watsopano ndi za pa masiku onse a chikondwerero oyikidwa kutamandira Yehova, kudzanso nsembe zaufulu zopereka kwa Yehova.
6 RAB'bin Tapınağı'nın temeli henüz atılmadığı halde, yedinci ayın birinci günü RAB'be yakmalık sunular sunmaya başladılar.
Kuyambira pa tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, iwo anayambanso kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova, ngakhale kuti maziko a Nyumba ya Yehova anali asanamangidwe.
7 İsrailliler taşçılarla marangozlara para ödediler. Ayrıca sedir tomruklarını Lübnan'dan denize indirerek Yafa'ya getirmeleri için Saydalılar'a ve Surlular'a yiyecek, içecek, zeytinyağı sağladılar. Bütün bunlara Pers Kralı Koreş izin vermişti.
Ndipo anapereka ndalama kwa amisiri a miyala ndi kwa amisiri a matabwa, ndi chakudya, chakumwa ndi mafuta kwa anthu a ku Sidoni ndi a ku Turo, kuti abweretse mitengo ya mkungudza pa nyanja kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Yopa. Zonsezi anachita malinga ndi chilolezo chimene analandira kuchokera kwa Koresi, mfumu ya Peresiya.
8 Tanrı'nın Yeruşalim'deki Tapınağı'na vardıktan sonra, ikinci yılın ikinci ayında Şealtiel oğlu Zerubbabil, Yosadak oğlu Yeşu ve bütün öteki kardeşleri, kâhinler, Levililer ve sürgünden Yeruşalim'e dönenlerin tümü işe başladılar. RAB'bin Tapınağı'nın yapımını denetlemek için yirmi ve daha yukarı yaştaki Levililer'i görevlendirdiler.
Tsono mu chaka chachiwiri atabwera ku Yerusalemu, ku malo akale a Nyumba ya Yehova, mwezi wachiwiri Zerubabeli mwana wa Sealatieli, Yesuwa mwana wa Yozadaki pamodzi ndi abale awo onse, ansembe, Alevi ndi onse amene anabwera ku Yerusalemu kuchokera ku ukapolo, anayamba kugwira ntchito. Iwo anasankha Alevi a zaka zoyambira makumi awiri kuti aziyangʼanira ntchito ya kumanga Nyumba ya Yehova.
9 Levililer'den Yeşu, oğulları ve kardeşleri, Yahuda soyundan Kadmiel ile oğulları, Henadat'ın oğullarıyla torunları Tanrı'nın Tapınağı'nın yapımında çalışanları denetleme işini hep birlikte yüklendiler.
Yesuwa ndi ana ake aamuna kudzanso abale ake, Kadimieli ndi ana ake (ana a Yuda) onse pamodzi anasenza udindo woyangʼanira antchito ku Nyumba ya Mulungu, kuphatikizanso ana a Henadadi komanso Alevi, ana awo ndi abale awo.
10 Yapıcılar RAB'bin Tapınağı'nın temelini atınca, İsrail Kralı Davut'un kuralı uyarınca kâhinler RAB'bi övmek için tören giysilerini giymiş olarak ellerinde borazanlarla, Levili Asafoğulları da zillerle yerlerini aldılar.
Amisiri omanga nyumba atamanga maziko a Nyumba ya Yehova, ansembe anabwera akuyimba malipenga, atavala zovala zaunsembe. Ndipo Alevi, zidzukulu za Asafu, anadza akuyimba matambolini ndi kutenga udindo wawo wotamanda Yehova, potsata malangizo a Davide mfumu ya Aisraeli.
11 RAB'be övgüler, şükranlar sunarak ezgi okudular: “RAB iyidir; İsrail'e sevgisi sonsuzdur.” RAB'bin Tapınağı'nın temeli atıldığı için herkes yüksek sesle RAB'bi övmeye başladı.
Iwo ankayimba motamanda ndi mothokoza Yehova nyimbo iyi: “Yehova ndi wabwino; chikondi chake pa Israeli ndi chamuyaya.” Ndipo anthu onse ankafuwula kwambiri kumutamanda Yehova, chifukwa maziko a Nyumba ya Yehova anali kumangidwa.
12 Eski tapınağı görmüş birçok yaşlı kâhin, Levili ve boy başı tapınağın temelinin atıldığını görünce hıçkıra hıçkıra ağladılar. Birçokları da sevinç çığlıkları attı.
Koma ambiri mwa ansembe, Alevi ndiponso atsogoleri amabanja, akuluakulu amene anaona Nyumba ya Yehova yakale, analira mokweza pamene anaona maziko a nyumbayi akumangidwa. Komanso ena ambiri ankafuwula mosangalala.
13 Sevinç çığlıkları ağlama sesinden ayırt edilemiyordu. Çünkü halk avaz avaz bağırıyordu. Ses uzak yerlerden bile duyuluyordu.
Choncho panalibe amene ankatha kusiyanitsa liwu lofuwula mokondwerera ndi liwu la anthu olira, chifukwa anthuwo ankafuwula kwambiri. Ndipo liwu lofuwulalo limamveka kutali.