< Ezra 10 >

1 Ağlayarak kendini Tanrı'nın Tapınağı'nın önünde yere atan Ezra dua edip günahlarını açıkladı. Bu arada erkek, kadın, çocuk, İsrailliler'den çok büyük bir topluluk Ezra'nın çevresine toplandı. Onlar da hıçkıra hıçkıra ağlıyordu.
Pamene Ezara ankapemphera ndi kuvomereza tchimo lawo, akulira ndipo atadzigwetsa pansi ku Nyumba ya Mulungu, anthu ambiri anabwera kwa iye kudzasonkhana naye. Panali amuna, akazi ndi ana, kuchokera mʼdziko lonse la Israeli ndipo ankalira kwambiri.
2 Elamoğulları'ndan Yehiel oğlu Şekanya, Ezra'ya şöyle dedi: “Çevremizdeki halklardan yabancı karılar aldığımız için Tanrımız'a ihanet ettik. Buna karşın İsrail için hâlâ umut var.
Ndipo Sekaniya, mwana wa Yehieli, wa fuko la Elamu, anawuza Ezara kuti, “Ife takhala osakhulupirika kwa Mulungu wathu ndipo takhala tikukwatira akazi achilendo a mayiko akunowa. Koma ngakhale zili chomwechi, chikhulupiriro chilipobe pakati pa Aisraeli.
3 Senin ve Tanrımız'ın buyrukları karşısında titreyenlerin öğütleri uyarınca, bütün yabancı kadınları ve çocuklarını uzaklaştırmak için Tanrımız'la şimdi bir antlaşma yapalım. Bu antlaşma yasaya uygun olsun.
Tsopano tiyeni tichite naye pangano Mulungu wathu, kuti tichotse akazi onsewa ndi ana awo, potsata malangizo a inu mbuye wanga ndi wa anthu amene amaopa malamulo a Mulungu wathu. Lolani kuti zichitike motsatira malamulo.
4 Haydi kalk! Sorumluluk senin üzerinde. Biz seni destekleyeceğiz. Güçlü ol ve gerekeni yap!”
Tsono dzukani, imeneyi ndi ntchito yanu. Ife tikuthandizani. Limbani mtima ndipo gwirani ntchitoyi.”
5 Bunun üzerine yerden kalkan Ezra önde gelen Levili kâhinlere ve öbür İsrailliler'e söyleneni yapmaları için ant içirdi. Hepsi ant içti.
Choncho Ezara anayimirira ndipo analumbiritsa akulu a ansembe, Alevi ndi Aisraeli onse, kuti adzachitedi monga Sekaniya ananenera. Tsono onse analumbira.
6 Sonra Ezra Tanrı'nın Tapınağı'nın önünden ayrılıp Elyaşiv oğlu Yehohanan'ın odasına gitti. Orada gecelerken ne yemek yedi, ne su içti. Sürgünden dönenler Tanrı'ya bağlı kalmadığı için yas tutuyordu.
Ezara anachoka ku Nyumba ya Mulungu napita ku chipinda cha Yehohanani, mwana wa Eliyasibu. Anatandala kumeneko usiku wonse ndipo sanadye chakudya kapena kumwa madzi popeza ankalira chifukwa cha kusankhulupirika kwa anthu obwera ku ukapolo.
7 Sürgünden dönenlerin hepsinin Yeruşalim'de toplanması için Yahuda ve Yeruşalim'de bir duyuru yapıldı:
Tsono anthu analengeza mʼdziko lonse la Yuda ndi mʼmizinda yonse ya Yerusalemu kwa onse ochokera ku ukapolo aja kuti asonkhane ku Yerusalemu.
8 Halkın önderlerinin ve ileri gelenlerinin kararı uyarınca, üç gün içinde gelmeyenin bütün malına el konulacak, kendisi de sürgünden dönenler topluluğundan atılacaktı.
Ananena kuti wina aliyense amene saonekera pakutha pa masiku atatu, adzalandidwa katundu wake, potsata malangizo a nduna ndi akuluakulu, ndipo adzachotsedwa mʼgulu la anthu obwerako ku ukapolo.
9 Bütün Yahudalı ve Benyaminli erkekler üç gün içinde Yeruşalim'de toplandılar. Dokuzuncu ayın yirminci günü hepsi Tanrı'nın Tapınağı'nın önündeki alandaydı. Hem durumun öneminden, hem de yağmurdan ötürü herkes titriyordu.
Choncho anthu onse a mʼdziko la Yuda ndi a mʼdziko la Benjamini anasonkhana ku Yerusalemu asanathe masiku atatu. Limeneli linali tsiku la 20 la mwezi wa 9. Anthu onse anakhala pansi pa bwalo la Nyumba ya Mulungu akunjenjemera chifukwa cha mvula yambiri imene inagwa.
10 Kâhin Ezra kalkıp, “Siz Tanrı'ya ihanet ettiniz” dedi, “Yabancı kadınlarla evlendiniz. İsrail'in suçuna suç kattınız.
Ndipo wansembe Ezara anayimirira nawuza anthuwo kuti, “Inu mwachimwa pomakwatira akazi achikunja ndi kumawonjezera pa tchimo la Aisraeli.
11 Şimdi atalarınızın Tanrısı RAB'be suçunuzu açıklayın. O'nun istediğini yapın. Çevredeki halklardan ve yabancı karılardan ayrılın.”
Tsopano lapani kwa Yehova, Mulungu wa makolo anu ndi kuchita zimene akufuna. Dzipatuleni kwa anthu a mayiko enawa ndi kwa akazi achikunjawa.”
12 Topluluk yüksek sesle şöyle karşılık verdi: “Bütün söylediklerini yapacağız.
Gulu lonse la anthu linayankha ndi mawu ofuwula kuti, “Nʼzoona! Tichita monga mwaneneramu.
13 Yalnız kalabalık çok, üstelik hava da yağmurlu. Dışarda duracak gücümüz kalmadı. Hem bu bir iki günde çözülecek iş değil. Çünkü bu konuda çok günah işledik.
Koma pano pali anthu ambiri ndiponso mvula ikugwa kwambiri, choncho sitingakayime panja. Ndiponso ntchitoyi si ya tsiku limodzi kapena awiri, chifukwa tachimwa kwambiri pa zimene tachitazi.
14 Bütün topluluk adına önderlerimiz bu konuyla ilgilensin. Sonra kentlerimizde yabancı kadınla evli olan herkes saptanan bir zamanda kentin ileri gelenleri ve yargıçlarıyla birlikte gelsin. Yeter ki, Tanrımız'ın bu konudaki kızgın öfkesi üzerimizden kalksın.”
Tsono mulole kuti atsogoleri athu ayimirire mʼmalo mwa anthu onse. Aliyense wa mʼmizinda yathu amene anakwatira mkazi wachikunja abwere pa nthawi imene inu munene, ndipo abwere pamodzi ndi akuluakulu ndi oweruza a mzindawo. Choncho mkwiyo wa Mulungu wathu udzatichoka.”
15 Ancak, Asahel oğlu Yonatan, Tikva oğlu Yahzeya ve onları destekleyen Meşullam ile Levili Şabbetay buna karşı çıktılar.
Koma Yonatani yekha mwana wa Asaheli ndi Yahazieli mwana wa Tikiva ndiwo anatsutsapo pa zimenezi. Tsono Mesulamu ndi Mlevi Sebetai anawayikira kumbuyo.
16 Sürgünden dönenler bu öneriye göre davrandılar. Kâhin Ezra adlarını belirterek her boydan boy başlarını seçti. Onuncu ayın birinci günü oturup konuyu incelemeye başladılar.
Choncho anthu obwerako ku ukapolo aja anachita zimene zimafunika. Ndipo wansembe Ezara anasankha amuna amene anali atsogoleri a mabanja potsata mafuko awo ndipo onsewo analembedwa mayina awo. Tsiku loyamba la mwezi wa khumi anayambapo kuyifufuza nkhani imeneyi.
17 Birinci ayın birinci günü yabancı kadınlarla evlenen bütün erkeklerin durumunu incelemeyi bitirdiler.
Ndipo pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba anali atathana nawo anthu amene anakwatira akazi achilendo aja.
18 Kâhinlerin soyundan gelip yabancı kadınlarla evlenenler şunlardı: Yosadak oğlu Yeşu'nun oğullarından ve kardeşlerinin soyundan Maaseya, Eliezer, Yariv, Gedalya.
Nawu mʼndandanda wa ansembe amene anakwatira akazi achikunja: Pa banja la Yesuwa ndi abale ake, ana a Yozadaki, panali awa: Maaseiya, Eliezara, Yaribu ndi Gedaliya.
19 Bunlar karılarını kovacaklarına söz verdiler. İşledikleri suç için suç sunusu olarak sürüden bir koç sundular.
Iwo anatsimikiza zochotsa akazi awo ndipo chifukwa cha kulakwa kwawo aliyense anapereka nkhosa yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
20 İmmeroğulları'ndan: Hanani, Zevadya.
Pa banja la Imeri panali awa: Hanani ndi Zebadiya.
21 Harimoğulları'ndan: Maaseya, Eliya, Şemaya, Yehiel, Uzziya.
Pa banja la Harimu panali awa: Maseya, Eliya, Semaya, Yehieli ndi Uziya.
22 Paşhuroğulları'ndan: Elyoenay, Maaseya, İsmail, Netanel, Yozavat, Elasa.
Pa banja la Pasuri panali awa: Eliyoenai, Maseya, Ismaeli, Netaneli, Yozabadi ndi Eleasa.
23 Levililer'den: Yozavat, Şimi, Kelaya –Kelita– Petahya, Yahuda, Eliezer.
Pakati pa Alevi panali: Yozabadi, Simei, Kelaya (ndiye kuti, Kelita). Petaya, Yuda ndi Eliezara.
24 Ezgicilerden: Elyaşiv. Tapınak kapı nöbetçilerinden: Şallum, Telem, Uri.
Pakati pa oyimba nyimbo panali Eliyasibu. Ochokera kwa alonda a zipata: Salumu, Telemu ndi Uri.
25 Öbür İsrailliler'den: Paroşoğulları'ndan: Ramya, Yizziya, Malkiya, Miyamin, Elazar, Malkiya, Benaya.
Ochokera pakati pa Aisraeli ena: a fuko la Parosi anali Ramiya, Iziya, Malikiya, Miyamini, Eliezara, ndi Benaya.
26 Elamoğulları'ndan: Mattanya, Zekeriya, Yehiel, Avdi, Yeremot, Eliya.
A fuko la Elamu anali Mataniya, Zekariya, Yehieli, Abidi, Yeremoti ndi Eliya.
27 Zattuoğulları'ndan: Elyoenay, Elyaşiv, Mattanya, Yeremot, Zavat, Aziza.
A fuko la Zatu anali Eliyoenai, Eliyasibu, Mataniya, Yeremoti, Zabadi ndi Aziza.
28 Bevayoğulları'ndan: Yehohanan, Hananya, Zabbay, Atlay.
A fuko la Bebai anali Yehohanani, Hananiya, Zabayi ndi Atilayi.
29 Banioğulları'ndan: Meşullam, Malluk, Adaya, Yaşuv, Şeal, Yeremot.
A fuko la Bani anali Mesulamu, Maluki, Adaya, Yasubu, Seali ndi Yeremoti.
30 Pahat-Moavoğulları'ndan: Adna, Kelal, Benaya, Maaseya, Mattanya, Besalel, Binnuy, Manaşşe.
A fuko la Pahati-Mowabu anali Adina, Kelali, Benaya, Maseya, Mataniya, Bezaleli, Binuyi ndi Manase.
31 Harimoğulları'ndan: Eliezer, Yişşiya, Malkiya, Şemaya, Şimon,
A fuko la Harimu anali Eliezara, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,
32 Benyamin, Malluk, Şemarya.
Benjamini, Maluki ndi Semariya.
33 Haşumoğulları'ndan: Mattenay, Mattatta, Zavat, Elifelet, Yeremay, Manaşşe, Şimi.
A fuko la Hasumu anali Mataneyi, Matata, Zabadi, Elifeleti, Yeremayi, Manase ndi Simei.
34 Banioğulları'ndan: Maaday, Amram, Uel,
A fuko la Bani anali Madai, Amramu, Uweli,
35 Benaya, Bedeya, Keluhu,
Benaya, Bediya, Keluhi,
36 Vanya, Meremot, Elyaşiv,
Vaniya, Meremoti, Eliyasibu,
37 Mattanya, Mattenay, Yaasay,
Mataniya, Matenayi ndi Yasu.
38 Bani, Binnuy, Şimi,
A fuko la Binuyi anali Simei,
39 Şelemya, Natan, Adaya,
Selemiya, Natani, Adaya,
40 Maknadvay, Şaşay, Şaray,
Makinadebayi, Sasai, Sarai,
41 Azarel, Şelemya, Şemarya,
Azaleli, Selemiya, Semariya,
42 Şallum, Amarya, Yusuf.
Salumu, Amariya ndi Yosefe.
43 Nevooğulları'ndan: Yeiel, Mattitya, Zavat, Zevina, Yadday, Yoel, Benaya.
A fuko la Nebo anali Yeiyeli, Matitiya, Zabadi, Zebina, Yadai, Yoweli ndi Benaya.
44 Bunların hepsi yabancı kadınlarla evlenmişti. Bazılarının bu kadınlardan çocukları da vardı.
Onsewa anakwatira akazi achilendo. Tsono anawasudzula akaziwo ndi kuwatumiza kwawo pamodzi ndi ana awo.

< Ezra 10 >